Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Ad-Duhā   Ayah:

Ad-Duhā

وَٱلضُّحَىٰ
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا سَجَىٰ
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
[452] M’masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo Mtumiki (s.a.w) osamutsikira chivumbulutso. Iye poona izi adali kukaika ndi kudandaula kwakukulu, nao okanira a pa Makka adali kumchita chipongwe. Adali kumunena kuti: “Kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?’’ Basi apa Allah akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha okanira aja kuti: “Sadamusiye ndipo sadakwiye naye.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لَّكَ مِنَ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَسَوۡفَ يُعۡطِيكَ رَبُّكَ فَتَرۡضَىٰٓ
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
[453] Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Allah, ndi zapadziko mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Allah adamchitira mnyengo yochepa modabwitsa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ يَجِدۡكَ يَتِيمٗا فَـَٔاوَىٰ
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَوَجَدَكَ ضَآلّٗا فَهَدَىٰ
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
[454] Mneneri Muhammad (s.a.w) asanapatsidwe uneneri wake ndi Allah anali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira yachiongoko.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَوَجَدَكَ عَآئِلٗا فَأَغۡنَىٰ
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَمَّا ٱلۡيَتِيمَ فَلَا تَقۡهَرۡ
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنۡهَرۡ
Ndiponso wopempha usamukalipire.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَمَّا بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثۡ
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Ad-Duhā
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara