Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Aya: (69) Sura: Suratu Al'ahzab
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ ءَاذَوۡاْ مُوسَىٰ فَبَرَّأَهُ ٱللَّهُ مِمَّا قَالُواْۚ وَكَانَ عِندَ ٱللَّهِ وَجِيهٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musakhale monga amene adamvutitsa Mûsa; koma Allah adamuyeretsa kuzimene ankamnenera. Ndipo iye kwa Allah adali wolemekezeka.[331]
[331] M’ndime iyi, Allah akulangiza Asilamu kuti asamuvutitse Mtumiki ndi kumnenera mawu opanda ulemu monga momwe Ayuda ankamunenera Musa. Ana a Israeli adamunamizira Musa kuti ali ndi khate pathupi lake, kapena kuti ali ndi matenda a mwera (phudzi). Koma Allah adamuyeretsa kuzomwe adali kumunamizirazo. Adamuyeretsa motere monga momwe Bukhari akunenera muhadisi yomwe idalandiridwa kuchokera kwa Abu Huraira (r.a) kuti Mtumiki (s.a.w) adati: Musa adali munthu wamanyazi, ndipo amabisa thupi lake. Khungu lake silimaoneka chifukwa cha manyazi ake. Ndipo adamuvutitsa ena mwa ana a Israeli. Adati: “Sangadzibise motere koma pa khungu lake pali chochititsa manyazi, mwina khate kapena matenda amphepo yamwera (phudzi), kapena matenda ena aliwonse!” Ndipo Allah adafuna kumuyeretsa ku zimene ankamunamizirazo. Tsiku lina Musa adakhala payekha navula nsalu zake naika pa mwala. Kenako adayamba kusamba. Pamene adamaliza kusamba adacheukira komwe adaika nsalu zake kuti azitenge. Adaona mwala ukuthawitsa nsalu zake. Musa adatenga ndodo yake nkumathamangira mwalawo uku akunena: “Nsalu zanga, iwe mwala! Nsalu zanga iwe mwala!’’ Mpaka adadutsa pomwe adakhala akuluakulu a ana a Israeli namuona thupi lake lili losalala kwabasi; lopanda chilema chilichonse. Potero Allah adamuyeretsa ku zomwe ankamunenerazo.
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Aya: (69) Sura: Suratu Al'ahzab
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassarar Maanonin Alurani mai girma zuwa Yaren shishiwa wanda Khalid Ibrahim Bitala kwafi na Shekarar 2020 Miladiyya

Rufewa