Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (23) Surah / Kapitel: Al-Ahzâb
مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ رِجَالٞ صَدَقُواْ مَا عَٰهَدُواْ ٱللَّهَ عَلَيۡهِۖ فَمِنۡهُم مَّن قَضَىٰ نَحۡبَهُۥ وَمِنۡهُم مَّن يَنتَظِرُۖ وَمَا بَدَّلُواْ تَبۡدِيلٗا
Mwa okhulupirira alipo amuna ena amene adakwaniritsa zomwe adamlonjeza Allah (kuti sadzathawa pa nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w), ena mwa iwo adamaliza moyo wawo (nakwaniritsa lonjezo lawo pofera pa njira ya Allah). Ndipo ena mwa iwo akuyembekezerabe (kufera pa njira ya Allah). Ndipo sadasinthe konse (lonjezo lawo).[320]
[320] Imamu Ibnu Jarir Taburiyu adalemba m’buku lake kuti Anasi Bun Malik adati:- M’bale wa bambo anga, Anasi bun Nadhari sadakhale nawo pa nkhondo ya Badri, ndipo adati: “Sindidakhale pamodzi ndi Mtumiki pa nkhondo yoyamba. Ngati Allah atandifikitsa pa nkhondo ina Allah adzaona zimene ndidzachita pomenya nkhondo modzipereka.” Pa tsiku la nkhondo ya Uhud, pamene Asilamu adabalalikana kuthawa ndipo iye adati:- “E Allah! Ine ndikudzipatula ku zomwe achita awa, osakhulupilira. Ndiponso ndikudandaula mzimene achita awa, Asilamu amene athawa.” Kenako adayenda ndi lupanga lake nakumana ndi Saad bun Muadhi, nati: “E iwe Saad! Ine ndikumva fungo la ku Munda wa mtendere pafupi ndi phiri ili la Uhud.” Kenako adachita nkhondo kufikira adaphedwa. Ndipo Saad adati: “E iwe Mtumiki wa Allah! Sindinathe kuchita chimene iye adachita.” Anasi bun Malik adati: “Tidampeza ali m’gulu lophedwa uku ali ndi mabala okwanira 80, ena otemedwa ndi malupanga, ndipo ena olasidwa ndi mikondo ndi mipaliro. Sitidamzindikire kufikira pamene adadza mlongo wake naamzindikira kupyolera m’nsonga za zala zake.” Ndipo Anasi adatinso: “Tidali kukambirana kuti ndime iyi ikukamba za iye.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (23) Surah / Kapitel: Al-Ahzâb
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen