Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Bayyinah   Ayah:

Al-Bayyinah

لَمۡ يَكُنِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ وَٱلۡمُشۡرِكِينَ مُنفَكِّينَ حَتَّىٰ تَأۡتِيَهُمُ ٱلۡبَيِّنَةُ
Amene adakanira (Allah ndi Mthenga Wake) mwa omwe adapatsidwa buku ndi opembedza mafano sadali olekana (ndi umbuli wawo ndi kusalabadira kwawo choona) mpaka pomwe chidawadzera chisonyezo choonekera poyera.[466]
[466] “Akafiri” omwe adapatsidwa buku, ndi Ayuda ndi Akhristu. “Amushirikina” ndi omwe adali kupembedza mafano. Tanthauzo la ma Ayah awa 1- 4 ndikuti asadatulukire Muhammad (s.a.w), Ayuda ndi Akhristu omwe adali ku Madina, pamene adali kuwauza opembedza mafano kuti: “Yayandikira nthawi yotulukira Mneneri. Ife tidzamtsatira, tidzakhala pamodzi ndi iye. Tidzakumenyani nkhondo mpaka kukugonjetsani.” Adali kuyembekezera kuti Mneneriyo adzakhala mwa iwo. Pamene adali kumva izi, opembedza mafano aja, adali odandaula. Iwonso adali kuyembekezera Mneneriyo; limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti: “Sadali olekana mpaka pomwe chidawadzera chisonyezo choonekera poyera.”
Apa ndiye kuti fuko lililonse mwa mafuko atatu aja lidali ndi mtima wopitiriza zipembedzo zawo, osaleka mpaka chiwafikire chisonyezo. Tanthauzo la “chisonyezo,” apa ndi Muhammad (s.a.w) monga Ayah yachiwiri yafotokozera.
Pamene adafika Mneneri, opembedza mafano aja ndiwo adayamba kumukhulupilira, koma Ayuda ndi Akhristu pamene adaona kuti Mneneri sali wochokera mwa iwo monga m’mene adali kuyembekezera adakhumudwa; ena mwa iwo adamkhulupilira pomwe ena sadamkhulupirire. Ili ndilo tanthauzo lakuti, “sadalekane omwe adapatsidwa mabuku mpaka pomwe chidawafikira chisonyezo.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
رَسُولٞ مِّنَ ٱللَّهِ يَتۡلُواْ صُحُفٗا مُّطَهَّرَةٗ
(Yemwe ndi) Mtumiki wochokera kwa Allah akuwawerengera makalata oyeretsedwa (ku zonama).[467]
[467] Tanthauzo la “Makalata oyeretsedwa kuzonama” ndi Qur’an.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فِيهَا كُتُبٞ قَيِّمَةٞ
Omwe mkati mwake muli malamulo oongoka (ofotokoza za choona).[468]
[468] Kapena kuti “mkati mwake muli mabuku olingana,” ndiye kuti m’Qur’an muli zophunzitsa za mabuku onse omwe Allah adavumbulutsa kwa Aneneri onse akale.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا تَفَرَّقَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ إِلَّا مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَةُ
Sadalekane omwe adapatsidwa mabuku mpaka pomwe chidawafikira chisonyezo (chosonyeza kuti Muhammad (s.a.w) ndi mthenga wa Allah yemwe adalonjezedwa mmabuku awo).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَآ أُمِرُوٓاْ إِلَّا لِيَعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مُخۡلِصِينَ لَهُ ٱلدِّينَ حُنَفَآءَ وَيُقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَيُؤۡتُواْ ٱلزَّكَوٰةَۚ وَذَٰلِكَ دِينُ ٱلۡقَيِّمَةِ
Ndipo sadalamulidwe (china) koma kuti ampembedze Allah (Mmodzi yekha) ndikuyeretsa chipembedzo chake popendekera ku choona (ndi kusiya njira zonama) ndi kuti asunge Swala ndiponso apereke chopereka (cha pachuma chawo); chimenecho (ndicho) chipembedzo choongoka.[469]
[469] Tanthauzo lake ndikuti “Mneneri uyu” sadadze ndi chinthu cha chilendo chakuti ndikumukanira. Koma iye akulamula za kupembedza Allah Mmodzi ndi kumuyeretsera chipembedzo Chake; kuima ndi kupemphera, kupereka chopereka ndi zina zotero. Zoterezi ndizonso adali kuphunzitsa aneneri onse omwe adadza ndi zipembedzo zoongoka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ وَٱلۡمُشۡرِكِينَ فِي نَارِ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَآۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمۡ شَرُّ ٱلۡبَرِيَّةِ
Ndithu amene sadakhulupirire (Mneneri) (s.a.w) pakati pa anthu a mabuku ndi opembedza mafano adzalowetsedwa ku Jahannam ndikukhala m’menemo nthawi yaitali; iwowo ndiwo zolengedwa zoipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ أُوْلَٰٓئِكَ هُمۡ خَيۡرُ ٱلۡبَرِيَّةِ
Ndithu amene akhulupirira (mwa Allah ndi Mthenga Wake) ndikumachita zabwino, iwo ndiwo zolengedwa zabwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
جَزَآؤُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ جَنَّٰتُ عَدۡنٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ رَّضِيَ ٱللَّهُ عَنۡهُمۡ وَرَضُواْ عَنۡهُۚ ذَٰلِكَ لِمَنۡ خَشِيَ رَبَّهُۥ
Malipiro awo kwa Mbuye wawo, ndi minda yamuyaya momwe ikuyenda pansi pake mitsinje; adzakhala m’menemo muyaya. Allah adzawayanja nawonso adzamuyanja (chifukwa cha zomwe adzawapatse); zimenezo ndi za yemwe awope Mbuye wake (Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Bayyinah
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara