Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-'Adiyat   Câu:

Chương Al-'Adiyat

وَٱلۡعَٰدِيَٰتِ ضَبۡحٗا
Ndikulumbilira akavalo othamanga ali ndi phuma,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱلۡمُورِيَٰتِ قَدۡحٗا
Ndi otulutsa moto ku zikhotwa (pomenyetsa miyendo m’miyala),
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱلۡمُغِيرَٰتِ صُبۡحٗا
Ndi othira nkhondo adani mmawa (dzuwa lisadatuluke),
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَثَرۡنَ بِهِۦ نَقۡعٗا
Ndi kuulutsa fumbi lambiri (kwa adani) nthawi imeneyo,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَوَسَطۡنَ بِهِۦ جَمۡعًا
Ndikulowelera mkatikati mwa adani.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لِرَبِّهِۦ لَكَنُودٞ
Ndithu munthu ali wokanira Mbuye wake, (sathokoza Allah pa zimene amdalitsa nazo).[472]
[472] Tanthauzo la “kukanira Mbuye wake” ndi kuukanira mtendere Wake. Ndipo kukanira mtendere ndiko kusagwiritsira ntchito mtenderewo mnjira zabwino, monga m’mapemphero ndi zina zotero.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّهُۥ عَلَىٰ ذَٰلِكَ لَشَهِيدٞ
Ndithudi iye pa zimenezi ndi mboni (yodzichitira yekha kupyolera mzochitachita zake).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّهُۥ لِحُبِّ ٱلۡخَيۡرِ لَشَدِيدٌ
Ndipo ndithu iye ndiwokonda chuma kwambiri (ndiponso ngwamsulizo).[473]
[473] Kapena kuti ali wofunitsitsa chuma kwambiri; kumeneko ndikumangoti mtima dyokodyoko pachuma. Ukachipeza ndikumachichitira umbombo ndipo ndikumaganiza kuti chumacho nchopambana china chilichonse.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ أَفَلَا يَعۡلَمُ إِذَا بُعۡثِرَ مَا فِي ٱلۡقُبُورِ
Kodi sakudziwa zikadzatulutsidwa za m’manda,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَحُصِّلَ مَا فِي ٱلصُّدُورِ
Ndikudzasonkhanitsidwa ndi kuonekera poyera zomwe zidali m’mitima?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ رَبَّهُم بِهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّخَبِيرُۢ
Ndithu tsiku limenelo Mbuye wawo adzawadziwa kwambiri (ndikuwalongosolera zonse zochita zawo).[474]
[474] “Kuwadziwa kwambiri,” kukutanthauza kuti Iye ngodziwa zazikuluzikulu ndi zazing’onozing’ono zoonekera poyera ndi zobisika. Tsiku limenelo adzawalipira chilichonse chimene adachita.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-'Adiyat
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại