قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: سورۂ غاشیہ   آیت:

سورۂ غاشیہ

هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡغَٰشِيَةِ
Kodi yakudzera, (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Qiyâma (imene idzaphimba anthu ndi zoopsa zake)?
عربی تفاسیر:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ خَٰشِعَةٌ
Nkhope zina tsiku limenelo, zidzakhala zonyozeka,[425]
[425] Tanthauzo la nkhope apa ndi eni nkhopezo. Amene akunenedwa pamenepa ndi anthu oipa. Allah watchula nkhope chifukwa ndi chiwalo cholemekezeka pa chilengedwe cha munthu ndipo ndi pamene pali chithunzi chake.
عربی تفاسیر:
عَامِلَةٞ نَّاصِبَةٞ
Zogwira ntchito yotopetsa kwambiri.
عربی تفاسیر:
تَصۡلَىٰ نَارًا حَامِيَةٗ
Zikalowa ku Moto wotentha kwambiri.
عربی تفاسیر:
تُسۡقَىٰ مِنۡ عَيۡنٍ ءَانِيَةٖ
Zikamwetsedwa mu kasupe wotentha kwabasi.
عربی تفاسیر:
لَّيۡسَ لَهُمۡ طَعَامٌ إِلَّا مِن ضَرِيعٖ
Sadzakhala ndichakudya koma minga.
عربی تفاسیر:
لَّا يُسۡمِنُ وَلَا يُغۡنِي مِن جُوعٖ
Yosanenepetsa (thupi) ndiponso yosathetsa njala.
عربی تفاسیر:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ نَّاعِمَةٞ
Nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zosangalala.
عربی تفاسیر:
لِّسَعۡيِهَا رَاضِيَةٞ
Zidzakondwera ndi malipiro a zochita zake (za pa dziko lapansi).[426]
[426] Tanthauzo la “kukondweretsedwa ndi zochita zawo’’ ndikuti anthu abwino adzakondwera ndi ntchito zawo zabwino zomwe adazichita pa dziko lapansi akadzakhala ndi malipiro abwino pa tsiku lachimaliziro.
عربی تفاسیر:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’minda ya pamwamba (Jannah).
عربی تفاسیر:
لَّا تَسۡمَعُ فِيهَا لَٰغِيَةٗ
Sizikamva m’menemo mawu oipa, (otukwana ndi kulaula).
عربی تفاسیر:
فِيهَا عَيۡنٞ جَارِيَةٞ
Mmenemo muli kasupe woyenda (mokongola).[427]
[427] (Ndime 12-16) Zosangalatsa zenizeni za tsiku lachimaliziro monga momwe adatiuzira Mneneri (s.a.w) kuti ku Jannah kuli zinthu zimene diso silidapenyepo ngakhale khutu silidamvepo ndipo sizidapitepo m’maganizo a munthu. Choncho zokondweretsa izi zimene Allah watiuza apa akungofanizira ndi zinthu zomwe tikuzidziwa.
عربی تفاسیر:
فِيهَا سُرُرٞ مَّرۡفُوعَةٞ
Mmenemo muli makama a pamwamba,
عربی تفاسیر:
وَأَكۡوَابٞ مَّوۡضُوعَةٞ
Ndi zikho zoikidwa bwino (pamaso pawo),
عربی تفاسیر:
وَنَمَارِقُ مَصۡفُوفَةٞ
Ndi misamiro yoikidwa bwino m’mizeremizere
عربی تفاسیر:
وَزَرَابِيُّ مَبۡثُوثَةٌ
Ndi mphasa (zamtengo wapatali, carpet) zoyalidwa ponseponse.
عربی تفاسیر:
أَفَلَا يَنظُرُونَ إِلَى ٱلۡإِبِلِ كَيۡفَ خُلِقَتۡ
Kodi (akunyozera kulingalira zisonyezo za Allah), sakulingalira kungamira idalengedwa motani?[428]
[428] (Ndime 17-20) Allah akuwauza kuti ayang’ane chilengedwe cha ngamira, thambo, mapiri ndi nthaka. Pambuyo pake alingalire, aone kuti amene adalenga zimenezo ngotha kuchita chilichonse monga kuukitsa anthu m’manda. Cholinga cha Allah potchula zinthu zimenezi, ngakhale kuti malangizowa nga munthu aliyense, koma adali kuwauza akafiri a pa Makka amene zinthu zimenezi maso awo ankaziona nthawi ndi nthawi.
عربی تفاسیر:
وَإِلَى ٱلسَّمَآءِ كَيۡفَ رُفِعَتۡ
Ndi thambo (limene akuliona nthawi zonse) m’mene lidatukulidwira (kutali popanda mzati)?
عربی تفاسیر:
وَإِلَى ٱلۡجِبَالِ كَيۡفَ نُصِبَتۡ
Ndi mapiri momwe adakhazikitsidwira (molimba)?
عربی تفاسیر:
وَإِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَيۡفَ سُطِحَتۡ
Ndi nthaka momwe idayalidwira.
عربی تفاسیر:
فَذَكِّرۡ إِنَّمَآ أَنتَ مُذَكِّرٞ
Basi, kumbutsa (anthu) ndithu iwe, ndiwe mkumbutsi.
عربی تفاسیر:
لَّسۡتَ عَلَيۡهِم بِمُصَيۡطِرٍ
Sindiwe wokakamiza anthu (kuti akhulupirire).[429]
[429] Ayah iyi ikukwana kuwatsutsa adani a Chisilamu amene akunena kuti, “chipembedzo cha Chisilamu chidafala ndi lupanga.” Kutanthauza kuti ankawakakamiza anthu kuti achivomere chipembedzochi. Sichodabwitsa kuona adani a Chisilamu akuchinyoza chipembedzochi, koma chodabwitsa nchakuti mawu onamawa nkumatulukanso mkamwa mwa anthu omwe amadzitcha kuti ndi Asilamu. Nzoona alipo ena mwa anthu odziwa za chipembedzo (ma Ulama) amene adanena kuti chipembedzo cha Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga. Koma simonga momwe akutanthauzilira adani amene sadziwa za Chisilamu nkumangotsatira mabodza a akuluakulu awo. Cholinga cha ma Ulama ponena kuti “Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga” kumeneko ndi kudziteteza kwa adani omwe adafuna kuchithetsa, osati kuwakakamiza anthu kulowa mchipembedzo. Kukakamiza anthu kulowa mChisilamu nkosaloledwa. Amene akudziwa mbiri ya Chisilamu, akudziwa kuti Asilamu sadalamulidwe kuchita Jihâd mpaka pamene akafiri adali kuwazunza. Pali nkhani zambiri za Maswahaba (otsatira Mneneri) (s.a.w) ku Madina pamene adafuna kuwakakamiza ana awo kulowa m’Chisilamu, koma Mneneri adawakaniza kutero. Basi, munthu amene akunena zoterezo mwina akutero pa chifukwa chosadziwa za chipembedzo cha Chisilamu, mwinanso nkukhala misala basi.
عربی تفاسیر:
إِلَّا مَن تَوَلَّىٰ وَكَفَرَ
Koma amene anyoza ndi kukanira (ulaliki wako),
عربی تفاسیر:
فَيُعَذِّبُهُ ٱللَّهُ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَكۡبَرَ
Allah amulanga chilango chachikulu zedi.
عربی تفاسیر:
إِنَّ إِلَيۡنَآ إِيَابَهُمۡ
Ndithu kobwerera kwawo ndi kwa Ife basi.
عربی تفاسیر:
ثُمَّ إِنَّ عَلَيۡنَا حِسَابَهُم
Ndipo ndithu kuwerengedwa kwawo kuli kwa Ife.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: سورۂ غاشیہ
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ - ترجمے کی لسٹ

قرآن کریم کے معانی کا شیشیوا ترجمہ، ترجمہ خالد ابراہیم بيتلا نے کیا ہے۔نسخہ ۲۰۲۰م۔

بند کریں