قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە زەلزەلە   ئايەت:

سۈرە زەلزەلە

إِذَا زُلۡزِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ زِلۡزَالَهَا
Likadzagwedezedwa dziko lapansi kugwedezeka kwake kwamphamvu,
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَأَخۡرَجَتِ ٱلۡأَرۡضُ أَثۡقَالَهَا
Ndipo nthaka idzatulutsa mitolo yake (zinthu zomwe zidali mkati mwake, monga akufa ndi miyala ya mtengo wapatali),
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَقَالَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا لَهَا
Ndipo munthu adzanena (mwa mantha, ndikudabwa nthawi imeneyo). Ha! Yatani nthaka, (kodi Qiyâma yafika)?
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
يَوۡمَئِذٖ تُحَدِّثُ أَخۡبَارَهَا
Tsiku limenelo idzanena nkhani zake zonse, (zabwino kapena zoipa).[470]
[470] Idzanena nthaka pa tsiku limenelo pamene Allah adzaiuza kuti inene monga momwe amazinenetsera zinthu zimene chikhalire sizilankhula, pakuti Allah ndi Wamphamvu zonse. Kapena m’mene iti idzakhalire nthaka kudzakwanira munthu kudziwa kuti ikutanthauza chakuti, popanda kutulutsa mawu monga momwe timadziwira munthu wosangalala ndi wachisoni; wanjala ndi wokhuta popanda kuyankhula. Nkhani zomwe idzafotokoza nthaka pa tsiku limenelo, monga momwe adanenera Mneneri Muhammad (s.a.w), ndi izi:- Tsiku la chiweruziro nthaka idzamuikira umboni munthu aliyense kapena m’badwo uliwonse pa chimene adachita pamwamba pake (pamwamba pa nthaka). Limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti “ Nthaka idzanena nkhani zake.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
بِأَنَّ رَبَّكَ أَوۡحَىٰ لَهَا
Pakuti Mbuye wako adzailamula kutero (kuti igwedezeke ndikunena zimene zinkachitika pamwamba pake).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
يَوۡمَئِذٖ يَصۡدُرُ ٱلنَّاسُ أَشۡتَاتٗا لِّيُرَوۡاْ أَعۡمَٰلَهُمۡ
Tsiku limenelo anthu adzachoka (m’manda) ali m’magulu obalalika kuti akasonyezedwe ntchito zawo (ndikudziwa chiwerengero chawo chimene chili kwa Allah).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٍ خَيۡرٗا يَرَهُۥ
Choncho, amene angachite chabwino cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake.[471]
[471] (Ndime 7-8) Ma Ayah awiriwa akutidziwitsa kuti munthu adzalipidwa pa chilichonse chimene akuchita, chabwino kapena choipa, ngakhale chikhale chochepa monga kulemera kwa kanjere kochepa kwambiri.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖ شَرّٗا يَرَهُۥ
Ndipo amene angachite choipa cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake. (Allah sachitira chinyengo aliyense).
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: سۈرە زەلزەلە
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش