Check out the new design

Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - Çevaca Tercüme - Halid İbrahim Pitala * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Sure: Sûratu'l-Lokmân   Ayet:
أَلَمۡ تَرَوۡاْ أَنَّ ٱللَّهَ سَخَّرَ لَكُم مَّا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَأَسۡبَغَ عَلَيۡكُمۡ نِعَمَهُۥ ظَٰهِرَةٗ وَبَاطِنَةٗۗ وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يُجَٰدِلُ فِي ٱللَّهِ بِغَيۡرِ عِلۡمٖ وَلَا هُدٗى وَلَا كِتَٰبٖ مُّنِيرٖ
Kodi simuona kuti Allah adakugonjetserani zakumwamba ndi zapansi ndi kukukwaniritsirani chisomo Chake, choonekera ndi chobisika? Ndipo alipo ena mwa anthu amene akukangana pa za Allah popanda kuzindikira ngakhale chiongoko, ngakhalenso buku lounika.[313]
[313] E inu anthu! Ndithu Allah Wolemekezeka adakupangirani zonse zili kumwamba monga dzuwa mwezi, nyenyezi kuti muthandizike nazo. Ndipo adakupangirani zonse zomwe zili m’nthaka monga mapiri, mitengo, zipatso, mitsinje, ndi zina zambiri zosawerengeka kuti zonsezi zigonjere inu ndikuti muthandizike nazo.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱتَّبِعُواْ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ قَالُواْ بَلۡ نَتَّبِعُ مَا وَجَدۡنَا عَلَيۡهِ ءَابَآءَنَآۚ أَوَلَوۡ كَانَ ٱلشَّيۡطَٰنُ يَدۡعُوهُمۡ إِلَىٰ عَذَابِ ٱلسَّعِيرِ
Ndipo akauzidwa kuti: “Tsatani zimene Allah watsitsa.” Akunena: “Koma tikutsata zimene tidawapeza nazo makolo athu.” Kodi ngakhale kuti satana akuwaitanira ku chilango cha Moto (woyaka, adzatsatirabe)?
Arapça tefsirler:
۞ وَمَن يُسۡلِمۡ وَجۡهَهُۥٓ إِلَى ٱللَّهِ وَهُوَ مُحۡسِنٞ فَقَدِ ٱسۡتَمۡسَكَ بِٱلۡعُرۡوَةِ ٱلۡوُثۡقَىٰۗ وَإِلَى ٱللَّهِ عَٰقِبَةُ ٱلۡأُمُورِ
Ndipo amene akupereka nkhope yake kwa Allah (amene akugonjera Allah kwatunthu) ali ochita zabwino, ndiye kuti wagwira chogwilira cholimba. Ndipo mapeto a zinthu zonse nkwa Allah basi.
Arapça tefsirler:
وَمَن كَفَرَ فَلَا يَحۡزُنكَ كُفۡرُهُۥٓۚ إِلَيۡنَا مَرۡجِعُهُمۡ فَنُنَبِّئُهُم بِمَا عَمِلُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ
Koma amene sadakhulupirire (Allah ndi mtima wake) choncho kusakudandaulitse kusakhulupirira kwake. Kobwerera kwawo nkwa Ife basi. Kumeneko tidzawauza zimene adachita. Ndithu Allah Ngodziwa zonse zam’zifuwa.
Arapça tefsirler:
نُمَتِّعُهُمۡ قَلِيلٗا ثُمَّ نَضۡطَرُّهُمۡ إِلَىٰ عَذَابٍ غَلِيظٖ
Tikuwasangalatsa pang’ono (apo pa dziko lapansi). Kenako tidzawakankhira ku chilango chokhwima.
Arapça tefsirler:
وَلَئِن سَأَلۡتَهُم مَّنۡ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ لَيَقُولُنَّ ٱللَّهُۚ قُلِ ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِۚ بَلۡ أَكۡثَرُهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo ukawafunsa: “Ndani adalenga thambo ndi nthaka?” Ndithu anena: “Ndi Allah.” Nena: “Kutamandidwa konse nkwa Allah.” Koma ambiri a iwo sadziwa.
Arapça tefsirler:
لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ إِنَّ ٱللَّهَ هُوَ ٱلۡغَنِيُّ ٱلۡحَمِيدُ
Zonse zakumwamba ndi za pansi, nza Allah. Ndithu Allah Ngwachikwanekwane, Ngotamandidwa.
Arapça tefsirler:
وَلَوۡ أَنَّمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ مِن شَجَرَةٍ أَقۡلَٰمٞ وَٱلۡبَحۡرُ يَمُدُّهُۥ مِنۢ بَعۡدِهِۦ سَبۡعَةُ أَبۡحُرٖ مَّا نَفِدَتۡ كَلِمَٰتُ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo ndithu ngakhale mitengo yonse ili m’nthaka ikadakhala zolembera, ndipo nyanja (nkukhala inki), ndipo pambuyo pake ndikuionjezeranso (madzi ake) ndi nyanja zisanu ndi ziwiri, mawu a Allah sakadatha. Ndithu Allah Ngwamphamvu, Wanzeru zakuya.[314]
[314] Ndime iyi ikufotokoza kuti mawu a Allah ngochuluka. Mitengo yonse pa dziko lapansi itakhala ngati mapensulo ndipo nyanja zonse pa dziko lapansi, nkuwonjezanso nyanja zina, zikadakhala inki, zonse zikadatha koma mawu a Allah alipobe.
Arapça tefsirler:
مَّا خَلۡقُكُمۡ وَلَا بَعۡثُكُمۡ إِلَّا كَنَفۡسٖ وَٰحِدَةٍۚ إِنَّ ٱللَّهَ سَمِيعُۢ بَصِيرٌ
Kulengedwa kwanu, ngakhale kuukitsidwa kwanu m’manda sikuli kanthu koma kuli ngati (kulenga kapena kuukitsa kwa) munthu mmodzi. (Palibe chokanika kwa Allah). Ndithu Allah Ngwakumva, Ngopenya chilichonse.
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Sure: Sûratu'l-Lokmân
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - Çevaca Tercüme - Halid İbrahim Pitala - Mealler fihristi

Halid İbrahim Pitala Tercümesi.

Kapat