Check out the new design

Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: ət-Tovbə   Ayə:
ٱسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ أَوۡ لَا تَسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ إِن تَسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ سَبۡعِينَ مَرَّةٗ فَلَن يَغۡفِرَ ٱللَّهُ لَهُمۡۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
(E iwe Mtumiki!) Uwapemphere chikhululuko (achiphamaso) kapena usawapemphere, (zonsezo nchimodzimodzi). Ngakhale utawapemphera chikhululuko chochuluka kwabasi mokwanira makumi asanu ndi awiri (70) Allah sangawakhululukire. Zimenezo nchifukwa chakuti iwo amkana Allah ndi Mtumiki Wake. Ndipo Allah satsogolera anthu ophwanya malamulo (Ake).
Ərəbcə təfsirlər:
فَرِحَ ٱلۡمُخَلَّفُونَ بِمَقۡعَدِهِمۡ خِلَٰفَ رَسُولِ ٱللَّهِ وَكَرِهُوٓاْ أَن يُجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَقَالُواْ لَا تَنفِرُواْ فِي ٱلۡحَرِّۗ قُلۡ نَارُ جَهَنَّمَ أَشَدُّ حَرّٗاۚ لَّوۡ كَانُواْ يَفۡقَهُونَ
Akondwa amene adasiidwa m’mbuyo (osapita kunkhondo) chifukwa chakukhala kwawo m’mbuyo polekana ndi Mtumiki wa Allah, nakuda kumenyana pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo, nati (kwa anzawo): “Musapite (ku nkhondo) m’nthawi yotenthayi.” Auze: “Moto wa Jahannam ngotentha kwambiri akadakhala akuzindikira.”
Ərəbcə təfsirlər:
فَلۡيَضۡحَكُواْ قَلِيلٗا وَلۡيَبۡكُواْ كَثِيرٗا جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Choncho, aseke pang’ono (padziko lapansi). Ndipo adzalira kwambiri (patsiku lachimaliziro); (iyo ndi) mphoto ya zomwe adapeza (kuchokera m’zochita zawo zoipa).[212]
[212] Anthu achinyengo (achiphamaso) adakana kupita naye limodzi Mtumiki (s.a.w) ku nkhondo namasangalalira kukhala kwawoko. Ndipo apa Allah akuwauza kuti asangalale ndi kuseka pang’ono. Koma adzalira ndi kukukuta mano nthawi yaitali.
Ərəbcə təfsirlər:
فَإِن رَّجَعَكَ ٱللَّهُ إِلَىٰ طَآئِفَةٖ مِّنۡهُمۡ فَٱسۡتَـٔۡذَنُوكَ لِلۡخُرُوجِ فَقُل لَّن تَخۡرُجُواْ مَعِيَ أَبَدٗا وَلَن تُقَٰتِلُواْ مَعِيَ عَدُوًّاۖ إِنَّكُمۡ رَضِيتُم بِٱلۡقُعُودِ أَوَّلَ مَرَّةٖ فَٱقۡعُدُواْ مَعَ ٱلۡخَٰلِفِينَ
Ngati Allah akubweza (ku nkhondoko) nkufika kugulu lina la mwa iwo ndipo iwo nkukupempha chilolezo chakutuluka (kupita ku nkhondo zomwe zidzapezeke mtsogolo), nena: “Inu simudzatuluka nane mpaka muyaya, ngakhalenso kumenyana ndi adani pamodzi nane; inu mudakonda kukhala nthawi yoyamba; choncho khalani (nthawi zonse) pamodzi ndi otsalira (pambuyo).”
Ərəbcə təfsirlər:
وَلَا تُصَلِّ عَلَىٰٓ أَحَدٖ مِّنۡهُم مَّاتَ أَبَدٗا وَلَا تَقُمۡ عَلَىٰ قَبۡرِهِۦٓۖ إِنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَمَاتُواْ وَهُمۡ فَٰسِقُونَ
Ndipo usamupemphelere konse aliyense wa iwo yemwe wamwalira, ndipo usaimilire pamanda ake (kumpemphelera); ndithu iwo amukana Allah ndi Mtumiki Wake, ndipo amwalira uku ali opandukira chilamulo (cha Allah).
Ərəbcə təfsirlər:
وَلَا تُعۡجِبۡكَ أَمۡوَٰلُهُمۡ وَأَوۡلَٰدُهُمۡۚ إِنَّمَا يُرِيدُ ٱللَّهُ أَن يُعَذِّبَهُم بِهَا فِي ٱلدُّنۡيَا وَتَزۡهَقَ أَنفُسُهُمۡ وَهُمۡ كَٰفِرُونَ
Ndipo chisakudolole chuma chawo kapena ana awo. Ndithu Allah akufuna kuwalanga ndi zimenezo pa dziko lapansi, ndi kuti mizimu yawo ichoke ali osakhulupirira.
Ərəbcə təfsirlər:
وَإِذَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٌ أَنۡ ءَامِنُواْ بِٱللَّهِ وَجَٰهِدُواْ مَعَ رَسُولِهِ ٱسۡتَـٔۡذَنَكَ أُوْلُواْ ٱلطَّوۡلِ مِنۡهُمۡ وَقَالُواْ ذَرۡنَا نَكُن مَّعَ ٱلۡقَٰعِدِينَ
Ndipo Sura ikavumbulutsidwa (yonena kuti): “Mkhulupirireni Allah ndi kumenya nkhondo (chifukwa cha chipembedzo Chake) pamodzi ndi Mtumiki Wake,” opeza bwino mwa iwo akukupempha chilolezo (kuti asapite ku nkhondo), ndipo akuti: “Tisiye tikhale pamodzi ndi okhala (otsalira m’mbuyo).”
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: ət-Tovbə
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. - Tərcumənin mündəricatı

Khalid İbrahim Beytala tərəfindən tərcümə.

Bağlamaq