قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە ئەلەق   ئايەت:

سۈرە ئەلەق

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِنۡ عَلَقٍ
Adalenga munthu kuchokera ku magazi owundana.[461]
[461] Madzi ambewu ya munthu, pambuyo pokhazikika mchiberekero kwa masiku makumi anayi, amatembenuka ndikukhala magazi. Ili ndilo tanthauzo la Ayah imeneyi.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
ٱقۡرَأۡ وَرَبُّكَ ٱلۡأَكۡرَمُ
Werenga! Ndipo Mbuye wako ndi Wopereka kwambiri.[462]
[462] Ayah 3 ndi 5 Mtumiki (s.a.w) akuyankhidwa pa kunena kwake kwa kuti: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Choncho Allah akumuuza kuti Iye ndi Mfulu weniweni, ndi Yemwe adawaphunzitsa anthu kulemba ndi cholembera ndi zonse zomwe sadali kuzidziwa. Kwa ufulu Wake wochuluka ndi mphamvu Zake pa chilichonse, sichovuta kwa Iye (Allah) kumphunzitsa Mtumiki Wake kuwerenga molakatula.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
ٱلَّذِي عَلَّمَ بِٱلۡقَلَمِ
Yemwe waphunzitsa (munthu kulemba) ndi cholembera.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
عَلَّمَ ٱلۡإِنسَٰنَ مَا لَمۡ يَعۡلَمۡ
Waphunzitsa munthu zinthu (zambiri) zomwe (iye) sadali kuzidziwa.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
كَلَّآ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَيَطۡغَىٰٓ
Zoona ndithu koma munthu akupyola malire (podzikweza).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَن رَّءَاهُ ٱسۡتَغۡنَىٰٓ
Chifukwa chodziona kuti walemera.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
إِنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلرُّجۡعَىٰٓ
Palibe chikaiko, (iwe Mneneri (s.a.w) kobwerera (onse) nkwa Mbuye wako basi; (adzawaukitsa).[463]
[463] Tanthauzo lake nkuti musanyengedwe ndi chumacho chifukwa chakuti, popanda chikaiko, mubwerera kwa Mbuye wanu ndipo chumacho sichidzakuthandizani chilichonse pa maso Pake.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يَنۡهَىٰ
Kodi wamuona yemwe akuletsa,
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
عَبۡدًا إِذَا صَلَّىٰٓ
Kapolo (wa Allah) akamapemphera?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَرَءَيۡتَ إِن كَانَ عَلَى ٱلۡهُدَىٰٓ
Tandiuza ngati ali pachiongoko?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَوۡ أَمَرَ بِٱلتَّقۡوَىٰٓ
Kapena kuti akulamulira zoopa Allah?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَرَءَيۡتَ إِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰٓ
Tandiuza (za woletsayo) ngati akutsutsa (zimene wadza nazo Mneneri) ndikunyoza (chikhulupiliro ndi ntchito yabwino)?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَلَمۡ يَعۡلَم بِأَنَّ ٱللَّهَ يَرَىٰ
Kodi sakudziwa kuti Allah akuona (machitidwe ake. Ndipo adzamlipira)?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
كَلَّا لَئِن لَّمۡ يَنتَهِ لَنَسۡفَعَۢا بِٱلنَّاصِيَةِ
Ayi ndithu ngati sasiya timukoka tsitsi lapatsumba (tiligwira mwamphamvu tsumba lake ndikukamponya ku Moto).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
نَاصِيَةٖ كَٰذِبَةٍ خَاطِئَةٖ
Tsumba labodza (ndiponso) lamachimo.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَلۡيَدۡعُ نَادِيَهُۥ
Basi aliitane gulu lakelo, (la amene amakhala nawo pabwalo kuti amthandize pano pa dziko kapena tsiku lachimaliziro),
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
سَنَدۡعُ ٱلزَّبَانِيَةَ
Nafe tiitana azabaniya (angelo a ku Moto).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
كَلَّا لَا تُطِعۡهُ وَٱسۡجُدۡۤ وَٱقۡتَرِب۩
Ayi ndithu usamumvere (pa zimene akukuletsazo); koma gwetsa nkhope yako pansi, ndipo dziyandikitse kwa Mbuye wako.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە ئەلەق
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش