Check out the new design

Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fassara da harshan Shishiyo - Khalid Ibrahim Bitala * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Sura: Al'taubah   Aya:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ قَٰتِلُواْ ٱلَّذِينَ يَلُونَكُم مِّنَ ٱلۡكُفَّارِ وَلۡيَجِدُواْ فِيكُمۡ غِلۡظَةٗۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلۡمُتَّقِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Menyani nkhondo ndi awo osakhulupirira amene ali pafupi nanu, ndipo apeze kuuma mtima mwa inu. Ndipo dziwani kuti ndithu Allah ali pamodzi ndi oopa (Iye).
Tafsiran larabci:
وَإِذَا مَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٞ فَمِنۡهُم مَّن يَقُولُ أَيُّكُمۡ زَادَتۡهُ هَٰذِهِۦٓ إِيمَٰنٗاۚ فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ فَزَادَتۡهُمۡ إِيمَٰنٗا وَهُمۡ يَسۡتَبۡشِرُونَ
Ndipo nthawi zonse sura (yatsopano) ikavumbulutsidwa, alipo mwa iwo (achiphamaso) amene akunena: “Ndani mwa inu sura iyi yamuonjezera chikhulupiliro?” Koma amene akhulupirira yawaonjezera chikhulupiliro ndipo iwo akukondwera.
Tafsiran larabci:
وَأَمَّا ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ فَزَادَتۡهُمۡ رِجۡسًا إِلَىٰ رِجۡسِهِمۡ وَمَاتُواْ وَهُمۡ كَٰفِرُونَ
Koma amene ali ndi matenda m’mitima mwawo, yawaonjezera zoipa pamwamba pa zoipa zomwe adali nazo, ndipo akufa ali osakhulupirira.
Tafsiran larabci:
أَوَلَا يَرَوۡنَ أَنَّهُمۡ يُفۡتَنُونَ فِي كُلِّ عَامٖ مَّرَّةً أَوۡ مَرَّتَيۡنِ ثُمَّ لَا يَتُوبُونَ وَلَا هُمۡ يَذَّكَّرُونَ
Kodi saona kuti iwo akuyesedwa mayeso chaka chilichonse kamodzi, kapena kawiri, (kapena kochulukirapo)? Koma salapa (kwa Allah) ndiponso iwo sakumbukira.
Tafsiran larabci:
وَإِذَا مَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٞ نَّظَرَ بَعۡضُهُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٍ هَلۡ يَرَىٰكُم مِّنۡ أَحَدٖ ثُمَّ ٱنصَرَفُواْۚ صَرَفَ ٱللَّهُ قُلُوبَهُم بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَفۡقَهُونَ
Ndipo nthawi iliyonse sura yatsopano ikavumbulutsidwa amayang’anana (iwo achiphamaso kuti athawe, asamvere mawu ake, uku akuuzana pakati pawo): “Kodi alipo amene akukuonani?” Kenako amatembenuka nkuthawa. Tero, Allah waikhotetsa mitima yawo chifukwa chakuti iwo ndi anthu osazindikira.
Tafsiran larabci:
لَقَدۡ جَآءَكُمۡ رَسُولٞ مِّنۡ أَنفُسِكُمۡ عَزِيزٌ عَلَيۡهِ مَا عَنِتُّمۡ حَرِيصٌ عَلَيۡكُم بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ رَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndithu wakudzerani Mtumiki wochokera mwa inu. Zimamudandaulitsa iye zomwe zikukuvutitsani; iye ngoikira mtima pa inu pokufunirani zabwino; ndipo pa okhulupirira ngodekha ndiponso ngwachisoni.
Tafsiran larabci:
فَإِن تَوَلَّوۡاْ فَقُلۡ حَسۡبِيَ ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ عَلَيۡهِ تَوَكَّلۡتُۖ وَهُوَ رَبُّ ٱلۡعَرۡشِ ٱلۡعَظِيمِ
Koma ngati (iwo osakhulupirira) apitiriza kunyoza, nena: “Allah wandikwanira (palibe vuto lingapezeke kuchokera kwa inu) palibe woti nkupembedzedwa koma Iye basi. Ndatsamira kwa Iye. Ndipo Iye, ndi Bwana wa Arsh (mpando wachifumu) yaikulu!”
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Sura: Al'taubah
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fassara da harshan Shishiyo - Khalid Ibrahim Bitala - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassararta Khalid Ibrahim Bitala.

Rufewa