Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (104) Surah / Kapitel: Al-Kahf
ٱلَّذِينَ ضَلَّ سَعۡيُهُمۡ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَهُمۡ يَحۡسَبُونَ أَنَّهُمۡ يُحۡسِنُونَ صُنۡعًا
“Iwo ndi omwe khama lawo lataika m’moyo wa pa dziko lapansi, pomwe iwowo akuganiza kuti akuchita zabwino”.[263]
[263] M’ndime iyi akutiuza kuti amene sadakhulupirire Allah, pa tsiku lachimaliziro ndiye kuti zonse zochita zawo zidzakhala zowonongeka. Ntchito zabwino za munthu kuti zikalandiridwe kwa Allah, poyamba akhulupirire Allah ndiponso akhulupirire kuti tsiku lachimaliziro lilipo. Koma ngati sakhulupilira, ndiye kuti zochita zake sizikayesedwa pasikelo koma akangomponya kung’anjo yamoto. Pankhaniyi Mtumiki (s.a.w) adati: “Tsiku la Qiyâma padzabwera munthu wamtali, wakudyabwino, wakumwa zomwaimwa, koma kwa Allah adzakhala wopepuka wosafanana ngakhale ndikulemera kwa phiko la udzudzu.” Hadisiyi adainena ndi Al -Hafizi Ibn Hajar m’buku la Fatuhul Bari, Volume 8 tsamba la 324.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (104) Surah / Kapitel: Al-Kahf
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen