Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (34) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
ٱلرِّجَالُ قَوَّٰمُونَ عَلَى ٱلنِّسَآءِ بِمَا فَضَّلَ ٱللَّهُ بَعۡضَهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ وَبِمَآ أَنفَقُواْ مِنۡ أَمۡوَٰلِهِمۡۚ فَٱلصَّٰلِحَٰتُ قَٰنِتَٰتٌ حَٰفِظَٰتٞ لِّلۡغَيۡبِ بِمَا حَفِظَ ٱللَّهُۚ وَٱلَّٰتِي تَخَافُونَ نُشُوزَهُنَّ فَعِظُوهُنَّ وَٱهۡجُرُوهُنَّ فِي ٱلۡمَضَاجِعِ وَٱضۡرِبُوهُنَّۖ فَإِنۡ أَطَعۡنَكُمۡ فَلَا تَبۡغُواْ عَلَيۡهِنَّ سَبِيلًاۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيّٗا كَبِيرٗا
Amuna ndiayang’aniri pa akazi chifukwa choti Allah watukula ena pa ulemelero pamwamba pa ena, chifukwa cha chuma chawo chimene apereka. Choncho, akazi abwino ndi omwe ali omvera, odzisunga ngakhale amuna awo palibe pakuti Allah wawalamula kudzisunga. Ndipo akazi omwe mukuopa mnyozo wawo, achenjezeni; ndipo kenako achokereni pamphasa, (apo ayi), akwapuleni (kukwapula kosavulaza), koma ngati akukumverani, musawafunire njira yowavutitsira. Ndithu Allah ndi yemwe ali Wapamwamba, Wamkulu (kuposa inu nonse).[122]
[122] Apa akuti amuna ndi amene akhale ndi ulamuliro pa akazi awo, powatsogolera ku miyambo yabwino. Osati kuti mkazi adzitukumule kwa mwamuna wake poti iye ngophunzira zedi kapena wanzeru zochuluka kotero kuti mwamuna m’nyumba osamuyesa kanthu. Ngati atero ndiye kuti sakhala Asilamu owona. M’ndimeyi atchulamonso makhalidwe ofunika kuti akazi akhale nawo. Ndipo atchulamo malangizo olangira nawo mkazi ngati samvera. Choyamba amchenjeze ndi mawu. Ngati kuchenjezako sikunathandize, asagone naye limodzi pamphasa. Ndipo ngati akupitirizabe kuchita mnyozo akupatsidwa chilolezo mwamuna kuti amlange pommenya mwakumuopyeza, osati kumenya komgulula nako mano. Komabe mahadisi a Mtumiki (s.a.w) akunena kuti asanaganize zommenya ayeseyese kumkonza ponena naye mofewa ndi kumuonetsa kulakwa kwake. Ngati atalephera zonsezi, aitane anthu kuti adzawayanjanitse m’njira yabwino. Naonso anthuwo akhale ndi cholinga choyanjanitsa osati kupasula. Amunanso akuwachenjeza apa kuti iwo ndi amene ali ndi nyonga ndi udindo. Allah ndiye Wamkulu kuposa iwo amunawo. Mawu oti “Hafizatu Lilighaibi” maulama ena akuwatanthauzira kuti “Akhale osunga chinsinsi,” chimene chili pakati pa iwo ndi amuna awo ndi zonse zomwe zimachitika m’nyumba, pakuti nthawi zambiri akazi sakhalira kuulula za m’nyumba.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (34) Surah / Kapitel: An-Nisâ’
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen