Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (237) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
وَإِن طَلَّقۡتُمُوهُنَّ مِن قَبۡلِ أَن تَمَسُّوهُنَّ وَقَدۡ فَرَضۡتُمۡ لَهُنَّ فَرِيضَةٗ فَنِصۡفُ مَا فَرَضۡتُمۡ إِلَّآ أَن يَعۡفُونَ أَوۡ يَعۡفُوَاْ ٱلَّذِي بِيَدِهِۦ عُقۡدَةُ ٱلنِّكَاحِۚ وَأَن تَعۡفُوٓاْ أَقۡرَبُ لِلتَّقۡوَىٰۚ وَلَا تَنسَوُاْ ٱلۡفَضۡلَ بَيۡنَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٌ
Ndipo ngati mwalekana nawo (akaziwo) musanakhudzane nawo mutawadziwitsa gawo la chiwongo chawo, apatseni theka la chimene mudagwirizana kuwapatsa pokhapokha ngati akaziwo atakana okha (theka la chiwongocho), kapena (mwamuna) uja yemwe kumangitsa kwa ukwati kuli m’manja mwake amusiire (chiwongo chonsecho mkaziyo). Ndipo ngati mutasiirana (zimenezo) zingakuyandikitseni kumbali yoopa Allah. Ndipo musaiwale kuchitirana zabwino pakati panu (ngakhale kuti mukulekana). Ndithudi Allah akuona zonse zimene mukuchita.[40]
[40] Ngati udamkwatira mkazi ndipo nkulekana naye usanalowane naye, umpatse theka lachiwongo chomwe chidatchulidwa. Ngati udampatsa chiwongo chonse, ndiye kuti akubwezere theka lake. Koma ndibwino kwa mwamuna kumpatsa mkazi chiwongo chonse ngati anali asanampatse. Ngati anampatsa asaitanitsenso chiwongocho. Ndibwinonso kwa mkazi kubweza chiwongo chonse ngati adampatsa chonse, kapena kukana kuti asampatse ngati anali asanapatsidwe. Aliyense mwa awiriwa asakhale ndi chibaba chofuna kupeza ndalama pakutha pa ukwatiwo. Malamulo tanenawa amagwira ntchito ngati chiwongo chidatchulidwa kuchuluka kwake pomwe ankafunsira ukwati. Koma ngati chiwongocho sanachitchule kuchuluka kwake kotero kuti sadagwirizane za chiwongocho kuti adzapereka mwakutimwakuti, pamenepa ndiye kuti ampatse chinthu cholekanira choti chimsangalatse. Ili ndilo tanthauzo la zomwe zatchulidwa m’ndime ya 236.
Ndithudi apa akutilangiza mwamphamvu kuti tizichitirana zabwino ngakhale panthawi yolekana ukwati. Anthu asaiwale ubwino ndi chikondi zomwe ankachitirana pakati pawo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (237) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen