Check out the new design

Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: At-Taubah   Vers:
ٱلتَّٰٓئِبُونَ ٱلۡعَٰبِدُونَ ٱلۡحَٰمِدُونَ ٱلسَّٰٓئِحُونَ ٱلرَّٰكِعُونَ ٱلسَّٰجِدُونَ ٱلۡأٓمِرُونَ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَٱلنَّاهُونَ عَنِ ٱلۡمُنكَرِ وَٱلۡحَٰفِظُونَ لِحُدُودِ ٱللَّهِۗ وَبَشِّرِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
(Awo amene alonjezedwa kupeza izi, ndi) omwe amalapa (akalakwa); ochita mapemphero (awo m’njira yoyenera); otamanda Allah kwambiri; ochulukitsa kusala (Swaumu kapena oyendayenda padziko ncholinga chochitira zabwino anthu), owerama, ogwetsa nkhope zawo pansi; olamula zabwino; oletsa zoipa ndi osunga malire a Allah (malamulo Ake). Choncho, auze nkhani yabwino awo amene akhulupirira.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
مَا كَانَ لِلنَّبِيِّ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَن يَسۡتَغۡفِرُواْ لِلۡمُشۡرِكِينَ وَلَوۡ كَانُوٓاْ أُوْلِي قُرۡبَىٰ مِنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُمۡ أَنَّهُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَحِيمِ
Nkosayenera kwa Mneneri ndi amene akhulupirira kuwapemphera chikhululuko opembedza mafano ngakhale atakhala abale awo, pambuyo poonekera kwa iwo kuti iwowo ndi anthu a ku Moto.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَا كَانَ ٱسۡتِغۡفَارُ إِبۡرَٰهِيمَ لِأَبِيهِ إِلَّا عَن مَّوۡعِدَةٖ وَعَدَهَآ إِيَّاهُ فَلَمَّا تَبَيَّنَ لَهُۥٓ أَنَّهُۥ عَدُوّٞ لِّلَّهِ تَبَرَّأَ مِنۡهُۚ إِنَّ إِبۡرَٰهِيمَ لَأَوَّٰهٌ حَلِيمٞ
Ndipo sikudali kupempha chikhululuko kwa Ibrahim kuwapemphera bambo wake koma chifukwa cha lonjezo lomwe adamulonjeza. Koma pamene zidaonekera kwa iye poyera kuti iwo (bambo wake) ndi mdani wa Allah, adadzipatula kwa iwo. Ndithudi, Ibrahim adali wochulukitsa kupempha Allah modzichepetsa, woleza mtima.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيُضِلَّ قَوۡمَۢا بَعۡدَ إِذۡ هَدَىٰهُمۡ حَتَّىٰ يُبَيِّنَ لَهُم مَّا يَتَّقُونَۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٌ
Ndipo Allah sangasokeretse anthu (ndi kupititsa chilango pa iwo) pambuyo powaongolera ku Chisilamu; koma pokhapokha atawonetsa poyera kwa iwo zimene zingafunike kuzipewa. Ndithu Allah Ngodziwa chilichonse.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّ ٱللَّهَ لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُۚ وَمَا لَكُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ مِن وَلِيّٖ وَلَا نَصِيرٖ
Ndithudi, Allah ndi Wake ufumu wakumwamba Ndi pansi. Amapereka moyo ndi imfa. Inu mulibe mtetezi ngakhale mthandizi koma Allah basi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَّقَد تَّابَ ٱللَّهُ عَلَى ٱلنَّبِيِّ وَٱلۡمُهَٰجِرِينَ وَٱلۡأَنصَارِ ٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُوهُ فِي سَاعَةِ ٱلۡعُسۡرَةِ مِنۢ بَعۡدِ مَا كَادَ يَزِيغُ قُلُوبُ فَرِيقٖ مِّنۡهُمۡ ثُمَّ تَابَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّهُۥ بِهِمۡ رَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndithu Allah wafunira zabwino Mtumiki Wake ndi Amuhajirina ndi Answari amene adamtsatira iye (Muhammad {s.a.w}) m’nthawi yamasautso (pokamenyana ndi Aroma pankhondo ya Tabuk), nthawi yomwe mitima ya ena a iwo idatsala pang’ono kupotoka (kutsata machitidwe achikafiri); kenako Allah adawatembenukira ndi chifundo. Ndithu Iye (Allah) kwa iwo Ngodekha, Ngwachisoni chosatha.[213]
[213] Nkhondo ya Tabuk idachitika m’mwezi wa Rajab m’chaka cha chisanu nchinayi chakusamuka. Idali pakati pa Asilamu ndi Aroma. Gulu lankhondo la Chisilamu lomwe lidapita kunkhondo linkatchedwa “Gulu la Masautso” chifukwa kukonzekera kwa nkhondoyi kudachitika m’nyengo ya masautso kwa anthu. Ndipo pamene Mtumiki adafika ku Tabuk, adadza msogoleri wa gulu lankhondo la Aroma wotchedwa Yohane namvana kuti pasakhale nkhondo. M’malo mwake iye adzapereka “Jiziya” (msonkho), motero Mtumiki adabwerera ku Madina. lyi idali nkhondo yake yomaliza.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: At-Taubah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - Die Übersetzung in Chichewa - Khalid Ibrahim Bityala. - Übersetzungen

Übersetzung von Khalid Ibrahim Bitala.

Schließen