Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Jumu‘a   Vers:

Al-Jumu‘a

يُسَبِّحُ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ ٱلۡمَلِكِ ٱلۡقُدُّوسِ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡحَكِيمِ
Zonse zakumwamba ndi dziko lapansi zikulemekeza Allah; Mfumu, Woyera, Wamphamvu zopambana ndi nzeru zakuya (ndi kumyeretsa ku makhalidwe osayenerana ndi ulemelero Wake).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
هُوَ ٱلَّذِي بَعَثَ فِي ٱلۡأُمِّيِّـۧنَ رَسُولٗا مِّنۡهُمۡ يَتۡلُواْ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتِهِۦ وَيُزَكِّيهِمۡ وَيُعَلِّمُهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَإِن كَانُواْ مِن قَبۡلُ لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Iye ndiAmene adatumiza kwa Ummiyyina (osadziwa kulemba ndi kuwerenga), Mtumiki wochokera mwa iwo kuti awawerengere ndime Zake ndi kuti awayeretse (ku uchimo ndi kumakhalidwe oipa) ndi kuwaphunzitsa Qur’an ndi mawu anzeru (a mtumiki) ndithu kale adali osokera kowonekera (Mtumiki {s.a.w} asadadze kwa iwo).[361]
[361] Arabu amatchedwa “Ummiyyuna” chifukwa chakuti samadziwa kulemba ndi kuwerenga. Kusadziwa kulemba ndi kuwerenga kudafala pakati pawo ndipo ngakhale Mtumiki amene samadziwa kulemba ndi kuwerenga chilichonse. M’ndime imeneyi, Allah akutiphunzitsa kuti adampereka Muhammad (s.a.w) kuti awaongolere anthu ku njira yoongoka. Iyeyu adaperekedwa panyengo imene anthu adali ndi khumbo la Mneneri wa Allah kuti awatsogolere ku njira yolungama pakuti pa nthawiyo zipembedzo zonse za Allah zidali zitaonongeka. Pachiyambi Arabu amatsatira chipembedzo cha Ibrahim. Kenako adasintha nkuyamba kupembedza mafano. Adayambitsa zinthu zambiri zosalolezedwa ndi Allah. Ndipo nawonso anthu amabuku, Ayuda ndi Akhrisitu, adasintha zophunzitsa za mabuku awo. Choncho Allah adapereka Muhammad (s.a.w) ndi malamulo aakulu okwanira bwino. Mkati mwake mudali chilichonse chofunika m’moyo wa anthu pa nyengo zosiyanasiyana pa moyo wa pa dziko ndi wa pa tsiku lachimaliziro. Allah adampatsa zabwino zomwe sadampatseponso wina aliyense, woyamba ndi womaliza.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَءَاخَرِينَ مِنۡهُمۡ لَمَّا يَلۡحَقُواْ بِهِمۡۚ وَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
Ndipo (adamtumizanso) kwa ena mwa iwo, omwe sadakumane nawo, ndipo Iye (Allah) Ngopambana (pa chinthu chilichonse ndi Wamphamvu zoposa ndiponso) Ngwanzeru zakuya.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ذَٰلِكَ فَضۡلُ ٱللَّهِ يُؤۡتِيهِ مَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ ذُو ٱلۡفَضۡلِ ٱلۡعَظِيمِ
Umenewo ndiwo ubwino wa Allah akuupereka kwa amene wamfuna (mwa akapolo Ake); ndipo Allah yekha ndi Mwini ubwino waukulu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
مَثَلُ ٱلَّذِينَ حُمِّلُواْ ٱلتَّوۡرَىٰةَ ثُمَّ لَمۡ يَحۡمِلُوهَا كَمَثَلِ ٱلۡحِمَارِ يَحۡمِلُ أَسۡفَارَۢاۚ بِئۡسَ مَثَلُ ٱلۡقَوۡمِ ٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِۚ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Fanizo la (Ayuda) amene adawasenzetsa Taurat (pokakamizidwa kuti atsatire zophunzitsa za bukulo, koma osatsatira), ali ngati bulu amene akusenza mabuku akuluakulu anzeru, (koma osathandizika nawo). Taonani kuipa fanizo la anthu amene atsutsa zisonyezo za Allah. Ndipo Allah saongola anthu achinyengo.[362]
[362] Allah Wotukuka, akufanizira Ayuda amene amadziwa kuwerenga Taurat bwinobwino, koma zomwe akuwerengazo osazigwiritsa ntchito, ngati bulu wosenza mabuku akuluakulu popanda chopeza pomwe mabukuwo ali odzaza ndi zinthu zabwino zophunzitsa nzeru zabwino.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ هَادُوٓاْ إِن زَعَمۡتُمۡ أَنَّكُمۡ أَوۡلِيَآءُ لِلَّهِ مِن دُونِ ٱلنَّاسِ فَتَمَنَّوُاْ ٱلۡمَوۡتَ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Nena: “E inu Ayuda! Ngati mwadziganizira kuti ndithu ndinu okondedwa a Allah kuposa (mitundu ina ya) anthu, ilakelakeni imfa (kuti mukalowe ku mtendere wa Allah) ngati mukunena zoona.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَلَا يَتَمَنَّوۡنَهُۥٓ أَبَدَۢا بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيهِمۡۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo sangailakelake mpang’ono pomwe chifukwa cha (zoipa) zimene manja awo atsogoza! Ndipo Allah akudziwa bwino za (anthu) osalungama.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلۡ إِنَّ ٱلۡمَوۡتَ ٱلَّذِي تَفِرُّونَ مِنۡهُ فَإِنَّهُۥ مُلَٰقِيكُمۡۖ ثُمَّ تُرَدُّونَ إِلَىٰ عَٰلِمِ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِ فَيُنَبِّئُكُم بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Nena (kuti): “Ndithu imfa imene mukuithawa (palibe chipeneko) ikumana nanu; kenako muzabwezedwa kwa wodziwa zobisika ndi zooneka; ndipo adzakuuzani zimene mudali kuchita.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا نُودِيَ لِلصَّلَوٰةِ مِن يَوۡمِ ٱلۡجُمُعَةِ فَٱسۡعَوۡاْ إِلَىٰ ذِكۡرِ ٱللَّهِ وَذَرُواْ ٱلۡبَيۡعَۚ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Kukaitanidwa ku Swala (pemphero la Ijuma) tsiku la Ijuma, pitani mwachangu kukamtamanda Allah. Ndipo siyani malonda; zimenezo (mwalamulidwazo) nzabwino kwa inu ngati mukudziwa.[363]
[363] M’ndime imeneyi akutiphunzitsa kuti tikamva adhana (kuitana) tsiku la Ijuma, tisiye chilichonse chimene tikuchita ndi kupita mwachangu kukapemphera pemphero la Ijuma. Pempheroli ndilofunika kwa msilamu aliyense makamaka amuna. Asilamu amasonkhana m’Misikiti ikuluikulu pa tsiku limeneli pa sabata iliyonse. Ndipo pa tsiku limeneli ndipomwe Allah adakwaniritsa zolenga zake zonse. Adam adalengedwa pa tsikuli ndipo adalowetsedwa ku Jannah tsiku lomweli. Ndipo adatulutsidwa m’menemo pa tsiku la Ijuma. Mtumiki adafotokozanso za kuti Qiyâma idzadza tsiku la Ijuma.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِذَا قُضِيَتِ ٱلصَّلَوٰةُ فَٱنتَشِرُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَٱبۡتَغُواْ مِن فَضۡلِ ٱللَّهِ وَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ كَثِيرٗا لَّعَلَّكُمۡ تُفۡلِحُونَ
Choncho Swala (ya Ijumayo) ikatha, balalikanani pa dziko, ndipo funani ubwino wa Allah; ndipo mtamandeni Allah kwambiri kuti mupambane (pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِذَا رَأَوۡاْ تِجَٰرَةً أَوۡ لَهۡوًا ٱنفَضُّوٓاْ إِلَيۡهَا وَتَرَكُوكَ قَآئِمٗاۚ قُلۡ مَا عِندَ ٱللَّهِ خَيۡرٞ مِّنَ ٱللَّهۡوِ وَمِنَ ٱلتِّجَٰرَةِۚ وَٱللَّهُ خَيۡرُ ٱلرَّٰزِقِينَ
Ndipo akaona malonda kapena masewero, akubalalika kunka ku zimenezo ndi kukusiya uli chiimire (ukuchita khutuba ndi anthu ochepa). Nena (kwa iwo): “Zimene zili kwa Allah nzabwino kwa inu kuposa masewero ndi malonda. Ndipo Allah Ngwabwino kwambiri kuposa opatsa onse.”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Jumu‘a
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen