Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Ibrahim   Câu:

Chương Ibrahim

الٓرۚ كِتَٰبٌ أَنزَلۡنَٰهُ إِلَيۡكَ لِتُخۡرِجَ ٱلنَّاسَ مِنَ ٱلظُّلُمَٰتِ إِلَى ٱلنُّورِ بِإِذۡنِ رَبِّهِمۡ إِلَىٰ صِرَٰطِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَمِيدِ
Alif-Lâm-Ra. (Ili ndi) buku lomwe talivumbulutsa kwa iwe kuti uwatulutse anthu mu mdima ndi kuwaika mkuunika - mwalamulo la Mbuye wawo - uwapititse kunjira ya Mwini mphamvu zoposa, Woyamikidwa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱللَّهِ ٱلَّذِي لَهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ وَوَيۡلٞ لِّلۡكَٰفِرِينَ مِنۡ عَذَابٖ شَدِيدٍ
Allah, Yemwe ndi Zake zonse zakumwamba ndi pansi. Ndipo kuonongeka ndi chilango chokhwima kudzatsimikizika pa osakhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِينَ يَسۡتَحِبُّونَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا عَلَى ٱلۡأٓخِرَةِ وَيَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ وَيَبۡغُونَهَا عِوَجًاۚ أُوْلَٰٓئِكَ فِي ضَلَٰلِۭ بَعِيدٖ
Amene akukondetsa moyo wadziko lapansi kuposa moyo wa pambuyo pa imfa, ndipo amatsekereza (anthu) ku njira ya Allah ndikufuna kuikhotetsa (pomwe njirayo njosakhota). Iwo ali mkusokera kotalikana kwambiri (ndi choonadi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا مِن رَّسُولٍ إِلَّا بِلِسَانِ قَوۡمِهِۦ لِيُبَيِّنَ لَهُمۡۖ فَيُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
Ndipo sitidamtume mtumiki aliyense koma ndi chiyankhulo cha anthu ake kuti awafotokozere. Kenako Allah akumsiya kusokera amene wamfuna (chifukwa mwini wake safuna kuongoka). Ndipo amamuongolera yemwe wamfuna, ndipo Iye Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا مُوسَىٰ بِـَٔايَٰتِنَآ أَنۡ أَخۡرِجۡ قَوۡمَكَ مِنَ ٱلظُّلُمَٰتِ إِلَى ٱلنُّورِ وَذَكِّرۡهُم بِأَيَّىٰمِ ٱللَّهِۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَٰتٖ لِّكُلِّ صَبَّارٖ شَكُورٖ
Ndipo ndithu tidamtumiza Mûsa ndi zozizwitsa Zathu (tidamuuza): “Achotse anthu ako mu mdima (wa umbuli) ndi kuwaika mkuunika (kwa chikhulupiliro) ndipo uwakumbutse masiku a Allah (a masautso).” Ndithu m’zimenezo muli zizindikiro kwa yense wopirira, wothokoza.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذۡ قَالَ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَةَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ إِذۡ أَنجَىٰكُم مِّنۡ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ يَسُومُونَكُمۡ سُوٓءَ ٱلۡعَذَابِ وَيُذَبِّحُونَ أَبۡنَآءَكُمۡ وَيَسۡتَحۡيُونَ نِسَآءَكُمۡۚ وَفِي ذَٰلِكُم بَلَآءٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَظِيمٞ
Ndipo (akumbutse anthu ako) pamene Mûsa adauza anthu ake: “Kumbukirani mtendere wa Allah umene uli pa inu pamene adakupulumutsani kwa anthu a Farawo, omwe adakuzunzani ndi chilango choipa. Ankazinga (kupha) ana anu aamuna ndi kuwasiya amoyo ana anu aakazi; ndithu m’zimenezi mudali mayeso aakulu ochokera kwa Mbuye wanu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذۡ تَأَذَّنَ رَبُّكُمۡ لَئِن شَكَرۡتُمۡ لَأَزِيدَنَّكُمۡۖ وَلَئِن كَفَرۡتُمۡ إِنَّ عَذَابِي لَشَدِيدٞ
Ndipo (kumbukani) pamene Mbuye wanu adalengeza kuti: “Ngati muthokoza, ndikuonjezerani; ndipo ngati simuthokoza (dziwani kuti) chilango changa nchaukali.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقَالَ مُوسَىٰٓ إِن تَكۡفُرُوٓاْ أَنتُمۡ وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا فَإِنَّ ٱللَّهَ لَغَنِيٌّ حَمِيدٌ
Ndipo Mûsa adati (kwa anthu ake): “Ngati inu mukana (pakusiya kuthokoza) pamodzi ndi onse a m’dziko, (Allah salabadira chilichonse pa zimenezo), ndithudi Allah Ngwachikwanekwane; Ngotamandidwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ يَأۡتِكُمۡ نَبَؤُاْ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ قَوۡمِ نُوحٖ وَعَادٖ وَثَمُودَ وَٱلَّذِينَ مِنۢ بَعۡدِهِمۡ لَا يَعۡلَمُهُمۡ إِلَّا ٱللَّهُۚ جَآءَتۡهُمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ فَرَدُّوٓاْ أَيۡدِيَهُمۡ فِيٓ أَفۡوَٰهِهِمۡ وَقَالُوٓاْ إِنَّا كَفَرۡنَا بِمَآ أُرۡسِلۡتُم بِهِۦ وَإِنَّا لَفِي شَكّٖ مِّمَّا تَدۡعُونَنَآ إِلَيۡهِ مُرِيبٖ
Kodi siidakudzereni nkhani ya omwe adalipo patsogolo panu? Anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu? Ndi omwe adadza pambuyo pawo? Omwe palibe akuwadziwa kupatula Allah. Atumiki awo adawadzera ndi umboni oonekera. Koma adabwezera manja awo kukamwa kwawo (kusonyeza kutsutsa), ndipo adati: “Ndithu ife tikuzikana zimene mwatumizidwa nazo, ndipo ife tili mchikaiko pa zimene mukuitanira, ndiponso mchipeneko.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ قَالَتۡ رُسُلُهُمۡ أَفِي ٱللَّهِ شَكّٞ فَاطِرِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ يَدۡعُوكُمۡ لِيَغۡفِرَ لَكُم مِّن ذُنُوبِكُمۡ وَيُؤَخِّرَكُمۡ إِلَىٰٓ أَجَلٖ مُّسَمّٗىۚ قَالُوٓاْ إِنۡ أَنتُمۡ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا تُرِيدُونَ أَن تَصُدُّونَا عَمَّا كَانَ يَعۡبُدُ ءَابَآؤُنَا فَأۡتُونَا بِسُلۡطَٰنٖ مُّبِينٖ
Atumiki awo adati: “Kodi mwa Allah, Mlengi wa thambo ndi nthaka muli chikaiko? Iye akukuitanani kuti akukhululukireni machimo anu, ndi kuti (mukakhulupirira) akupatseni nthawi (pokutalikitsirani moyo wanu) kufikira pa nthawi yoyikidwa.” Adati: “Inu sikanthu kena koma ndinu anthu ngati ife. Mungofuna kutitsekereza ku zimene ankazipembedza makolo athu; choncho tibweretsereni umboni woonekera.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَتۡ لَهُمۡ رُسُلُهُمۡ إِن نَّحۡنُ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُكُمۡ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ يَمُنُّ عَلَىٰ مَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦۖ وَمَا كَانَ لَنَآ أَن نَّأۡتِيَكُم بِسُلۡطَٰنٍ إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ
Atumiki awo adati kwa iwo: “(Zoonadi), ife ndife anthu ngati inu, koma Allah amamchitira zabwino yemwe wamfuna mwa akapolo ake. Ndipo ife tilibe nyonga zokubweretserani chisonyezo koma mwachilolezo cha Allah. Ndipo kwa Allah yekha atsamire okhulupirira onse.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا لَنَآ أَلَّا نَتَوَكَّلَ عَلَى ٱللَّهِ وَقَدۡ هَدَىٰنَا سُبُلَنَاۚ وَلَنَصۡبِرَنَّ عَلَىٰ مَآ ءَاذَيۡتُمُونَاۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُتَوَكِّلُونَ
“Nanga kwa ife kuli chiyani kuti tisatsamire kwa Allah pomwe watisonyeza njira zathu. Ndipo tipirira pa zimene mukutisautsa nazo. Choncho, kwa Allah Yekha atsamire otsamira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لِرُسُلِهِمۡ لَنُخۡرِجَنَّكُم مِّنۡ أَرۡضِنَآ أَوۡ لَتَعُودُنَّ فِي مِلَّتِنَاۖ فَأَوۡحَىٰٓ إِلَيۡهِمۡ رَبُّهُمۡ لَنُهۡلِكَنَّ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo amene sadakhulupirire, adanena kwa atumiki awo: “Ndithu tikutulutsani m’dziko lathu, pokhapokha mubwelere m’chipembedzo chathu.” Koma Mbuye wawo (Allah) adawavumbulutsira uthenga (wakuti): “Ndithu tiwaononga ochita zoipa (osakhulupirira).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَنُسۡكِنَنَّكُمُ ٱلۡأَرۡضَ مِنۢ بَعۡدِهِمۡۚ ذَٰلِكَ لِمَنۡ خَافَ مَقَامِي وَخَافَ وَعِيدِ
“Ndipo tikukhazikani (inu) pambuyo pawo m’dzikomo. Apeza zimenezi omwe aopa kuimilira pamaso pa Ine, ndi kuopa chilango Chnga.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱسۡتَفۡتَحُواْ وَخَابَ كُلُّ جَبَّارٍ عَنِيدٖ
Ndipo (atumikio) adapempha chithandizo (kwa Allah), ndipo adaonongeka aliyense wodzikuza, wamakani.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مِّن وَرَآئِهِۦ جَهَنَّمُ وَيُسۡقَىٰ مِن مَّآءٖ صَدِيدٖ
(Yemwe) kutsogolo kwake Jahannam ikumdikira, ndipo (kumeneko) adzamumwetsa madzi amafinya (otuluka m’matupi a anthu a ku Moto).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَتَجَرَّعُهُۥ وَلَا يَكَادُ يُسِيغُهُۥ وَيَأۡتِيهِ ٱلۡمَوۡتُ مِن كُلِّ مَكَانٖ وَمَا هُوَ بِمَيِّتٖۖ وَمِن وَرَآئِهِۦ عَذَابٌ غَلِيظٞ
Adzakhala akumwa koma movutikira ndipo ululu wa imfa udzamdzera mbali zonse koma sadzafa; ndipo kuonjezera apo, pali chilango (china) chaukali.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مَّثَلُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِرَبِّهِمۡۖ أَعۡمَٰلُهُمۡ كَرَمَادٍ ٱشۡتَدَّتۡ بِهِ ٱلرِّيحُ فِي يَوۡمٍ عَاصِفٖۖ لَّا يَقۡدِرُونَ مِمَّا كَسَبُواْ عَلَىٰ شَيۡءٖۚ ذَٰلِكَ هُوَ ٱلضَّلَٰلُ ٱلۡبَعِيدُ
Fanizo la amene sadakhulupirire Mbuye wawo, zochita zawo (zabwino zomwe sadzalipidwa nazo chabwino chilichonse chifukwa chakuti sadazichite pofuna kukondweretsa Allah) zili ngati phulusa lomwe likuulutsidwa ndi mphepo ya mkuntho; ndipo sadzatha kupindula chilichonse pa zimene adachita, uko ndikutaika konka nako kutali (ndi choonadi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ بِٱلۡحَقِّۚ إِن يَشَأۡ يُذۡهِبۡكُمۡ وَيَأۡتِ بِخَلۡقٖ جَدِيدٖ
Kodi siuona kuti Allah adalenga thambo ndi nthaka mwachoonadi? Ndipo atafuna angakuchotseni (nthawi imodzi) ndikubweretsa zolengedwa zina zatsopano.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ بِعَزِيزٖ
Ndipo zimenezo kwa Allah sizovuta.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَبَرَزُواْ لِلَّهِ جَمِيعٗا فَقَالَ ٱلضُّعَفَٰٓؤُاْ لِلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُوٓاْ إِنَّا كُنَّا لَكُمۡ تَبَعٗا فَهَلۡ أَنتُم مُّغۡنُونَ عَنَّا مِنۡ عَذَابِ ٱللَّهِ مِن شَيۡءٖۚ قَالُواْ لَوۡ هَدَىٰنَا ٱللَّهُ لَهَدَيۡنَٰكُمۡۖ سَوَآءٌ عَلَيۡنَآ أَجَزِعۡنَآ أَمۡ صَبَرۡنَا مَا لَنَا مِن مَّحِيصٖ
Ndipo onse (adzatuluka m’manda mwawo ndiponso) akaonekera kwa Allah (kuti awalipire). Pamenepo ofooka (omwe adasokera chifukwa chotsatira atsogoleri awo) adzanena kwa omwe ankadzikuza: “Ndithu ife tidali kukutsatirani inu; kodi inu simungathe kutichotsera kanthu kochepa m’chilango cha Allah chi?” (Atsogoleri) adzati: “Allah akadationgolera, tikadakuongolerani; (koma tsopano) ndi chimodzimodzi kwa ife titekeseke ndi chilangochi, kapena tipirire nacho; tilibe pothawira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقَالَ ٱلشَّيۡطَٰنُ لَمَّا قُضِيَ ٱلۡأَمۡرُ إِنَّ ٱللَّهَ وَعَدَكُمۡ وَعۡدَ ٱلۡحَقِّ وَوَعَدتُّكُمۡ فَأَخۡلَفۡتُكُمۡۖ وَمَا كَانَ لِيَ عَلَيۡكُم مِّن سُلۡطَٰنٍ إِلَّآ أَن دَعَوۡتُكُمۡ فَٱسۡتَجَبۡتُمۡ لِيۖ فَلَا تَلُومُونِي وَلُومُوٓاْ أَنفُسَكُمۖ مَّآ أَنَا۠ بِمُصۡرِخِكُمۡ وَمَآ أَنتُم بِمُصۡرِخِيَّ إِنِّي كَفَرۡتُ بِمَآ أَشۡرَكۡتُمُونِ مِن قَبۡلُۗ إِنَّ ٱلظَّٰلِمِينَ لَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo satana adzanena chiweruzo chikadzalamulidwa (oipa kulowa ku Moto, abwino kulowa ku Munda wamtendere): “Ndithu Allah adakulonjezani lonjezo loona (ndipo wakwaniritsa). Nane ndidakulonjezani, koma sindidakukwaniritsireni. Ndidalibe mphamvu pa inu (yokukakamizirani kunditsata) koma ndimangokuitanani basi, ndipo munkandiyankha. Choncho musandidzudzule, koma dzidzudzuleni nokha. Sindingathe kukuthangatani ndiponso inu simungathe kundithangata. Ndithu ine ndidakukana kundiphatikiza kwanu ndi Allah kale. Ndithu ochita zoipa adzapeza chilango chowawa.”[242]
[242] Omasulira Qur’an adati: Chiweruzo chikadzaweruzidwa, anthu abwino nkukakhazikika ku Munda wa mtendere pomwe anthu oipa nkukalowa ku Moto, anthu a ku Moto adzayamba kumadzudzula satana ndi kumnyoza. Ndipo satana adzaimilira pakati pawo pagome la Moto m’katikati mwa Jahannam nadzanena kwa anthu onse a ku Moto kuti: “Musandidzudzule, koma dzudzulani mitima yanu. Mitima yanu ndiyomwe idakuonongani. Ine ndinkangokuitanani chabe, sindidakukakamizeni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأُدۡخِلَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَا بِإِذۡنِ رَبِّهِمۡۖ تَحِيَّتُهُمۡ فِيهَا سَلَٰمٌ
Ndipo amene adakhulupirira ndi kuchita zabwino, adzalowetsedwa ku Minda yomwe pansi (ndi patsogolo) pake mitsinje ikuyenda, adzakhala m’menemo nthawi yaitali mwachilolezo cha Mbuye wawo. Kulonjerana kwawo m’menemo kudzakhala: “Mtendere!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ تَرَ كَيۡفَ ضَرَبَ ٱللَّهُ مَثَلٗا كَلِمَةٗ طَيِّبَةٗ كَشَجَرَةٖ طَيِّبَةٍ أَصۡلُهَا ثَابِتٞ وَفَرۡعُهَا فِي ٱلسَّمَآءِ
Kodi suona momwe Allah waponyera fanizo (la liwu labwino)? Liwu labwino lili ngati mtengo wabwino (umene) mizu yake njolimba, ndipo nthambi zake zanka kumwamba.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
تُؤۡتِيٓ أُكُلَهَا كُلَّ حِينِۭ بِإِذۡنِ رَبِّهَاۗ وَيَضۡرِبُ ٱللَّهُ ٱلۡأَمۡثَالَ لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَذَكَّرُونَ
Umapereka zipatso zake nthawi iliyonse mwachifuniro cha Mbuye wake. (Umo ndi momwe liwu labwino lilili, limabwera ndi zabwino). Ndipo Allah amaponyera anthu mafanizo kuti akumbukire.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَثَلُ كَلِمَةٍ خَبِيثَةٖ كَشَجَرَةٍ خَبِيثَةٍ ٱجۡتُثَّتۡ مِن فَوۡقِ ٱلۡأَرۡضِ مَا لَهَا مِن قَرَارٖ
Tsono fanizo la liwu loipa, lili ngati mtengo woipa, umene wazulidwa m’nthaka omwe uli osakhazikika.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يُثَبِّتُ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ بِٱلۡقَوۡلِ ٱلثَّابِتِ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَفِي ٱلۡأٓخِرَةِۖ وَيُضِلُّ ٱللَّهُ ٱلظَّٰلِمِينَۚ وَيَفۡعَلُ ٱللَّهُ مَا يَشَآءُ
Allah amawalimbikitsa amene akhulupirira ndi mawu olimba m’moyo wa dziko lapansi, ndi moyo wapambuyo pa imfa; ndipo Allah amawalekelera kusokera omwe akudzichitira okha zoipa; ndipo Allah amachita zimene wafuna.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ بَدَّلُواْ نِعۡمَتَ ٱللَّهِ كُفۡرٗا وَأَحَلُّواْ قَوۡمَهُمۡ دَارَ ٱلۡبَوَارِ
Kodi sudawaone omwe asintha mtendere wa Allah moukana ndikuwafikitsa anthu awo (omwe adawatsata m’zoipa) kunyumba ya chionongeko?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
جَهَنَّمَ يَصۡلَوۡنَهَاۖ وَبِئۡسَ ٱلۡقَرَارُ
(Yomwe ndi) Jahannam; adzailowa; taonani kuipa malo okhazikikapo!
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَعَلُواْ لِلَّهِ أَندَادٗا لِّيُضِلُّواْ عَن سَبِيلِهِۦۗ قُلۡ تَمَتَّعُواْ فَإِنَّ مَصِيرَكُمۡ إِلَى ٱلنَّارِ
Ndipo ampangira Allah anzake kuti asokeretse (anthu) kunjira Yake! Nena: “Sangalalani pang’ono chabe! Ndithu kobwerera kwanu nkuMoto!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قُل لِّعِبَادِيَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يُقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَيُنفِقُواْ مِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ سِرّٗا وَعَلَانِيَةٗ مِّن قَبۡلِ أَن يَأۡتِيَ يَوۡمٞ لَّا بَيۡعٞ فِيهِ وَلَا خِلَٰلٌ
Auze akapolo Anga amene akhulupirira kuti apemphere Swala ndikupereka zina mwa zomwe tawapatsa, mobisa ndi moonekera lisanawafike tsiku lopanda (chithandizo cha) kudziombola ndi (chithandizo cha) ubwenzi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱللَّهُ ٱلَّذِي خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ وَأَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَخۡرَجَ بِهِۦ مِنَ ٱلثَّمَرَٰتِ رِزۡقٗا لَّكُمۡۖ وَسَخَّرَ لَكُمُ ٱلۡفُلۡكَ لِتَجۡرِيَ فِي ٱلۡبَحۡرِ بِأَمۡرِهِۦۖ وَسَخَّرَ لَكُمُ ٱلۡأَنۡهَٰرَ
Allah ndi Yemwe adalenga thambo ndi nthaka, ndipo adatsitsa madzi ku mitambo, ndi madziwo adatulutsa zipatso kuti zikhale Rizq lanu (chakudya chanu). Ndipo adakufewetserani zombo kuti ziziyenda pa nyanja mwa lamulo Lake; ndiponso adakufewetserani mitsinje.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَسَخَّرَ لَكُمُ ٱلشَّمۡسَ وَٱلۡقَمَرَ دَآئِبَيۡنِۖ وَسَخَّرَ لَكُمُ ٱلَّيۡلَ وَٱلنَّهَارَ
Adakufewetseraninso dzuwa ndi mwezi, mopitilira (nthawi zonse). Ndiponso adakufewetserani usiku ndi usana.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَءَاتَىٰكُم مِّن كُلِّ مَا سَأَلۡتُمُوهُۚ وَإِن تَعُدُّواْ نِعۡمَتَ ٱللَّهِ لَا تُحۡصُوهَآۗ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَظَلُومٞ كَفَّارٞ
Ndipo wakupatsani mu zonse zomwe mwampempha (ndi zimene simudam’pemphe). Ngati mutayesa kuwerenga madalitso a Allah, simungathe kuwawerenga. Ndithu munthu ngwachinyengo chachikulu, ngosathokoza.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِيمُ رَبِّ ٱجۡعَلۡ هَٰذَا ٱلۡبَلَدَ ءَامِنٗا وَٱجۡنُبۡنِي وَبَنِيَّ أَن نَّعۡبُدَ ٱلۡأَصۡنَامَ
Ndipo (kumbukani) pamene Ibrahim adanena: “Mbuye wanga! Uchiteni mzinda uwu (wa Makka) kukhala wa mtendere; ndipo ndipatuleni ine ndi ana anga ku machitidwe opembedza mafano.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبِّ إِنَّهُنَّ أَضۡلَلۡنَ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلنَّاسِۖ فَمَن تَبِعَنِي فَإِنَّهُۥ مِنِّيۖ وَمَنۡ عَصَانِي فَإِنَّكَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
“Mbuye wanga! Ndithu (mafano) awa asokeretsa anthu ambiri. Choncho amene wanditsata, ndithu iyeyo ali mwa ine (mudzamulipira chabwino monga mwandilonjeza), ndipo amene wandinyoza (mutha kumukhululukira) ndithu Inu Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَّبَّنَآ إِنِّيٓ أَسۡكَنتُ مِن ذُرِّيَّتِي بِوَادٍ غَيۡرِ ذِي زَرۡعٍ عِندَ بَيۡتِكَ ٱلۡمُحَرَّمِ رَبَّنَا لِيُقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ فَٱجۡعَلۡ أَفۡـِٔدَةٗ مِّنَ ٱلنَّاسِ تَهۡوِيٓ إِلَيۡهِمۡ وَٱرۡزُقۡهُم مِّنَ ٱلثَّمَرَٰتِ لَعَلَّهُمۡ يَشۡكُرُونَ
“Mbuye wanga! Ndithu ine ndaikhazika ina mwa mbumba yanga (mwana wanga Ismail) pachigwa ichi (cha Makka) chopanda zomera pa Nyumba Yanu Yopatulika (Al-Ka’ba); Mbuye wathu (aloleni) kuti akhale opemphera Swala; choncho ichiteni mitima ya anthu kukhala yopendekera kwa iwo (akonde kudzakhala malo amenewo), ndipo apatseni zipatso kuti athokoze.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبَّنَآ إِنَّكَ تَعۡلَمُ مَا نُخۡفِي وَمَا نُعۡلِنُۗ وَمَا يَخۡفَىٰ عَلَى ٱللَّهِ مِن شَيۡءٖ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا فِي ٱلسَّمَآءِ
“Mbuye wathu! Ndithu Inu mukudziwa zimene tikubisa ndi zomwe tikuonetsa poyera. Ndipo palibe chilichonse chobisika kwa Allah, m’dziko kapena kumwamba.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ ٱلَّذِي وَهَبَ لِي عَلَى ٱلۡكِبَرِ إِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَۚ إِنَّ رَبِّي لَسَمِيعُ ٱلدُّعَآءِ
“Kuyamikidwa konse nkwa Allah Yemwe wandipatsa ine ku ukulu Ismail ndi Ishâq. Ndithu Mbuye wanga Ngwakumva pempho (la kapolo Wake).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبِّ ٱجۡعَلۡنِي مُقِيمَ ٱلصَّلَوٰةِ وَمِن ذُرِّيَّتِيۚ رَبَّنَا وَتَقَبَّلۡ دُعَآءِ
“Mbuye wanga! Ndichiteni kukhala wopemphera Swala pamodzi ndi mbumba yanga. Mbuye wathu! Landirani zopempha zanga.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبَّنَا ٱغۡفِرۡ لِي وَلِوَٰلِدَيَّ وَلِلۡمُؤۡمِنِينَ يَوۡمَ يَقُومُ ٱلۡحِسَابُ
“Mbuye wathu! Ndikhululukireni ine ndi makolo anga ndi amene akhulupirira, (makamaka) patsiku la chiwerengero (Qiyâma)!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا تَحۡسَبَنَّ ٱللَّهَ غَٰفِلًا عَمَّا يَعۡمَلُ ٱلظَّٰلِمُونَۚ إِنَّمَا يُؤَخِّرُهُمۡ لِيَوۡمٖ تَشۡخَصُ فِيهِ ٱلۡأَبۡصَٰرُ
Ndipo usaganize kuti Allah waiwala zomwe akuchita oipa. Ndithudi, Iye akuwalekelera chabe mpaka tsiku lomwe maso awo adzatong’oke (chifukwa cha mantha).[243]
[243] Ndithudi machitidwe a Allah nkuwalekelera oipa pamene akuchita zoipa. Sawalanga mwachangu. Koma akafuna kuwalanga amawakhaulitsa ndi chilango choopsa. Choncho munthu asanyengeke pamene akulakwira Allah namulekelera osamulanga.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مُهۡطِعِينَ مُقۡنِعِي رُءُوسِهِمۡ لَا يَرۡتَدُّ إِلَيۡهِمۡ طَرۡفُهُمۡۖ وَأَفۡـِٔدَتُهُمۡ هَوَآءٞ
(Adzakhala) akuyenda mothamanga mitu ili m’mwamba ndipo maso awo osatha kuphethira, ndipo m’mitima mwawo muli mopanda kanthu (mopanda ganizo lililonse chifukwa cha kudzadzidwa ndi mantha).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَنذِرِ ٱلنَّاسَ يَوۡمَ يَأۡتِيهِمُ ٱلۡعَذَابُ فَيَقُولُ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ رَبَّنَآ أَخِّرۡنَآ إِلَىٰٓ أَجَلٖ قَرِيبٖ نُّجِبۡ دَعۡوَتَكَ وَنَتَّبِعِ ٱلرُّسُلَۗ أَوَلَمۡ تَكُونُوٓاْ أَقۡسَمۡتُم مِّن قَبۡلُ مَا لَكُم مِّن زَوَالٖ
Ndipo achenjeze anthu za tsiku lomwe chilango chidzawadzera; ndipo amene ankadzichitira okha zoipa adzakhala akunena: “Mbuye wathu! Tichedwetseni kanthawi kochepa (tipatseninso mwawi kuti tibwelere pa dziko); tikayankhe kuitana Kwanu ndi kuwatsata atumiki.” (Adzauzidwa): “Kodi simunkalumbira kale kuti inu simudzachoka (pa dziko)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَسَكَنتُمۡ فِي مَسَٰكِنِ ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ وَتَبَيَّنَ لَكُمۡ كَيۡفَ فَعَلۡنَا بِهِمۡ وَضَرَبۡنَا لَكُمُ ٱلۡأَمۡثَالَ
“Chikhalirecho mudakhala m’malo mommuja mwa omwe adadzichitira okha zoipa; ndipo kudaonekeratu poyera kwa inu mmene tidawachitira (powaononga); ndipo tidakufotokozerani mafanizo (osiyanasiyana koma inu mudatsutsa).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقَدۡ مَكَرُواْ مَكۡرَهُمۡ وَعِندَ ٱللَّهِ مَكۡرُهُمۡ وَإِن كَانَ مَكۡرُهُمۡ لِتَزُولَ مِنۡهُ ٱلۡجِبَالُ
Ndithudi, adachita ziwembu zawo, koma ziwembu zawo zili kwa Allah (akuzidziwa bwinobwino); ndipo ziwembu zawozo angakhale zitatha kuchotsetsa mapiri (sangamchite kanthu Mtumiki Muhammad (s.a.w} popeza Allah wamteteza).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَلَا تَحۡسَبَنَّ ٱللَّهَ مُخۡلِفَ وَعۡدِهِۦ رُسُلَهُۥٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٞ ذُو ٱنتِقَامٖ
Choncho usaganize kuti Allah Ngwakuswa lonjezo Lake kwa atumiki Ake. Ndithu Allah ndi mwini mphamvu (salephera chilichonse), Ngobwezera chilango mwaukali.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَوۡمَ تُبَدَّلُ ٱلۡأَرۡضُ غَيۡرَ ٱلۡأَرۡضِ وَٱلسَّمَٰوَٰتُۖ وَبَرَزُواْ لِلَّهِ ٱلۡوَٰحِدِ ٱلۡقَهَّارِ
(Likumbukireni) tsiku lomwe nthaka iyi idzasinthidwa kukhala nthaka ina (yachilendo), ndi thambonso (lidzakhala lina), ndipo iwo (anthu onse adzatuluka m’manda mwawo) adzaonekera pamaso pa Allah Mmodzi Wamphamvu (zopanda malire).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَرَى ٱلۡمُجۡرِمِينَ يَوۡمَئِذٖ مُّقَرَّنِينَ فِي ٱلۡأَصۡفَادِ
Ndipo oipa udzawaona tsiku limenelo atanjatidwa ndi unyolo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
سَرَابِيلُهُم مِّن قَطِرَانٖ وَتَغۡشَىٰ وُجُوهَهُمُ ٱلنَّارُ
Zovala zawo zidzakhala zaphula, ndipo Moto udzavindikira nkhope zawo;
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لِيَجۡزِيَ ٱللَّهُ كُلَّ نَفۡسٖ مَّا كَسَبَتۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ سَرِيعُ ٱلۡحِسَابِ
Kuti Allah aulipire mzimu uliwonse pa zomwe udakolola; ndithu; Allah Ngwachangu pakuwerengera.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
هَٰذَا بَلَٰغٞ لِّلنَّاسِ وَلِيُنذَرُواْ بِهِۦ وَلِيَعۡلَمُوٓاْ أَنَّمَا هُوَ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞ وَلِيَذَّكَّرَ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Izi zikukwana kukhala phunziro kwa anthu kuti achenjezedwe nazo, ndi kuti azindikire kuti Iye (Allah) ndi Mulungu Mmodzi basi, ndikuti eni nzeru akumbukire.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Ibrahim
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại