《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 章: 玛欧奈   段:

玛欧奈

أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يُكَذِّبُ بِٱلدِّينِ
Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
[487] Sura imeneyi ikufotokoza m’mene alili makhalidwe a anthu ambiri, ngakhale amene amadzitcha kuti ndi Asilamu. Aliyense amene ali ndi makhalidwe otere ndiye kuti sakhulupilira za tsiku la chiweruziro. Akadakhala kuti akukhulupilira za tsikuli, sibwenzi akusiya kuwachitira za chifundo osauka ndi amasiye. Sapereka chithandizo ngakhale kulimbikitsa ena ngati iye alibe.
阿拉伯语经注:
فَذَٰلِكَ ٱلَّذِي يَدُعُّ ٱلۡيَتِيمَ
Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).
阿拉伯语经注:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
阿拉伯语经注:
فَوَيۡلٞ لِّلۡمُصَلِّينَ
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَن صَلَاتِهِمۡ سَاهُونَ
Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]
[488] Kuchitira mphwayi mapemphero (Swala), kumeneku ndiko kupemphera modukizadukiza. Tsiku lina nkupempherapo, tsiku lina ayi. Kapenanso kupemphera modzionetsera kwa anthu (riyaa).
阿拉伯语经注:
ٱلَّذِينَ هُمۡ يُرَآءُونَ
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
[489] Riyaa ndiko kuchita ntchito yabwino ndicholinga choonetsa anthu, kuti akuone kuti ndiwe wabwino, mwina kuti ukhale wokondedwa ndi anthu. Kapenanso kuti upeze za m’matumba mwawo. Amenewa ndi machitidwe a “Shiriki” (kum’phatikiza Allah ndi zolengedwa Zake pa mapemphero) ndiponso ndi njira yobera anthu.
阿拉伯语经注:
وَيَمۡنَعُونَ ٱلۡمَاعُونَ
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 玛欧奈
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭