قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە ناس   ئايەت:

سۈرە ناس

قُلۡ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلنَّاسِ
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye (Mleri) wa anthu (Yemwe akulinganiza zinthu zawo).[503]
[503] Allah pokhala Mlengi wa anthu ndi amenenso amawalera kuyambira pamene ali m’mimba mpaka kumapeto a moyo wawo pano pa dziko. Kuwaleraku kuli muuzimu, mthupi, mu mpweya, ndi pa chilichonse chofunika pa moyo wawo. Kuonjezera pa zimenezi adawapatsa nzeru ndi kuwasonyeza njira zabwino za dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuzitsata njirazo. Adawasonyezanso njira zoipa za dziko lino lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuti azipewe njira zoipazo.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
مَلِكِ ٱلنَّاسِ
Mfumu ya anthu ( Imene iri ndi mphamvu yochita chirichonse pa iwo).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
إِلَٰهِ ٱلنَّاسِ
Wopembedzedwa wa anthu.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
مِن شَرِّ ٱلۡوَسۡوَاسِ ٱلۡخَنَّاسِ
Kuzoipa za mnong’onezi (yemwe amathira unong’onezi wake m’mitimaya anthu) yemwenso amabisala (posiya unong’onezi wake ngati mwini mtimawo atankumbukira Allah).[504]
[504] Mnong’onezi wa zoipa amene amabisala ndiye Satana, yemwe ntchito yake ndi kunong’oneza zoipa m’mitima ya anthu pofuna kuwasokeretsa ndi kuwaiwalitsa Allah. Koma akakumana ndi munthu wa chikhulupiliro cha mphamvu kapena yemwe amatamanda kwambiri Mbuye wake Allah, Satanayo amalephera ndipo amathawa; kubwerera m’mbuyo.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
ٱلَّذِي يُوَسۡوِسُ فِي صُدُورِ ٱلنَّاسِ
Yemwe amanong’oneza mzifuwa za anthu.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
مِنَ ٱلۡجِنَّةِ وَٱلنَّاسِ
Wochokera m’ziwanda ndi mwa anthu.”[505]
[505] Mchiyankhulo cha Chiarabu aliyense woipitsitsa amatchedwa “shaitan” satana, munthu kapena chiwanda. Satana wa muwanthu ndiwoipitsitsa kwambiri kwa anthu kuposa wa m’ziwanda.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە ناس
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش