Check out the new design

Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Āl ʿImrān   Vers:
لَن تَنَالُواْ ٱلۡبِرَّ حَتَّىٰ تُنفِقُواْ مِمَّا تُحِبُّونَۚ وَمَا تُنفِقُواْ مِن شَيۡءٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ بِهِۦ عَلِيمٞ
۞ Simudzapeza ubwino (weniweni) kufikira mutapereka m’zimene mukuzikonda. Ndipo chilichonse chimene mupereka, ndithudi, Allah akuchidziwa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
۞ كُلُّ ٱلطَّعَامِ كَانَ حِلّٗا لِّبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ إِلَّا مَا حَرَّمَ إِسۡرَٰٓءِيلُ عَلَىٰ نَفۡسِهِۦ مِن قَبۡلِ أَن تُنَزَّلَ ٱلتَّوۡرَىٰةُۚ قُلۡ فَأۡتُواْ بِٱلتَّوۡرَىٰةِ فَٱتۡلُوهَآ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Zakudya zonse zidali zololedwa kwa ana a Israyeli kupatula chimene adadziretsa Israyeli mwini wake Taurat isadavumbulutsidwe. Nena: “Bwerani ndi Tauratiyo ndipo iwerengeni ngati mukunena zoona.”[74]
[74] Ayuda adauza Mtumiki (s.a.w) kuti: “Iwe sukutsata chikhalidwe cha Ibrahim ngakhale umadzinyenga kuti ukumtsata. Nanga bwanji ukudya nyama ya ngamira, pomwe mneneri Ibrahim sadali kudya ngamira?” Apa Allah akuwatsutsa kuti ngabodza. Ndipo buku lawo la Taurat ndilo mboni pa bodza lawoli. atavundukula buku lawo la Taurat apeza kuti yemwe adadziletsa kudya ngamira ndi Yakobo, yemwe ankadziwikanso kuti Israeli, osati mneneri Ibrahim.Yakobo njemwe adasala kudya nyama ya ngamira mwa chifuniro chake. Ndipo izi adazichita popanda kukakamizidwa ndi Allah.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَمَنِ ٱفۡتَرَىٰ عَلَى ٱللَّهِ ٱلۡكَذِبَ مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلظَّٰلِمُونَ
Choncho aliyense amene adzapekera bodza Allah pambuyo pa izi iwo ndiwochita zoipa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ صَدَقَ ٱللَّهُۗ فَٱتَّبِعُواْ مِلَّةَ إِبۡرَٰهِيمَ حَنِيفٗاۖ وَمَا كَانَ مِنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Nena: “Allah wanena zoona. Choncho tsatirani chipembedzo cha Ibrahim yemwe adali wolungama; sadali mwa ophatikiza Allah ndi mafano.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّ أَوَّلَ بَيۡتٖ وُضِعَ لِلنَّاسِ لَلَّذِي بِبَكَّةَ مُبَارَكٗا وَهُدٗى لِّلۡعَٰلَمِينَ
Ndithudi, nyumba yoyamba yomwe idakhazikitsidwa chifukwa cha anthu (kuti azipempheramo) ndiyomwe ili pa Bakka (ku Makka); yodalitsidwa ndiponso ndichiongolo kwa anthu onse.[75]
[75] Apa akunenetsa kuti nyumba yoyamba kukhazikitsidwa kwa anthu kuti ikhale yochitira mapemphero ndi Al-Kaaba, osati Baiti Muqaddas monga momwe Ayuda amakhulupilira.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِيهِ ءَايَٰتُۢ بَيِّنَٰتٞ مَّقَامُ إِبۡرَٰهِيمَۖ وَمَن دَخَلَهُۥ كَانَ ءَامِنٗاۗ وَلِلَّهِ عَلَى ٱلنَّاسِ حِجُّ ٱلۡبَيۡتِ مَنِ ٱسۡتَطَاعَ إِلَيۡهِ سَبِيلٗاۚ وَمَن كَفَرَ فَإِنَّ ٱللَّهَ غَنِيٌّ عَنِ ٱلۡعَٰلَمِينَ
M’menemo muli zizindikiro zoonekera (zozindikiritsa kupatulika kwake ndi ukale wake); ndi pamalo pomwe Ibrahim adali kuimilira; ndipo amene akulowamo amakhala m’chitetezo; ndipo Allah walamula anthu kuti akachite Hajj ku nyumbayo amene angathe kukonzekera ulendo wonka kumeneko. Ndipo yemwe angakane, (osapitako pomwe ali nazo zomuyenereza), ndithudi, Allah Ngwachikwanekwane pa zolengedwa Zake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ يَٰٓأَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ لِمَ تَكۡفُرُونَ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ وَٱللَّهُ شَهِيدٌ عَلَىٰ مَا تَعۡمَلُونَ
Nena: “E inu amene mudapatsidwa buku! chifukwa chiyani mukuzikana zizindikiro za Allah pomwe Allah ndi Mboni wa zonse zimene mukuchita?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ يَٰٓأَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ لِمَ تَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ مَنۡ ءَامَنَ تَبۡغُونَهَا عِوَجٗا وَأَنتُمۡ شُهَدَآءُۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Nena: “ E inu amene mudapatsidwa buku! Chifukwa chani mukutsekereza anthu amene akhulupirira kuyenda pa njira ya Allah? Mukufuna kuti ikhote pomwe inu ndinu mboni (kuti ndi njira ya Allah yopanda choipa)? Komatu Allah sanyalanyaza zomwe mukuchita.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِن تُطِيعُواْ فَرِيقٗا مِّنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ يَرُدُّوكُم بَعۡدَ إِيمَٰنِكُمۡ كَٰفِرِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Ngati muwamvera ena mwa amene apatsidwa buku, akubwezani kuti mukhale osakhulupirira pambuyo pa chikhulupiliro chanu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Āl ʿImrān
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. - Übersetzungen

Übersetzung von Khalid Ibrahim Bitala.

Schließen