قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە بەلەد   ئايەت:

سۈرە بەلەد

لَآ أُقۡسِمُ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndikulumbilira mzinda uwu (wa Makka).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَأَنتَ حِلُّۢ بِهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ
Ndipo iwe udzatsikira mu mzindawu mwa ufulu (ndi kuuonjezera ulemelero).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَوَالِدٖ وَمَا وَلَدَ
Ndiponso ndikulumbilira chobereka ndi choberekedwa, (kudzera mwa iwo mtundu wa anthu udasungidwa).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِي كَبَدٍ
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
[439] Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake, chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe kupilira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda chida. Ndipo pamwamba pa izi, Allah wamukakamiza zinthu zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye achita chikulembedwa. Pa tsiku lachimaliziro adzawerengedwa chilichonse chimene adachichita; chachikulu kapena chaching’ono.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّن يَقۡدِرَ عَلَيۡهِ أَحَدٞ
Kodi (munthu wolengedwa ndi mavutoyu) akuganiza kuti palibe amene angamuthe? [440]
[440] Tanthauzo lake apa nkuti munthu akuganiza kuti palibe aliyense amene angamuweruze pa zolakwa zake.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
يَقُولُ أَهۡلَكۡتُ مَالٗا لُّبَدًا
Akunena (monyadira kuti): “Ndaononga chuma chambiri (chifukwa choletsa Chisilamu kufala).”[441]
[441] (Ndime 6-7) Mawu awa akunenedwa kwa okanira omwe adali kupereka chuma chawo pomenyana ndi Usilamu kapena kufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Kenako adali kudzitama chifukwa chopereka chuma chambiri pa njirayo. Izi zikumukhudza aliyense amene akufuna kuti Chisilamu chionongeke. Ndipo iwo amaganiza kuti Allah sakudziwa za maganizo awo oipa.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَيَحۡسَبُ أَن لَّمۡ يَرَهُۥٓ أَحَدٌ
Kodi akuganiza kuti palibe akumuona?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَلَمۡ نَجۡعَل لَّهُۥ عَيۡنَيۡنِ
Kodi sitidampangire maso awiri (amene akuyang’anira)?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَلِسَانٗا وَشَفَتَيۡنِ
Ndilirime ndi milomo iwiri (zimene akulankhulira)?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَهَدَيۡنَٰهُ ٱلنَّجۡدَيۡنِ
Ndipo tamlongosolera njira ziwiri: (yabwino ndi yoipa, ndipo tampatsa mphamvu yosankhira njira imene akufuna).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَلَا ٱقۡتَحَمَ ٱلۡعَقَبَةَ
Kodi walikwera phiri lovutalo (lomwe lingakamfikitse ku Jannah)?[442]
[442] Tanthauzo lake ndikuti bwanji munthu sathokoza chifundo chimenechi (chopatsidwa maso ndi pakamwa) pogwiritsa ntchito chuma chake pa zinthu zabwino zimene Allah wazitchula m’ma Ayah akubwerawa? Ndipo tanthauzo la “kukwera phiri lovuta’’ ndiko kupereka chuma panjira ya Allah chimene chili ndinthu chovuta kwa anthu ambiri ndipo chimafanana ndikukwera phiri losongoka.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡعَقَبَةُ
Nanga nchiyani chakudziwitsa za kukwera phiri lovutalo?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَكُّ رَقَبَةٍ
(Kutero ndiko) kupereka ufulu kwa kapolo,
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَوۡ إِطۡعَٰمٞ فِي يَوۡمٖ ذِي مَسۡغَبَةٖ
Kapena kuwadyetsa (osowa) pa tsiku la njala,
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
يَتِيمٗا ذَا مَقۡرَبَةٍ
Amasiye achibale,
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَوۡ مِسۡكِينٗا ذَا مَتۡرَبَةٖ
Kapena wosauka wa fumbi lokhalokha (chifukwa cha kuvutika kwambiri),
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
ثُمَّ كَانَ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡمَرۡحَمَةِ
Komanso nakhala mmodzi mwa okhulupirira ndikumalangizana za kupirira, ndi kumalangizananso za chifundo.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Otero ndiwo (anthu abwino) a ku dzanja lamanja.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا هُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Koma amene sanakhulupirire Ayah Zathu, ndi anthu a kudzanja lamanzere (oipa).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
عَلَيۡهِمۡ نَارٞ مُّؤۡصَدَةُۢ
Moto wozungulira mbali zonse udzakhala pa iwo (ndikuwatsekera makomo).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە بەلەد
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش