Kodi mmodzi wa inu angakonde kukhala ndi munda wa mitengo ya kanjedza ndi mphesa womwe pansi pake mitsinje ikuyenda, iye mmenemo napeza dzinthu dzamitundumitundu, numpeza ukalamba uku ali ndi ana ofooka; ndipo kamvuluvulu wa moto naugwera (mundawo), nupseleratu (angazikonde zimenezi)? Umo ndimomwe Allah akukulongosolerani ma Ayah (ndime za mawu Ake) kuti muganizire.
Satana amakuopsezani ndi umphawi ndi kukulamulirani kuchita zoipa (monga umbombo), pomwe Allah akukulonjezani chikhululuko kuchokera kwa Iye ndi ubwino (waukulu ngati mupereka); ndipo Allah ali nazo zambiri, Ngodziwa.[54]
[54] (Ndime 268-271) apa Allah akuwalimbikitsa mtima amene akupereka kuti panthawi iliyonse pamene akupereka Allah adzawaonjezera. Ndipo akuwachenjeza kuti asamamvetsere udyerekezi wa satana umene amauthira m’mitima yawo powauza kuti: “Ngati mupereka, musauka.” Koma Allah akuwauza kuti: “Perekani simusauka. M’malomwake mupeza bwino pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro.”
M’ndime zomwezi Allah wafotokoza za (lonjezo) “naziri” kuti naziri iliyonse imene tikumlonjeza Allah akuidziwa.
Mawu oti “Naziri” nga Chiarabu. M’chichewa akuthandauza kuti, “ndikapeza chakuti ndidzachita chakutichakuti,” “kapena kuti, akachira m’bale wanga ndidzapereka chakutichakuti kwa Allah.”
Mawu anaziriwa siabwino pa malamulo a Chisilamu, ngakhale kuti anthu ambiri amakonda kuchita naziri poganizira kuti akatero Allah awayankha mwachangu namaganiziranso kuti naziri nchinthu chabwino m’Chisilamu pomwe chili chosafunika m’Chisilamu.
Kusafunika kwa naziri m’Chisilamu kuli kotere: Umati: “Allah akandichitira chakutichakuti inenso ndichita chakutichakuti.” Mawu oterewa sali mawu abwino ndiponso akusonyeza kupanda mwambo ndiponso akusonyeza umbombo.
Chifukwa chakuti munthu ofuna kupereka kanthu sanganene kuti: “Muyambe mwandichitira chakuti ndipo ndikupatsani.” Koma ngakhale zili choncho akwaniritsebe malonjezowo. Koma ngati malonjezowo ali pa chinthu choletsedwa asawakwaniritse, ndipo m’malo mwake apereke dipo.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
Sakamakon Bincike:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".