Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (101) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
وَإِذَا ضَرَبۡتُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَلَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٌ أَن تَقۡصُرُواْ مِنَ ٱلصَّلَوٰةِ إِنۡ خِفۡتُمۡ أَن يَفۡتِنَكُمُ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْۚ إِنَّ ٱلۡكَٰفِرِينَ كَانُواْ لَكُمۡ عَدُوّٗا مُّبِينٗا
Ndipo ngati mukuyenda pa dziko, sikulakwa kwa inu kufupikitsa Swala ngati mukuopa kuti angakusokonezeni omwe sadakhulupirire. Ndithudi, osakhulupirira ndi adani anu oonekera.[138]
[138] Pamene Asilamu adawalamulira zakusamuka, adawafupikitsira Swala chifukwa cha mavuto am’njira monga kuti (a) Swala zokhala ndi raka zinayi akhoza kuziswali ndi raka ziwiriziwiri. (b) Akhoza kuswali katatu kokha patsiku m’malo mwakasanu. Izi zili motere: Swala ya Dhuhr nkuiphatikiza pamodzi ndi Swala ya Asr; kuzipemphera panthawi ya Dhuhr kapena kuzipemphera panthawi ya Asr. Swala ya Maghrib nkuipemphera pamodzi ndi Swala ya Isha. Adzayamba kupemphera Swala ya Maghrib raka zitatu kenako nkupemphera Isha raka ziwiri. Koma Swala ya Subh yokha njomwe imapempheredwa payokha ndiponso m’nthawi yake. Lamuloli analikhazikitsa pamene Asilamu adali ndi mantha ndi masautso am’njira. Ndipo lidasiidwa momwemo losasinthika mpaka lero m’nthawi yomwe anthu akukwera galimoto, sitima ndi ndege.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (101) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen