Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-Naba'   Câu:

Chương Al-Naba'

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ
۞ Kodi akufunsana zachiyani?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلۡعَظِيمِ
Za nkhani yayikulu ija.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِي هُمۡ فِيهِ مُخۡتَلِفُونَ
Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]
[372] Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupilira Allah) adali kufunsana wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Qiyâma ndi uneneri wa Mtumiki Muhammad. Amafunsana kuti, “Kodi nzoona tidzauka m’manda, nanga nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?” Adali kufunsananso kuti, “Kodi zakuti Allah ndi Mmodzi ndi zoona?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]
[373] Kuyankhula koti: “Kallaa” kwanenedwa kwambiri m’Qur’an. Tanthauzo lake nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]
[374] Allah, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi sadadziwebe mpaka pano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Allah, ndikuti Allah ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lachimaliziro; pamene munthu aliyense adzalipidwa pa zimene adachita? Basi tsiku lachimaliziro likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ مِهَٰدٗا
Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]
[375] Kuyambira Ayah iyi, kudzafika Ayah 16, Allah akusonyeza anthu Ake madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka madalitso amenewa m’dziko sangawasiye anthu Ake m’kusokera popanda kuwatumizira munthu wowaongolera ku njira yabwino, ndikuwadziwitsa zamtendere wapadziko ndi tsiku lachimaliziro. Ndikuti Allah amene adapanga zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake. Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلۡجِبَالَ أَوۡتَادٗا
Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَخَلَقۡنَٰكُمۡ أَزۡوَٰجٗا
Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَعَلۡنَا نَوۡمَكُمۡ سُبَاتٗا
Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَعَلۡنَا ٱلَّيۡلَ لِبَاسٗا
Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَعَلۡنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشٗا
Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَبَنَيۡنَا فَوۡقَكُمۡ سَبۡعٗا شِدَادٗا
Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَعَلۡنَا سِرَاجٗا وَهَّاجٗا
Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡمُعۡصِرَٰتِ مَآءٗ ثَجَّاجٗا
Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لِّنُخۡرِجَ بِهِۦ حَبّٗا وَنَبَاتٗا
Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَنَّٰتٍ أَلۡفَافًا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ كَانَ مِيقَٰتٗا
Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَوۡمَ يُنفَخُ فِي ٱلصُّورِ فَتَأۡتُونَ أَفۡوَاجٗا
Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ أَبۡوَٰبٗا
Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَسُيِّرَتِ ٱلۡجِبَالُ فَكَانَتۡ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]
[376] Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati akhazikika monga m’mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje louluka ndi mphepo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتۡ مِرۡصَادٗا
Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابٗا
Mbuto ya opyola malire.[377]
[377] Jahannam ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lachimaliziro. Apa Allah akutidziwitsa kuti Jahannam ndi malo amene akudikira akafiri kuti m’menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo powasonyeza zizindikiro zoti iwo ndi aneneri a Allah. Ndiponso kumulakwira Allah pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa Allah, kukana utumiki wa Mahammad (s.a.w) ndi kukana uthenga wa Qur’an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحۡقَابٗا
Adzakhala m’menemo muyaya.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرۡدٗا وَلَا شَرَابًا
Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِلَّا حَمِيمٗا وَغَسَّاقٗا
Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
جَزَآءٗ وِفَاقًا
Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ لَا يَرۡجُونَ حِسَابٗا
Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابٗا
Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَكُلَّ شَيۡءٍ أَحۡصَيۡنَٰهُ كِتَٰبٗا
Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَذُوقُواْ فَلَن نَّزِيدَكُمۡ إِلَّا عَذَابًا
Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ مَفَازًا
Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
حَدَآئِقَ وَأَعۡنَٰبٗا
Minda ndi zipatso za mphesa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَكَوَاعِبَ أَتۡرَابٗا
Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَكَأۡسٗا دِهَاقٗا
Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَّا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا كِذَّٰبٗا
Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
جَزَآءٗ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابٗا
Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]
[378] Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri: Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Allah kumene anthu Ake abwino adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m’mene afotokozera mu Ayah iyi ndi msura zina. Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa (osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa zake. Koma mowa wa patsiku la Qiyâma udzakhala wopanda zoipa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلرَّحۡمَٰنِۖ لَا يَمۡلِكُونَ مِنۡهُ خِطَابٗا
Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ صَفّٗاۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنۡ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحۡمَٰنُ وَقَالَ صَوَابٗا
Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلۡحَقُّۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا
Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّآ أَنذَرۡنَٰكُمۡ عَذَابٗا قَرِيبٗا يَوۡمَ يَنظُرُ ٱلۡمَرۡءُ مَا قَدَّمَتۡ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلۡكَافِرُ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ تُرَٰبَۢا
Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-Naba'
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại