Check out the new design

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Eggo e ɗemngal Ciiciiwa - Kaalid Ibrahiima Biitala. * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Aaya: (173) Simoore: Simoore nagge
إِنَّمَا حَرَّمَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡمَيۡتَةَ وَٱلدَّمَ وَلَحۡمَ ٱلۡخِنزِيرِ وَمَآ أُهِلَّ بِهِۦ لِغَيۡرِ ٱللَّهِۖ فَمَنِ ٱضۡطُرَّ غَيۡرَ بَاغٖ وَلَا عَادٖ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ
Iye akukuletsani (kudya) nyama yofa yokha, liwende, nyama yankhumba ndi nyama yodulidwa poikuwira mayina a mafano kusiya Allah. Koma amene wasimidwa (nadya) popanda kuchikhumba choletsedwacho ndi mosapyoza muyeso palibe tchimo kwa iye. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.[13]
[13] Apa Allah akutiuza kuti zinthu zinaizi nzoletsedwa kudya koma ngati munthu atavutika kwambiri ndi njala yofuna kufanayo (ndipo kulibe kopeza chakudya chovomerezeka), akumlola kuzidya pamuyeso wothetsa njalayo, osati mokhutitsa.
Chimene chadulidwa pochitchulira dzina lomwe si la Allah monga nyama zomwe zikuzingidwira kukwanitsa maloto a azimu, kapena yomwe yazingidwa chifukwa chotsilika nyumba, kapena kutsilika midzi, ndi zina zomwe zikuzingidwa kuti satana asawavutitse; zonsezi nzoletsedwa.
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Aaya: (173) Simoore: Simoore nagge
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Eggo e ɗemngal Ciiciiwa - Kaalid Ibrahiima Biitala. - Tippudi firooji ɗii

Eggo mum Khalid Ibrahim Beitala.

Uddude