Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Sure: Sûratu'n-Nisâ   Ayet:

Sûratu'n-Nisâ

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ ٱتَّقُواْ رَبَّكُمُ ٱلَّذِي خَلَقَكُم مِّن نَّفۡسٖ وَٰحِدَةٖ وَخَلَقَ مِنۡهَا زَوۡجَهَا وَبَثَّ مِنۡهُمَا رِجَالٗا كَثِيرٗا وَنِسَآءٗۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ ٱلَّذِي تَسَآءَلُونَ بِهِۦ وَٱلۡأَرۡحَامَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَيۡكُمۡ رَقِيبٗا
E inu anthu! Opani Mbuye wanu yemwe adakulengani kuchokera mwa munthu mmodzi (Adam) ndipo adalenga mmenemo mkazi wake (Hawa), ndipo adafalitsa amuna ndi akazi ambiri kuchokera mwa awiriwo. Ndipo opani Allah yemwe kupyolera mwa Iye mumapemphana. Ndipo (sungani) chibale. Ndithudi Allah Ndimyang’aniri pa inu (akuona chilichonse chimene muchita).[105]
[105] Ndime iyi ikulimbikitsa za kuopa Allah ndi kumulemekeza potsatira malamulo ake ndi kupewa zomwe Iye waletsa. Iye ndi amene adakulenga. Ndiyemwenso adalenga zonse zimene iwe adakulengera. Ngakhale iwe amene utafuna chithandizo kwa anzako umampempha ponena kuti: ‘‘Ndikukupempha m’dzina la Allah kuti undichitire chakuti.” Izi umachita poona kuti iye adzalemekeza dzina la Allah, ndipo adzakwaniritsa chomwe ukufunacho. Koma nanga bwanji ukuchita zimene Allah waletsa? Bwanji sukulemekeza lamulo lake pomwe iwe ukufuna kuti anthu achite zomwe sukuchita. Apa akutiuzanso kuti Allah akuona chilichonse chimene anthu ake akuchita, ngakhale chikhale chochepa chotani.
Arapça tefsirler:
وَءَاتُواْ ٱلۡيَتَٰمَىٰٓ أَمۡوَٰلَهُمۡۖ وَلَا تَتَبَدَّلُواْ ٱلۡخَبِيثَ بِٱلطَّيِّبِۖ وَلَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَهُمۡ إِلَىٰٓ أَمۡوَٰلِكُمۡۚ إِنَّهُۥ كَانَ حُوبٗا كَبِيرٗا
Ndipo apatseni ana amasiye chuma chawo; musasinthanitse choipa ndi chabwino. Ndipo musadye chuma chawo pochiphatikiza ndi chuma chanu. Ndithudi, (zonsezo) ndiuchimo waukulu.
Arapça tefsirler:
وَإِنۡ خِفۡتُمۡ أَلَّا تُقۡسِطُواْ فِي ٱلۡيَتَٰمَىٰ فَٱنكِحُواْ مَا طَابَ لَكُم مِّنَ ٱلنِّسَآءِ مَثۡنَىٰ وَثُلَٰثَ وَرُبَٰعَۖ فَإِنۡ خِفۡتُمۡ أَلَّا تَعۡدِلُواْ فَوَٰحِدَةً أَوۡ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡۚ ذَٰلِكَ أَدۡنَىٰٓ أَلَّا تَعُولُواْ
Ngati mwaopa kuti simungachite chilungamo pa amasiye (opaninso kusawachitira chilungamo akazi pamitala), choncho kwatirani amene mukuwafuna mwa akazi; awiri, kapena atatu, kapena anayi (basi). Koma ngati mukuopa kuti simungathe kuchita chilungamo, (kwatirani) mmodzi basi kapena amene manja anu akumanja adapeza (mdzakazi). Kutero kudzakuchititsani kuti musapendekere (kumbali yosalungama).[106]
[106] Maulama onse a malamulo a Chisilamu adamvana kuti ndime iyi yaika malire amitala yomwe munthu akhoza kukwatira. Ndipo ikuletsa kukwatira akazi opyola anayi pa nthawi imodzi.
Arapça tefsirler:
وَءَاتُواْ ٱلنِّسَآءَ صَدُقَٰتِهِنَّ نِحۡلَةٗۚ فَإِن طِبۡنَ لَكُمۡ عَن شَيۡءٖ مِّنۡهُ نَفۡسٗا فَكُلُوهُ هَنِيٓـٔٗا مَّرِيٓـٔٗا
Ndipo akazi apatseni chiwongo chawo monga mphatso. Koma (akazi anuwo) ngati atakupatsani mokoma mtima chilichonse (m’chiwongocho), idyani mokondwa ndi mothandizika nacho.[107]
[107] Kumuitanitsa chiwongo mkazi wako chimene udampatsa kapena kumlipitsa ndalama iliyonse, zotere nzosaloledwa. Koma ngati iye mwini atakugawira mokoma mtima kachinthu kam’chiwongocho landira usamkanire. Monga iwe umampatsa, iyenso akhoza kukupatsa.
Arapça tefsirler:
وَلَا تُؤۡتُواْ ٱلسُّفَهَآءَ أَمۡوَٰلَكُمُ ٱلَّتِي جَعَلَ ٱللَّهُ لَكُمۡ قِيَٰمٗا وَٱرۡزُقُوهُمۡ فِيهَا وَٱكۡسُوهُمۡ وَقُولُواْ لَهُمۡ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗا
Ozerezeka musawapatse chuma chanu chomwe Allah wachichita kukhala cholimbitsa matupi anu ndi moyo wanu. Koma adyetseni nacho ndikuwaveka nacho ndikuwauza mawu abwino (monga kuti: Mukadzakula ndikukhala olungama, tidzakupatsani chuma chanu).[108]
[108] Ayang’aniri a ana amasiye, monga momwe awauzira kuti asawachenjelere ana amasiye koma kuti awapatse chuma chawo mokwanira, apa akuwauzanso kuti apitirize kuyang’anira chuma cha ana amasiyewo. Asawapatse pomwe sali ozindikira zinthu, ali ofooka m’maganizo pomwe sakuzindikira kufunika kwa chuma kuopa kuti angasakaze chumacho. Tero asawapatse ngakhale misinkhu yawo ili yaikulu. Koma apitirize kuwasungira chumacho ndi kumawauza mawu abwino ponena kuti: “Mpaka pano ndikuona kuti mwanokha simungathe kuchiyendetsa bwino chuma chanu. Tero ndiloleni ndikusungirenibe mpaka nthawi yochepa kutsogoloku. Ndikadzaona kuti nzeru zakhazikika apo mpomwe ndidzakupatsani chumachi.”
Arapça tefsirler:
وَٱبۡتَلُواْ ٱلۡيَتَٰمَىٰ حَتَّىٰٓ إِذَا بَلَغُواْ ٱلنِّكَاحَ فَإِنۡ ءَانَسۡتُم مِّنۡهُمۡ رُشۡدٗا فَٱدۡفَعُوٓاْ إِلَيۡهِمۡ أَمۡوَٰلَهُمۡۖ وَلَا تَأۡكُلُوهَآ إِسۡرَافٗا وَبِدَارًا أَن يَكۡبَرُواْۚ وَمَن كَانَ غَنِيّٗا فَلۡيَسۡتَعۡفِفۡۖ وَمَن كَانَ فَقِيرٗا فَلۡيَأۡكُلۡ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ فَإِذَا دَفَعۡتُمۡ إِلَيۡهِمۡ أَمۡوَٰلَهُمۡ فَأَشۡهِدُواْ عَلَيۡهِمۡۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ حَسِيبٗا
Ayeseni amasiye (akayandikira kukula nsinkhu kuti muone kuti atha kuchita ntchito yabwino ndi chuma chawo mukawapatsa), kufikira atafika nthawi yokwatira/kukwatiwa. Ndipo ngati mutawaona kuti ali ndi nzeru zabwino, apatseni chuma chawo. Musachidye mosasamala ndi mwachangu poopa kuti angakule. Ndipo amene ali opeza bwino adziletse (kulandira mphoto yolelera ana amasiyewo). Koma amene ali wosauka adye mwa ubwino (osati moononga). Ndipo pamene mukuwapatsa chuma chawo, funani mboni (zoonelera kuperekedwa kwa chumacho). Ndipo Allah ali Wokwana kukhala Muwelengeri (ndi Woyang’anira).[109]
[109] Komatu akhale akumuyesayesa wamasiyeyo pomusiira kuti nthawi zina aziyendetsapo yekha chumacho kuti aphunzire kasamalidwe kake. Akaona kuti akukhoza, ampatse asamuchedwetsere mwadala.
Arapça tefsirler:
لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ مِمَّا قَلَّ مِنۡهُ أَوۡ كَثُرَۚ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا
Amuna m’chuma chimene makolo ndi achibale asiya ali ndi gawo. Naonso akazi ali ndigawo m’chuma chimene asiya makolo ndi achibale (chapafupi), ngakhale chitakhala chochepa kapena chochuluka ndigawo logawidwa (ndi Allah)[110]
[110] Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena kuti m’Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi. Mwamuna ali ndi udindo woyang’anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake. Koma mkazi alibe udindo woyang’anira mwamuna wake. Ndiponso alibe udindo woyang’anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo woyang’anira ana ake.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا حَضَرَ ٱلۡقِسۡمَةَ أُوْلُواْ ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينُ فَٱرۡزُقُوهُم مِّنۡهُ وَقُولُواْ لَهُمۡ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗا
Ndipo panthawi yogawa, ngati angabwere achibale, amasiye ndi osauka (omwe alibe gawo pa chumacho), apatseniko kanthu ndi kunena nawo mawu abwino.[111]
[111] Chuma nchinthu chimene chimachotsa moyo wa munthu mmalomwake, makamaka ngati chikupezeka m’njira yaulere yosachivutikira, monga chilili chuma chamasiye. Choncho amene alibepo gawo pa chumacho amangoti diso tong’o, kusilira. Ndipo nchifukwa chake Allah apa akunena kuti pogawa chuma chamasiyecho ngati achibale atabwerapo omwe alibepo gawo pa chumacho, awapatseko kachinthu kochepa ndi kuwapepesa kuti chomwe awapatsacho nchochepa.
Arapça tefsirler:
وَلۡيَخۡشَ ٱلَّذِينَ لَوۡ تَرَكُواْ مِنۡ خَلۡفِهِمۡ ذُرِّيَّةٗ ضِعَٰفًا خَافُواْ عَلَيۡهِمۡ فَلۡيَتَّقُواْ ٱللَّهَ وَلۡيَقُولُواْ قَوۡلٗا سَدِيدًا
Ndipo (wowasiirawo) aope (kusachita chilungamo), kuti naonso ngati atasiya ana awo ofooka pambuyo, akadawaopera (kuchenjeleredwa). Choncho aope Allah ndipo anene mawu olingana (kwa ana amasiyewo).
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَأۡكُلُونَ أَمۡوَٰلَ ٱلۡيَتَٰمَىٰ ظُلۡمًا إِنَّمَا يَأۡكُلُونَ فِي بُطُونِهِمۡ نَارٗاۖ وَسَيَصۡلَوۡنَ سَعِيرٗا
Ndithu amene akudya churna cha ana amasiye mopondereza, akudya ndi kuthira moto m’mimba zawo. Ndipo adzalowa ku Moto woyaka!
Arapça tefsirler:
يُوصِيكُمُ ٱللَّهُ فِيٓ أَوۡلَٰدِكُمۡۖ لِلذَّكَرِ مِثۡلُ حَظِّ ٱلۡأُنثَيَيۡنِۚ فَإِن كُنَّ نِسَآءٗ فَوۡقَ ٱثۡنَتَيۡنِ فَلَهُنَّ ثُلُثَا مَا تَرَكَۖ وَإِن كَانَتۡ وَٰحِدَةٗ فَلَهَا ٱلنِّصۡفُۚ وَلِأَبَوَيۡهِ لِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُ مِمَّا تَرَكَ إِن كَانَ لَهُۥ وَلَدٞۚ فَإِن لَّمۡ يَكُن لَّهُۥ وَلَدٞ وَوَرِثَهُۥٓ أَبَوَاهُ فَلِأُمِّهِ ٱلثُّلُثُۚ فَإِن كَانَ لَهُۥٓ إِخۡوَةٞ فَلِأُمِّهِ ٱلسُّدُسُۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِي بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍۗ ءَابَآؤُكُمۡ وَأَبۡنَآؤُكُمۡ لَا تَدۡرُونَ أَيُّهُمۡ أَقۡرَبُ لَكُمۡ نَفۡعٗاۚ فَرِيضَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Allah akukulamulani za ana anu achimuna apate gawo lolingana ndi gawo la akazi awiri. Ngati akaziwo ali (opitilira) awiri, ndiye kuti adzalandira zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu (2/3) za (chumacho) chimene wasiya (womwalira), ngati mwana wamkazi ndi mmodzi, apatsidwe gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2), naonso makolo ake awiri aliyense wa iwo alandile gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achuma chosiidwacho, ngati (womwalirayo) wasiya mwana (kapena mdzukulu). Koma ngati sadasiye mwana, ndipo makolo ake awiri ndiwo awasiira, ndiye kuti mayi wake alandire gawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho, (ndipo bambo alandire 2/3). Ngati wakufayo wasiya abale, ndiye kuti mayi wake apeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achumacho. (Kugawa chumaku kuchitike) atachotsapo chimene iye adalamulira kuti adzachipereke kwakutikwakuti, kapena kulipira ngongole (zake). Atate anu ndi ana anu, simudziwa inu kuti ndani mwa iwo amene ali ndi chithandizo chapafupi kwa inu. Amenewa ndi malamulo omwe akhazikitsidwa ndi Allah. Ndithudi, Allah ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.[112]
[112] Apa akufotokoza za kagawidwe ka chuma chamasiye (mirath).
a) Ngati munthu wamwalira nkusiya ana amuna ndi akazi tero mwana wamwamuna adzapeza magawo awiri ndipo wamkazi adzapeza gawo limodzi.
b) Munthu akafa nkusiya ana akazi okha, awiri kapena ochulukirapo, anawo adzatenga magawo awiri achumacho. Ndipo onsewo alandire mofanana. Pasapezeke wotenga zochuluka kuposa wina.
Tsono gawo lomwe latsala lidzaperekedwa kwa ena oti awagawire ngati alipo. Ngati palibe, ndiye kuti gawolo lidzaperekedwanso kwa ana akaziwo.
N.B Magawo awiri m’magawo atatu (2/3), apa akutanthauza kuti chuma chonsecho amachigawa m’magawo atatu ofanana. Ndipo akaziwo nkulandira magawo awiri mwa magawo atatuwo.
c) Ngati munthu atamwalira nkusiya mwana mmodzi wamkazi, ndiye kuti chumacho achigawe magawo awiri ofanana. Gawo limodzi mwa magawo awiri aja alipereke kwa mwana wamkaziyo. Ndipo gawo lotsalalo alipereke kwa ena ofunika kuwagawira ngati alipo. Ngati palibe, aliperekenso kwa mwana yemweyo. Lamulo la adzukulu likufanana ndi lamulo la ana ngati wakufayo adalibe ana koma adzukulu ake okha.
d) Munthu akafa nkusiya ana ndi makolo ake, (tate ndi mayi), tero tate adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) a chumacho. Nayenso mayi adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo chuma chotsalacho adzalandira ndi ana kapena adzukulu a muntnu wakufayo.
e) Munthu akafa nkusiya tate wake ndi mayi wake basi, popanda ana ndi adzukulu choncho apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo atatu a chumacho. Ndipo tate adzatenga magawo awiri.
f) Munthu akafa nkusiya mayi wake yekha ndi abale ake obadwa nawo kwa mayi ndi bambo mmodzi, kapena akumbali ya kwabambo okha kapena akumbali yamayi okha, apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi a chumacho. Anthu oyenera kuwagawira chuma chamasiye asawagawire msanga chumacho mpaka ngongole zonse za wakufayo atazibweza. Ndiponso mpaka apereke chilawo (wasiya) chomwe wakufayo adanena kuti chidzachitike. Owagawira chumawo asakhale anthu osusuka ndi chumacho. choyamba aonetsetse kuti izi zonse zakwaniritsidwa. Komatu chilawocho chisapyole pagawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho. Chikapyolera pamenepa ndiye kuti choonjezerapocho sichivomerezedwa.
Arapça tefsirler:
۞ وَلَكُمۡ نِصۡفُ مَا تَرَكَ أَزۡوَٰجُكُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّهُنَّ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَهُنَّ وَلَدٞ فَلَكُمُ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡنَۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِينَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۚ وَلَهُنَّ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡتُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّكُمۡ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَكُمۡ وَلَدٞ فَلَهُنَّ ٱلثُّمُنُ مِمَّا تَرَكۡتُمۚ مِّنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ تُوصُونَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۗ وَإِن كَانَ رَجُلٞ يُورَثُ كَلَٰلَةً أَوِ ٱمۡرَأَةٞ وَلَهُۥٓ أَخٌ أَوۡ أُخۡتٞ فَلِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُۚ فَإِن كَانُوٓاْ أَكۡثَرَ مِن ذَٰلِكَ فَهُمۡ شُرَكَآءُ فِي ٱلثُّلُثِۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصَىٰ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍ غَيۡرَ مُضَآرّٖۚ وَصِيَّةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَلِيمٞ
Inunso mupata gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2) achuma chimene akazi anu asiya ngati alibe mwana (kapena mdzukulu), ngati asiya mwana ndiye kuti inu mupata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) achuma chosiidwacho mutachotsapo zomwe adalamula kuti zipite kwakutikwakuti kapena ngongole zake, naonso akazi anu apata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) pa chuma chomwe mwasiya, ngati mulibe mwana (ndi mdzukulu). Koma ngati mwasiya mwana (ndi mdzukulu), (akaziwo) apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi atatu (1/8) pa chuma chomwe mwasiya mutachotsapo chomwe mudanena kuti chipite kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole (zanu). Ngati mwamuna kapena mkazi alowedwa m’malo pachuma pomwe alibe mwana (ndi mdzukulu) ngakhale makolo awiri, koma ali naye m’bale wake (wakuchikazi) kapena mlongo wake (wakuchikazinso) aliyense wa iwo apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo ngati ali ochulukirapo, ndiye kuti agawirana gawo limodzi m’magawo atatu (1/3) a chumacho pambuyo pochotsapo chomwe chidanenedwa kuti chipita kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole, popanda kupereka mavuto. Awa ndi malamulo ofunika omwe achokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri (pokhazikitsa malamulo); Woleza (pa akapolo Ake).[113]
[113] Apa akufotokoza mmene anthu ena angawagawireko chuma chamasiye.
a) Ngati atafa mkazi nkusiya mwamuna wake yekha popanda kusiya ana kapena adzukulu, mwamunayo alandire gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2) a chuma chomwe wasiya mkazi wakecho.
b) Akafa mkazi nkusiya mwamuna ndi nnwana wake kapena mdzukulu wake apa ndiye kuti mwamunayo adzalandira (1/4) gawo limodzi mwa magawo anayi achumacho.
c) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake popanda mwana kapena mdzukulu wake ndiye kuti mkaziyo adzalandira (1/4) gawo limodzi mwamagawo anayi achuma cha mwamuna wakecho. Ndipo chotsalacho achipereke kwa ena ofunika kuwagawira.
d) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake ndi mwana wake kapena mdzukulu wake, apa mkazi alandire (1/8) gawo limodzi mwa magawo asanu ndi atatu a chuma cha mwamunayo.
e) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena zidzukulu ndi makolo, koma nkusiya m’bale mmodzi wamwamuna kapena wamkazi wakumbali ya mayi, apa ndiye kuti m’baleyo adzalandira (1/6) gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi a chumacho. Ndipo chotsalacho adzawagawira ena oyenera kuwagawira ngati alipo. Koma ngati palibe ndiye kuti m’baleyo adzatenganso chotsalacho.
f) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena adzukulu ndi makolo, koma wasiya abale akumbali yamayi, amuna kapena akazi, apa ndiye kuti abalewa adzalandira (1/3) gawo limodzi mwa magawo atatu achuma cha womwalirayo. Ndipo adzagawana pakati pawo mofanana amuna ndi akazi omwe.
Arapça tefsirler:
تِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِۚ وَمَن يُطِعِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ يُدۡخِلۡهُ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ وَذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Amenewo ndiwo malire a Allah; (musawalumphe). Ndipo amene angamvere Allah ndi Mtumiki Wake adzamulowetsa m’Minda yomwe pansi (ndi patsogolo pake) mitsinje ikuyenda. Adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَعۡصِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَيَتَعَدَّ حُدُودَهُۥ يُدۡخِلۡهُ نَارًا خَٰلِدٗا فِيهَا وَلَهُۥ عَذَابٞ مُّهِينٞ
Koma amene anganyoze Allah ndi Mtumiki Wake, ndi kulumpha malire ake, (Allah) adzamulowetsa ku Moto; nadzakhala m’menemo nthawi yaitali. Ndipo adzapeza chilango chosambula.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّٰتِي يَأۡتِينَ ٱلۡفَٰحِشَةَ مِن نِّسَآئِكُمۡ فَٱسۡتَشۡهِدُواْ عَلَيۡهِنَّ أَرۡبَعَةٗ مِّنكُمۡۖ فَإِن شَهِدُواْ فَأَمۡسِكُوهُنَّ فِي ٱلۡبُيُوتِ حَتَّىٰ يَتَوَفَّىٰهُنَّ ٱلۡمَوۡتُ أَوۡ يَجۡعَلَ ٱللَّهُ لَهُنَّ سَبِيلٗا
Ndipo omwe achite cha uve (chigololo) mwa akazi anu, afunireni mboni zinayi za mwa inu zoikira umboni pa iwo. Ngati ataikira umboni (kuti achitadi cha uvecho), atsekereni m’nyumba kufikira imfa idzawapeze, kapena Allah adzawaikire njira ina (monga kuphedwa).[114]
[114] (Ndime 15-16) Izi ndi ndime zimene zikufotokoza za zilango zolanga nazo awa:-
a) Akazi amene amachitana ukwati akazi okhaokha
b) Amuna amene amachitana ukwati amuna okhaokha
c) Akazi ndi amuna amene akuchitana ukwati pamalo achabe a pathupi. Zinthu zonsezi nzoipa kwabasi.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّذَانِ يَأۡتِيَٰنِهَا مِنكُمۡ فَـَٔاذُوهُمَاۖ فَإِن تَابَا وَأَصۡلَحَا فَأَعۡرِضُواْ عَنۡهُمَآۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ تَوَّابٗا رَّحِيمًا
Ndipo amuna awiri mwa inu amene akuchita zauve (monga kuchitana ukwati amuna okhaokha ‘matanyula’), akhaulitseni (powalanga). Tsono ngati atalapa ndikukonza bwino (mkhalidwe wawowo) asiyeni. Ndithudi, Allah Ngolandira kulapa, ndiponso Ngwachisoni chambiri.
Arapça tefsirler:
إِنَّمَا ٱلتَّوۡبَةُ عَلَى ٱللَّهِ لِلَّذِينَ يَعۡمَلُونَ ٱلسُّوٓءَ بِجَهَٰلَةٖ ثُمَّ يَتُوبُونَ مِن قَرِيبٖ فَأُوْلَٰٓئِكَ يَتُوبُ ٱللَّهُ عَلَيۡهِمۡۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Ndithudi kulapa kovomerezeka ndi Allah nkwa omwe amachita zoipa mwa umbuli kenako nkulapa mwachangu. Amenewo ndiomwe Allah amawalandira kulapa kwawo. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru zakuya.[115]
[115] Ndime iyi ikusonyeza kuti Allah amalandira kulapa kuchokera kwa aliyense amene walapa. Komatu kuti kulapako kuvomerezeke, pafunika zinthu ziwiri:-
a) Akachita uchimo alape mwachangu. Osati azingopitiriza kulakwako mpaka akadzaona kuti ali pafupi kufa ndiye nkuyamba kulapa, zoterezi iyayi.
b) Uchimowo ukhale kuti adauchita chifukwa cha umbuli. Apa zikutanthauza kuti panthawiyo iye adadzazidwa ndi zilakolako za uchimo ndipo zidamchititsa kuti achimwe. Koma osati tchimolo likhale lolichita tsiku ndi tsiku popanda kulabadira chilichonse. Kulapa kwa uchimo wotero Allah sangakulandire. Ndipo mmalo mwake akamulanga ndi chilango chaukali.
Arapça tefsirler:
وَلَيۡسَتِ ٱلتَّوۡبَةُ لِلَّذِينَ يَعۡمَلُونَ ٱلسَّيِّـَٔاتِ حَتَّىٰٓ إِذَا حَضَرَ أَحَدَهُمُ ٱلۡمَوۡتُ قَالَ إِنِّي تُبۡتُ ٱلۡـَٰٔنَ وَلَا ٱلَّذِينَ يَمُوتُونَ وَهُمۡ كُفَّارٌۚ أُوْلَٰٓئِكَ أَعۡتَدۡنَا لَهُمۡ عَذَابًا أَلِيمٗا
Kulapa sikungalandiridwe pa omwe akuchita zoipa mpaka imfa kumfikira m’modzi wa iwo (pamenepo) nkunena: “Ndithudi ine ndikulapa tsopano.” Ngakhalenso pa omwe akufa ali osakhulupirira. Iwo tawakonzera chilango chopweteka.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا يَحِلُّ لَكُمۡ أَن تَرِثُواْ ٱلنِّسَآءَ كَرۡهٗاۖ وَلَا تَعۡضُلُوهُنَّ لِتَذۡهَبُواْ بِبَعۡضِ مَآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ إِلَّآ أَن يَأۡتِينَ بِفَٰحِشَةٖ مُّبَيِّنَةٖۚ وَعَاشِرُوهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ فَإِن كَرِهۡتُمُوهُنَّ فَعَسَىٰٓ أَن تَكۡرَهُواْ شَيۡـٔٗا وَيَجۡعَلَ ٱللَّهُ فِيهِ خَيۡرٗا كَثِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Sikovomerezedwa kwa inu kuwalowa chokolo akazi mowakakamiza. Ndipo musawaletse (kukwatiwa ndi amuna ena) ndi cholinga choti muwalande zina mwa zomwe mudawapatsa, (nkosaloledwa kutero) kupatula ngati atachita choipa choonekera. Ndipo khalani nawo mwa ubwino. Ngati mutawada (musalekane nawo), mwina mungade chinthu chomwe Allah waika zabwino zambiri mkati mwake.[116]
[116] Nthawi ya umbuli, chikhalidwe cha Arabu chidali chonchi:- Tate wa munthu akamwalira ana ake amamlowera chokolo akazi ake omwe sadabereke anawo. Mwana aliyense amalowa chokolo mwa mkazi watate wake yemwe sadali mayi wake wom’bala.
a) Akafuna kumkwatira adali kumtenga.
b) Ndipo akafuna kumkwatitsa kwa mwamuna wina, amamlamula ndalama mwamunayo iye natenga ndalamazo.
c) Kapena amangomuvutitsavutitsa kuti akafuna adziombole yekha pomlipira ndalama mwanayo.
d) Kapena amangommanga kuti asakwatiwenso mpaka imfa yake. Choncho apa Allah akuletsa machitidwe oipawa.
Arapça tefsirler:
وَإِنۡ أَرَدتُّمُ ٱسۡتِبۡدَالَ زَوۡجٖ مَّكَانَ زَوۡجٖ وَءَاتَيۡتُمۡ إِحۡدَىٰهُنَّ قِنطَارٗا فَلَا تَأۡخُذُواْ مِنۡهُ شَيۡـًٔاۚ أَتَأۡخُذُونَهُۥ بُهۡتَٰنٗا وَإِثۡمٗا مُّبِينٗا
Ndipo ngati mufuna kusintha mkazi wina m’malo mwa wina (pokwatira wina kusiya wakale) pomwe mmodzi wa iwo (woyambayo) mudampatsa milumilu ya chuma, musatenge (kulanda) chilichonse. Kodi mungachitenge mwa chinyengo ndi uchimo woonekera?
Arapça tefsirler:
وَكَيۡفَ تَأۡخُذُونَهُۥ وَقَدۡ أَفۡضَىٰ بَعۡضُكُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٖ وَأَخَذۡنَ مِنكُم مِّيثَٰقًا غَلِيظٗا
Kodi mungachitenge bwanji pomwe mudalowana wina ndi mnzake, ndipo (akazi) adalandira kwa inu chipangano cholimba?
Arapça tefsirler:
وَلَا تَنكِحُواْ مَا نَكَحَ ءَابَآؤُكُم مِّنَ ٱلنِّسَآءِ إِلَّا مَا قَدۡ سَلَفَۚ إِنَّهُۥ كَانَ فَٰحِشَةٗ وَمَقۡتٗا وَسَآءَ سَبِيلًا
Ndipo musakwatire akazi amene adakwatiwapo ndi atate anu, kupatula zomwe zidapita, (musabwerezenso kuzichita). Ndithudi, chinthu ichi nchauve ndipo nchodedwa ndiponso ndinjira yoipa.[117]
[117] Ndime iyi ndi zinzake zotsatira zikufotokoza za akazi omwe ngoletsedwa kuwakwatira pa Shariya ya Chisilamu. Ena mwa akaziwo ndi awa:-
1) Munthu sangakwatire mkazi yemwe bambo wake adamkwatirapo kapena yemwe adakwatiwapo ndi gogo wake wakuchimuna kapena kuchikazi. Koma osati amene adasiidwa ndimalume ake kapena m’bale watate wake. Amenewa akhoza kuwakwatira.
2) Mayi wako yemwe adakubereka ndi mayi wamayi wako.
3) Mwana wako wodziberekera wekha, kapena mwana amene mwana wako adabereka.
4) Tate wako wamkazi (zakhali) ndi alongo agogo ako.
5) Mayi wako wamng’ono (m’bale wamayi wako) ndi m’bale wamkazi wa agogo ako akuchikazi.
6) Mwana wa m’bale wako wobadwa naye bambo ndi mayi mmodzi kapena wobadwa naye mayi mmodzi kapena bambo mmodzi ndi ana onse akazi oberekedwa ndi mwanayo.
7) Mwana wamkazi wa mlongo wako (mfumukazi) wamayi ndi bambo mmodzi kapena wakumbali yabambo yokha kapenanso wakumbali yamayi yokha.
8) Mkazi yemwe adakuyamwitsapo ndi mayi ake amkaziyo kapena omwe adamuyamwitsaponso iye.
9) Mkazi yemwe unayamwa naye bere limodzi.
10) Mayi wamkazi wanu.
Arapça tefsirler:
حُرِّمَتۡ عَلَيۡكُمۡ أُمَّهَٰتُكُمۡ وَبَنَاتُكُمۡ وَأَخَوَٰتُكُمۡ وَعَمَّٰتُكُمۡ وَخَٰلَٰتُكُمۡ وَبَنَاتُ ٱلۡأَخِ وَبَنَاتُ ٱلۡأُخۡتِ وَأُمَّهَٰتُكُمُ ٱلَّٰتِيٓ أَرۡضَعۡنَكُمۡ وَأَخَوَٰتُكُم مِّنَ ٱلرَّضَٰعَةِ وَأُمَّهَٰتُ نِسَآئِكُمۡ وَرَبَٰٓئِبُكُمُ ٱلَّٰتِي فِي حُجُورِكُم مِّن نِّسَآئِكُمُ ٱلَّٰتِي دَخَلۡتُم بِهِنَّ فَإِن لَّمۡ تَكُونُواْ دَخَلۡتُم بِهِنَّ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ وَحَلَٰٓئِلُ أَبۡنَآئِكُمُ ٱلَّذِينَ مِنۡ أَصۡلَٰبِكُمۡ وَأَن تَجۡمَعُواْ بَيۡنَ ٱلۡأُخۡتَيۡنِ إِلَّا مَا قَدۡ سَلَفَۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Kwaletsedwa kwa inu kukwatira amayi anu, ana anu, alongo anu, azakhali anu, amayi anu aang’ono kapena aakulu, ana achikazi am’bale wanu, ana achikazi a mlongo wanu, amayi anu amene adakuyamwitsani, alongo anu oberekedwa ndi amene adakuyamwitsanipo. Mayi a akazi anu, ana achikazi owapeza amene mukuwasunga woberekedwa ndi akazi anu omwe mwalowana nawo. Koma ngati simudalowane nawo, nkosaletsedwa kwa inu kukwatira ana awowo; ndi akazi a ana amuna omwe ngochokera kumisana yanu. Ndiponso nkoletsedwa kwa inu kukwatira mophatikiza mkazi ndi mchemwali wake obadwa naye, kupatula zomwe zidapita. Ndithudi Allah Ngokhululuka kwambiri Ngwachisoni zedi.
Arapça tefsirler:
۞ وَٱلۡمُحۡصَنَٰتُ مِنَ ٱلنِّسَآءِ إِلَّا مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡۖ كِتَٰبَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡۚ وَأُحِلَّ لَكُم مَّا وَرَآءَ ذَٰلِكُمۡ أَن تَبۡتَغُواْ بِأَمۡوَٰلِكُم مُّحۡصِنِينَ غَيۡرَ مُسَٰفِحِينَۚ فَمَا ٱسۡتَمۡتَعۡتُم بِهِۦ مِنۡهُنَّ فَـَٔاتُوهُنَّ أُجُورَهُنَّ فَرِيضَةٗۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ فِيمَا تَرَٰضَيۡتُم بِهِۦ مِنۢ بَعۡدِ ٱلۡفَرِيضَةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
۞ Ndiponso (nkoletsedwa kwa inu kukwatira) akazi okwatiwa kupatula chimene manja anu akumanja apeza (mdzakazi). Ili ndi lamulo la Allah lomwe lili pa inu. Ndipo kwalolezedwa kwa inu (kukwatira akazi) omwe sali m’gulu ili. Afunefuneni ndi chuma chanu m’njira ya ukwati, osati chiwerewere. Choncho, amene mwawakwatira mwa iwo nkusangalala nawo, apatseni chiwongo chawo chomwe chakakamizidwa. Palibe kuipa kwa inu (kupereka) chomwe mwagwirizana m’malo mwa chomwe chidatchulidwa. Ndithudi, Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya (pokhazikitsa malamulo Ake).
Arapça tefsirler:
وَمَن لَّمۡ يَسۡتَطِعۡ مِنكُمۡ طَوۡلًا أَن يَنكِحَ ٱلۡمُحۡصَنَٰتِ ٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ فَمِن مَّا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُكُم مِّن فَتَيَٰتِكُمُ ٱلۡمُؤۡمِنَٰتِۚ وَٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِإِيمَٰنِكُمۚ بَعۡضُكُم مِّنۢ بَعۡضٖۚ فَٱنكِحُوهُنَّ بِإِذۡنِ أَهۡلِهِنَّ وَءَاتُوهُنَّ أُجُورَهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِ مُحۡصَنَٰتٍ غَيۡرَ مُسَٰفِحَٰتٖ وَلَا مُتَّخِذَٰتِ أَخۡدَانٖۚ فَإِذَآ أُحۡصِنَّ فَإِنۡ أَتَيۡنَ بِفَٰحِشَةٖ فَعَلَيۡهِنَّ نِصۡفُ مَا عَلَى ٱلۡمُحۡصَنَٰتِ مِنَ ٱلۡعَذَابِۚ ذَٰلِكَ لِمَنۡ خَشِيَ ٱلۡعَنَتَ مِنكُمۡۚ وَأَن تَصۡبِرُواْ خَيۡرٞ لَّكُمۡۗ وَٱللَّهُ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo amene sangathe mwa inu kupeza chuma chokwatilira mkazi amene ali mfulu wokhulupirira, (akwatireni adzakazi) achisungwana okhulupirira, mwa omwe manja anu akumanja apeza, Allah akudziwa kwambiri chikhulupiliro chanu. Ndinu amodzi kuchokera kwa wina ndi mnzake (nonsenu ndinu ana a Adam). Akwatireni ndi chilolezo cha mabwana awo, ndipo apatseni chiwongo chawo mwachilamulo. (Akwatireni) omwe ali akazi odzisunga, osati achiwerewere kapena ochita zibwenzi. Ndipo akakwatiwa, kenako nkuchita chauve, chilango chawo nditheka lachilango cha mfulu. Kumeneko (kukwatira akapoloko) ndilamulo kwa yemwe mwa inu akuopa kuti angachite chiwerewere. Koma ngati mutapirira (posiya kukwatira akapolo) ndibwino kwa inu kutero. Ndipo Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.
Arapça tefsirler:
يُرِيدُ ٱللَّهُ لِيُبَيِّنَ لَكُمۡ وَيَهۡدِيَكُمۡ سُنَنَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ وَيَتُوبَ عَلَيۡكُمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
Allah akufuna kukufotokozerani ndi kukutsogolerani kunjira za omwe adalipo patsogolo panu; ndiponso akufuna kulandira kulapa kwanu. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
وَٱللَّهُ يُرِيدُ أَن يَتُوبَ عَلَيۡكُمۡ وَيُرِيدُ ٱلَّذِينَ يَتَّبِعُونَ ٱلشَّهَوَٰتِ أَن تَمِيلُواْ مَيۡلًا عَظِيمٗا
Ndiponso Allah akufuna kulandira kulapa kwanu. Koma amene akutsata zilakolako zawo akufuna mupotoke; kupotoka kwakukulu.
Arapça tefsirler:
يُرِيدُ ٱللَّهُ أَن يُخَفِّفَ عَنكُمۡۚ وَخُلِقَ ٱلۡإِنسَٰنُ ضَعِيفٗا
Allah akufuna kukupeputsirani, pakuti munthu adalengedwa wofooka (alibe mphamvu za thupi ngakhale zolimbana ndi zilakolako za moyo).
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ إِلَّآ أَن تَكُونَ تِجَٰرَةً عَن تَرَاضٖ مِّنكُمۡۚ وَلَا تَقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُمۡ رَحِيمٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musadye chuma chanu mwachinyengo koma m’njira yamalonda ndi moyanjana pakati panu. Ndipo musadziphe nokha (ngakhale kupha anzanu). Ndithudi, Allah ali Wachisoni pa inu.[118]
[118] Apa akuletsa kudyerana chuma m’njira yachinyengo. Koma kugulitsana malonda mwachimvano onse awiri nkomwe kukuloledwa. Ndipo Allah pomwe wanena kuti musadziphe, m’mawu amenewa mukutanthauza munthu kudzipha yekha, ndi kupha msilamu mnzake poti msilamu ndi msilamu mnzake ali ngati thupi limodzi. Ndipo ngakhale yemwe sali msilamu saloledwa kumupha. Mawu oti “kupha” akutanthauza kupha munthu nkuferatu nthawi yomweyo. Mawuwa akutanthauzanso kuchita chinthu chomwe chingamchititse munthu uja kuonongeka mwapang’onopang’ono mpaka mathero ake nkuferatu. Izi zili monga amene akumwa mowa wakachasu kapena wina uliwonse, akudzipha yekha. Kapenanso kuchita chinthu china chilichonse chomwe mathero ake chimamupha munthu. Ndipo nayenso amene akuthandizira zimenezi, ali m’gulu lakupha munthu.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ عُدۡوَٰنٗا وَظُلۡمٗا فَسَوۡفَ نُصۡلِيهِ نَارٗاۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرًا
Ndipo amene achite izi molumpha malire ndi mopanda chilungamo, iyeyo tidzamulowetsa kumoto. Ndipo zimenezo nzopepuka kwa Allah.
Arapça tefsirler:
إِن تَجۡتَنِبُواْ كَبَآئِرَ مَا تُنۡهَوۡنَ عَنۡهُ نُكَفِّرۡ عَنكُمۡ سَيِّـَٔاتِكُمۡ وَنُدۡخِلۡكُم مُّدۡخَلٗا كَرِيمٗا
Ngati mudzitalikitsa kumachimo akuluakulu omwe mukuletsedwa, ndiye kuti tikufafanizirani zolakwa zanu (zing’onozing’ono) ndipo tidzakulowetsani malo aulemu.[119]
[119] Apa akuti ngati tipewa machimo akuluakulu, Allah adzatikhululukira timachimo ting’onoting’ono. Munthu nkovuta kuupewa uchimo ung’onoung’ono. Uchimotu suli wofanana. Pali wina waukulu. Palinso wina wokulitsitsa. Ndipo pali waung’ono ndi wina wochepetsetsa.
Machimo akuluakulu ali ngati awa: (a) Kuphatikiza Allah ndi mafano. (b) Kupha munthu wosalakwa. (c) Kuba. (d) Kuchita malonda akatapira (riba). (e) Kumwa zoledzeretsa. (f) Kuchita chiwerewere ndi zina zotero.
Tsono uchimo waung’ono uli monga: Kunena mawu osafunika ndi kuchiyang’ana chinthu choletsedwa ndi zina zotero zomwe nzovuta munthu kuzipewa. Choncho, munthu akapewa machimo akuluakulu ndiye kuti adzamkhululukira machimo ang’onoang’ono ngati sakuwachita mochulukitsa.
Enanso mwa machimo akuluakulu ndikusiya kutsata malamulo a Allah, monga (a) Kusiya kupemphera Swala zisanu. (b) Kusiya kupereka Zakaat ndi zithandizo zina zofunika. (c) Kusiya kumanga m’mwezi wa Ramadan. (d) Kusiya kuchita Hajj. (e) Kusiya kuyang’anira makolo ndi zina zotero.
Arapça tefsirler:
وَلَا تَتَمَنَّوۡاْ مَا فَضَّلَ ٱللَّهُ بِهِۦ بَعۡضَكُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖۚ لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا ٱكۡتَسَبُواْۖ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا ٱكۡتَسَبۡنَۚ وَسۡـَٔلُواْ ٱللَّهَ مِن فَضۡلِهِۦٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٗا
Ndipo musazilakelake (mwadumbo) zomwe Allah wawadalitsa nazo ena mwa inu. Amuna ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Nawonso akazi ali ndi gawo (lokwanira) la zomwe apeza. Ndipo mpempheni Allah zabwino zake. Ndithudi, Allah Ngodziwa chilichonse.[120]
[120] Apa akuletsa anthu kuchitirana dumbo. Koma chofunika nkuti munthu alimbike kugwira ntchito kuti nayenso apeze chomwe mnzake wapeza. Osati kumchitira dumbo ndi kumuda, pakuti iye palibe chimene wakulanda. Adagwira ntchito molimbika ndipo Allah wampatsa. Iwenso limbikira kugwira ntchito Allah akupatsa. Wopemphedwa ndi kupatsa ndiyemweyo Allah wathu.
Arapça tefsirler:
وَلِكُلّٖ جَعَلۡنَا مَوَٰلِيَ مِمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَۚ وَٱلَّذِينَ عَقَدَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡ فَـَٔاتُوهُمۡ نَصِيبَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدًا
Ndipo anthu tawaikira alowa mmalo pa zomwe asiya makolo awiri ndi achibale. Ndipo amene mudagwirizana nawo chipangano, apatseni gawo lawo. Ndithudi, Allah Ndimboni pa chilichonse.[121]
[121] Nthawi ya umbuli, munthu ankati akatenga mwana wa munthu wina nkumulera ankamuyesa mwana wake weniweni pomulowera chokolo pa chilichonse ngati mwanayo atafa. Ngakhale makolo ake enieni ndi abale ake atakhalapo sadali kuwagawira chilichonse. Tsono Chisilamu chidathetsa mchitidwe umenewu ponena kuti munthu aliyense azimlowa chokolo ndi abale ake.
Arapça tefsirler:
ٱلرِّجَالُ قَوَّٰمُونَ عَلَى ٱلنِّسَآءِ بِمَا فَضَّلَ ٱللَّهُ بَعۡضَهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ وَبِمَآ أَنفَقُواْ مِنۡ أَمۡوَٰلِهِمۡۚ فَٱلصَّٰلِحَٰتُ قَٰنِتَٰتٌ حَٰفِظَٰتٞ لِّلۡغَيۡبِ بِمَا حَفِظَ ٱللَّهُۚ وَٱلَّٰتِي تَخَافُونَ نُشُوزَهُنَّ فَعِظُوهُنَّ وَٱهۡجُرُوهُنَّ فِي ٱلۡمَضَاجِعِ وَٱضۡرِبُوهُنَّۖ فَإِنۡ أَطَعۡنَكُمۡ فَلَا تَبۡغُواْ عَلَيۡهِنَّ سَبِيلًاۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيّٗا كَبِيرٗا
Amuna ndiayang’aniri pa akazi chifukwa choti Allah watukula ena pa ulemelero pamwamba pa ena, chifukwa cha chuma chawo chimene apereka. Choncho, akazi abwino ndi omwe ali omvera, odzisunga ngakhale amuna awo palibe pakuti Allah wawalamula kudzisunga. Ndipo akazi omwe mukuopa mnyozo wawo, achenjezeni; ndipo kenako achokereni pamphasa, (apo ayi), akwapuleni (kukwapula kosavulaza), koma ngati akukumverani, musawafunire njira yowavutitsira. Ndithu Allah ndi yemwe ali Wapamwamba, Wamkulu (kuposa inu nonse).[122]
[122] Apa akuti amuna ndi amene akhale ndi ulamuliro pa akazi awo, powatsogolera ku miyambo yabwino. Osati kuti mkazi adzitukumule kwa mwamuna wake poti iye ngophunzira zedi kapena wanzeru zochuluka kotero kuti mwamuna m’nyumba osamuyesa kanthu. Ngati atero ndiye kuti sakhala Asilamu owona. M’ndimeyi atchulamonso makhalidwe ofunika kuti akazi akhale nawo. Ndipo atchulamo malangizo olangira nawo mkazi ngati samvera. Choyamba amchenjeze ndi mawu. Ngati kuchenjezako sikunathandize, asagone naye limodzi pamphasa. Ndipo ngati akupitirizabe kuchita mnyozo akupatsidwa chilolezo mwamuna kuti amlange pommenya mwakumuopyeza, osati kumenya komgulula nako mano. Komabe mahadisi a Mtumiki (s.a.w) akunena kuti asanaganize zommenya ayeseyese kumkonza ponena naye mofewa ndi kumuonetsa kulakwa kwake. Ngati atalephera zonsezi, aitane anthu kuti adzawayanjanitse m’njira yabwino. Naonso anthuwo akhale ndi cholinga choyanjanitsa osati kupasula. Amunanso akuwachenjeza apa kuti iwo ndi amene ali ndi nyonga ndi udindo. Allah ndiye Wamkulu kuposa iwo amunawo. Mawu oti “Hafizatu Lilighaibi” maulama ena akuwatanthauzira kuti “Akhale osunga chinsinsi,” chimene chili pakati pa iwo ndi amuna awo ndi zonse zomwe zimachitika m’nyumba, pakuti nthawi zambiri akazi sakhalira kuulula za m’nyumba.
Arapça tefsirler:
وَإِنۡ خِفۡتُمۡ شِقَاقَ بَيۡنِهِمَا فَٱبۡعَثُواْ حَكَمٗا مِّنۡ أَهۡلِهِۦ وَحَكَمٗا مِّنۡ أَهۡلِهَآ إِن يُرِيدَآ إِصۡلَٰحٗا يُوَفِّقِ ٱللَّهُ بَيۡنَهُمَآۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا خَبِيرٗا
Ndipo (inu aweruzi) ngati muopa mkangano pakati pawo (pa mwamuna ndi mkazi wake), tumizani nkhoswe ya kuchimuna ndi nkhoswe ya kuchikazi. Ngati iwo atafuna kuyanjanitsa, Allah awapatsa mphamvu zoyanjanitsira pakati pawo (okanganawo). Allah Ngodziwa nkhani zobisika, ndiponso Ngodziwa nkhani zoonekera.
Arapça tefsirler:
۞ وَٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ وَلَا تُشۡرِكُواْ بِهِۦ شَيۡـٔٗاۖ وَبِٱلۡوَٰلِدَيۡنِ إِحۡسَٰنٗا وَبِذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱلۡجَارِ ذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡجَارِ ٱلۡجُنُبِ وَٱلصَّاحِبِ بِٱلۡجَنۢبِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِ وَمَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ مَن كَانَ مُخۡتَالٗا فَخُورًا
Ndipo mpembedzeni Allah, ndipo musamphatikize ndi chilichonse; ndipo achitireni zabwino makolo awiri, ndi achibale, ndi ana amasiye ndi masikini ndi mnansi woyandikana naye nyumba, ndi wapadera wogundizana naye nyumba, ndi mnzako wokhala naye limodzi, ndi wapaulendo yemwe alibe choyendera, ndi omwe manja anu akumanja apeza (adzakazi). Ndithudi, Allah sakonda wodzitukumula ndi wodzitama.[123]
[123] M’ndime iyi akuwalamula anthu kuti apembedze Allah yekha ndi kumpempha Iye Yekha. Asapembedzenso china chilichonse, chamoyo kapena chakufa. Ndikuti awachitire zabwino makolo ake ndi onse amene awatchula m’ndimeyi. Sibwino kuthandiza anthu akumbali pomwe anthu omwe uli nawo pafupi sunawathandizepo.
Arapça tefsirler:
ٱلَّذِينَ يَبۡخَلُونَ وَيَأۡمُرُونَ ٱلنَّاسَ بِٱلۡبُخۡلِ وَيَكۡتُمُونَ مَآ ءَاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦۗ وَأَعۡتَدۡنَا لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا
Omwe amachita umbombo ndi kulamula anthu kuchita umbombo ndi kubisa zabwino zomwe Allah wawapatsa. Komatu osakhulupirira tawakonzera chilango choyalutsa.[124]
[124] Kubisa zonse zomwe Allah wawapatsa kuli monga munthu kukhala ndi maphunziro koma osaphunzitsa anthu kotero kuti nkufa nawo popanda kuphunzitsapo aliyense. Kutero sibwino. Koma akafuna kukalowa m’Munda wa mtendere wa Allah nkofunika kuti achite zinthu zabwino ncholinga chokondweretsa Allah. Osati kuti anthu amuone ndi kumtama. Amene akuchita chinthu chabwino ncholinga choti anthu amtamande, sakalandira mphoto iliyonse pa tsiku lachimaliziro.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ رِئَآءَ ٱلنَّاسِ وَلَا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَلَا بِٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۗ وَمَن يَكُنِ ٱلشَّيۡطَٰنُ لَهُۥ قَرِينٗا فَسَآءَ قَرِينٗا
Ndi omwe akupereka chuma chawo modzionetsera kwa anthu ndipo sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Ndiponso yemwe satana angakhale bwenzi lake, ndithudi ali ndi bwenzi loipa.
Arapça tefsirler:
وَمَاذَا عَلَيۡهِمۡ لَوۡ ءَامَنُواْ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَأَنفَقُواْ مِمَّا رَزَقَهُمُ ٱللَّهُۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِهِمۡ عَلِيمًا
Kodi pakadakhala vuto lanji kwa iwo ngati akadakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro napereka zina mwa zomwe Allah wawapatsa? Ndipo Allah ali Wodziwa bwino za iwo.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَظۡلِمُ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖۖ وَإِن تَكُ حَسَنَةٗ يُضَٰعِفۡهَا وَيُؤۡتِ مِن لَّدُنۡهُ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Ndithudi, Allah sachitira (anthu) zosalungama ngakhale kanthu kolemera ngati kanyelere; ngati kanthuko kali kabwino amakachulukitsa ndi kupereka malipiro aakulu kuchokera kwa Iye.
Arapça tefsirler:
فَكَيۡفَ إِذَا جِئۡنَا مِن كُلِّ أُمَّةِۭ بِشَهِيدٖ وَجِئۡنَا بِكَ عَلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِ شَهِيدٗا
Nanga zidzakhala bwanji tikadzabweretsa mboni pa m’badwo uliwonse ndikukubweretsa iwe (Mneneri Muhammad{s.a.w}) kuti ukhale mboni pa m’badwo uwu.
Arapça tefsirler:
يَوۡمَئِذٖ يَوَدُّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَعَصَوُاْ ٱلرَّسُولَ لَوۡ تُسَوَّىٰ بِهِمُ ٱلۡأَرۡضُ وَلَا يَكۡتُمُونَ ٱللَّهَ حَدِيثٗا
Tsiku limenelo aja omwe sadakhulupirire namunyoza Mtumiki, adzakhumba kuti nthaka ikadafafanizidwa pa iwo (akwiliridwe, asaukitsidwe). Ndipo sadzatha kum’bisira Allah nkhani iliyonse (m’zomwe adachita m’moyo wa pa dziko).
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَقۡرَبُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَأَنتُمۡ سُكَٰرَىٰ حَتَّىٰ تَعۡلَمُواْ مَا تَقُولُونَ وَلَا جُنُبًا إِلَّا عَابِرِي سَبِيلٍ حَتَّىٰ تَغۡتَسِلُواْۚ وَإِن كُنتُم مَّرۡضَىٰٓ أَوۡ عَلَىٰ سَفَرٍ أَوۡ جَآءَ أَحَدٞ مِّنكُم مِّنَ ٱلۡغَآئِطِ أَوۡ لَٰمَسۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ فَلَمۡ تَجِدُواْ مَآءٗ فَتَيَمَّمُواْ صَعِيدٗا طَيِّبٗا فَٱمۡسَحُواْ بِوُجُوهِكُمۡ وَأَيۡدِيكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَفُوًّا غَفُورًا
E inu amene mwakhulupirira! Musayandikire Swala uku muli oledzera, mpaka mudziwe chimene mukunena; ngakhalenso pamene muli ndi janaba (musapemphere kufikira mutasamba) kupatula amene ali pa ulendo (achite Tayammam). Ndipo ngati muli odwala, kapena muli pa ulendo, kapena m’modzi wanu wadza kuchokera kuchimbudzi, kapena mwakhudza akazi (m’njira ya ukwati) ndipo simunapeze madzi (osamba) chitani Tayammam ndi dothi labwino; lipakeni kunkhope kwanu ndi m’mikono mwanu. Ndithudi, Allah Ngofafaniza machimo, Ngokhululuka kwambiri.
Arapça tefsirler:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ نَصِيبٗا مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ يَشۡتَرُونَ ٱلضَّلَٰلَةَ وَيُرِيدُونَ أَن تَضِلُّواْ ٱلسَّبِيلَ
Kodi sukuwaona omwe adapatsidwa gawo la (nzeru zozindikira) buku (la Allah, omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu), akudzisankhira kusokera ndiponso akufuna mutasokera kusiya njira (yabwino).[125]
[125] (Ndime 44-46) Apa akutchula kuipa kwina kwa Ayuda ndi Akhrisitu. Iwo adali kusintha mawu omwe adali m’mabuku a Taurat ndi Injil, makamaka mawu amene adali kusonyeza za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Kapena adali kuwatanthauzira m’njira zina zogwirizana ndi zolinga zawo. Pamene adali kudza kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) makamaka Ayuda, akawalalikira mawu achipembedzo, ankati: “Tamva, titsatira,” pomwe m’mitima mwawo akuti “Sititsatira zonse zomwe ukunena. Koma tikungokunyenga chabe.” Amati akadza nkumva momwe maswahaba amanenera ndi Mtumiki (s.a.w), Mtumiki akawalalikira, amati: “Ismaa ghayra musma’” monga mwa chizolowezi cha Arabu akauzidwa mawu ofunika. Tanthuzo lake nkuti, “Imva siumvanso choipa kuchokera kwa ife ngati Allah afuna.” Naonso Ayuda adali kumnenera Mtumiki mawu omwewa, koma m’mitima mwawo akulinga tanthauzo lina. M’mitima mwawo amalinga kuti, “Siumva zabwino kuchokera kwa ife ngati Allah afuna, koma zokusowetsa mtendere zokhazokha.” Ndipo amati akabweranso Ayudawo nkumva maswahaba akumuuza Mtumiki kuti; “Raa’ina”. Kutanthauza kuti, “Tiyang’ane ndi diso lachifundo,” iwonso amayankhula mawu omwewa, koma mokhotetsa pang’ono mpaka kusinthika tanthauzo lake. M’chiyankhulo cha chiyuda limatanthauza kuti “E iwe mbutuma!” Ndipo iwo m’kunena kwawo amalinga tanthauzo limeneli. Choncho Asilamu anawauza kuti azigwiritsira ntchito mawu oti “Undhurna.” Ndipo mawuwa tanthauzo lake ndilofanana. Koma mawu awa Ayuda sakadatha kuwakhotetsa.
Arapça tefsirler:
وَٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِأَعۡدَآئِكُمۡۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَلِيّٗا وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ نَصِيرٗا
Ndipo Allah akudziwa bwinobwino za adani anu. Ndipo Allah akukwanira kukhala Mtetezi. Allah akukwananso kukhala Mthandizi.
Arapça tefsirler:
مِّنَ ٱلَّذِينَ هَادُواْ يُحَرِّفُونَ ٱلۡكَلِمَ عَن مَّوَاضِعِهِۦ وَيَقُولُونَ سَمِعۡنَا وَعَصَيۡنَا وَٱسۡمَعۡ غَيۡرَ مُسۡمَعٖ وَرَٰعِنَا لَيَّۢا بِأَلۡسِنَتِهِمۡ وَطَعۡنٗا فِي ٱلدِّينِۚ وَلَوۡ أَنَّهُمۡ قَالُواْ سَمِعۡنَا وَأَطَعۡنَا وَٱسۡمَعۡ وَٱنظُرۡنَا لَكَانَ خَيۡرٗا لَّهُمۡ وَأَقۡوَمَ وَلَٰكِن لَّعَنَهُمُ ٱللَّهُ بِكُفۡرِهِمۡ فَلَا يُؤۡمِنُونَ إِلَّا قَلِيلٗا
Mwa Ayuda alipo omwe amasintha mawu kuwachotsa m’malo mwake. Ndipo amanena (chabe ndi milomo yawo): “Tamva;” (pomwe mitima yawo ikunena): “Tanyoza.” (Ndipo akunena kuuza Mtumiki): “Imva koma wosamveredwa (ndipo pakati pakuyankhula kwawo amanena mawu akuti) ‘Raaina’ (ncholinga chomnenera kuti iye ndimbutuma), mokhotetsa malilime awo (mu zoyankhula zawo kuti akhale ngati akumunenera zabwino pomwe akumtembelera) ndi cholinga chotukwana chipembedzo (cha Chisilamu). Akadakhala kuti iwo adanena: “Tamva ndipo tamvera; ndipo imva, utiyang’anire,” (mmalo mwa kunena kwawo kwakuti: ‘Raaina’), zikadakhala zabwino ndizolingana kwa iwo. Koma Allah adawatembelera chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Sakhulupirira koma pang’ono basi.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ ءَامِنُواْ بِمَا نَزَّلۡنَا مُصَدِّقٗا لِّمَا مَعَكُم مِّن قَبۡلِ أَن نَّطۡمِسَ وُجُوهٗا فَنَرُدَّهَا عَلَىٰٓ أَدۡبَارِهَآ أَوۡ نَلۡعَنَهُمۡ كَمَا لَعَنَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلسَّبۡتِۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ مَفۡعُولًا
E inu amene mwapatsidwa buku! Zikhulupirireni zomwe tavumbulutsa zikutsimikizira zomwe muli nazo tisanazisinthe nkhope zanu ndi kuzitembenuzira kumbuyo kwake, kapena tisanawatembelere monga momwe tidawatembelera omwe sadalemekeze kupatulika kwa tsiku la Sabata. Ndipo lamulo la Allah ndilochitikadi.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَغۡفِرُ أَن يُشۡرَكَ بِهِۦ وَيَغۡفِرُ مَا دُونَ ذَٰلِكَ لِمَن يَشَآءُۚ وَمَن يُشۡرِكۡ بِٱللَّهِ فَقَدِ ٱفۡتَرَىٰٓ إِثۡمًا عَظِيمًا
Ndithudi Allah sangakukhululuke kuphatikizidwa (ndi chinachake), koma amakhululuka (machimo ena) osati amenewa kwa amene wamfuna. Ndipo amene angamphatikize Allah, ndithudi, wadzipekera uchimo waukulu.
Arapça tefsirler:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ يُزَكُّونَ أَنفُسَهُمۚ بَلِ ٱللَّهُ يُزَكِّي مَن يَشَآءُ وَلَا يُظۡلَمُونَ فَتِيلًا
Kodi sukuwaona omwe akudziyeretsa okha? Koma Allah amamuyeretsa amene wamufuna (pomulimbikitsa kuchita zabwino). Ndipo sadzaponderezedwa ngakhale ndi kachinthu kochepa konga kaulusi kokhala mkati mwakhokho la tende.[126]
[126] Ayuda adali kunyada chifukwa choti iwo adali nawo aneneri, ndiponso makolo awo omwe adali olungama. Ankati: “Poti makolo athu adali olungama palibe chochititsa mantha pa ife. Uchimo uliwonse umene ife tingachite Allah adzatikhululukira ngakhale uchimowo utakhala waukulu chotani.” Iwo ankadzitchanso kuti adali okondedwa a Allah. Ndipo iwowo ngomwe akuwatchula m’ndime iyi kuti “Kodi saona amene akudziyeretsa okha ndi mawu okha ochokera m’milomo popanda kuchita zimene adawalamula ndi kusiya zomwe adawaletsa?” Mwa Asilamu aliponso ena omwe ali ndi maganizo onga amenewa. Amangonyadira zochita zamakolo awo popanda kutsanzira chikhalidwe chamakolo awowo.
Arapça tefsirler:
ٱنظُرۡ كَيۡفَ يَفۡتَرُونَ عَلَى ٱللَّهِ ٱلۡكَذِبَۖ وَكَفَىٰ بِهِۦٓ إِثۡمٗا مُّبِينًا
Taona, momwe akumpekera Allah bodza! Ndipo izi zikukwana kukhala tchimo loonekera!
Arapça tefsirler:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ نَصِيبٗا مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡجِبۡتِ وَٱلطَّٰغُوتِ وَيَقُولُونَ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ هَٰٓؤُلَآءِ أَهۡدَىٰ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ سَبِيلًا
Kodi sukuwaona omwe apatsidwa gawo la nzeru zozindikira buku (la Allah)? Amakhulupirira mafano ndi asatana, ndipo akumati kwa amene sadakhulupirire: “Awa ali panjira yoongoka kwabasi kuposa okhulupirira (Asilamu).”[127]
[127] Mawu oti “Jibti ndi Twaghut’’ amanena za chinthu chomwe anthu akuchipembedza chamoyo kapena chakufa chomwe sichili Mulungu weniweni monga momwe lilili dzina loti Shaytan. Iloli limatchulidwa kwa aliyense amene akusokeretsa anthu ku njira ya Allah. Chifukwa cha kuipidwa ndi Asilamu, Ayuda adapita ku Makka kukapalana ubwenzi ndi Aquraish ndi Arabu ena opembedza mafano kuti athandizane nawo kumthira nkhondo Mtumiki Muhammad (s.a.w) pamodzi ndi omtsatira ake kuti achithetseretu chipembedzo cha Chisilamu. Choncho akuluakulu a Chiyuda atafika ku Makka adagwadira mafano ncholinga chofuna kukondweretsa Aquraish pomwe Ayudawo adali eni mabuku omwe salola kupembedza mafano. Adawalimbikitsanso Aquraish aja powauza kuti: “Zochita zanu pa chipembedzo chanu nzabwino kuposa zochita za Muhammad pachipembedzo chake chimene wadza nacho.” Iwo amanena izi akudziwa kuti akunama. Cholinga chawo kudali kupeza chithandizo kwa iwo kuti athetse Chisilamu chifukwa chakudzadzidwa ndi njiru m’mitima mwawo ponena kuti: “Nchotani kuti Muhammad (s.a.w) alandire chisomo chauneneri?” Iwo ankachita izi ngati kuti ufumu wa Allah udali m’manja mwawo kuti iwo ndi amene amagawa zachifundo cha Allah, chonsecho, Allah amapereka kwa yemwe wamfuna. Iye amachita chimene wafuna. Safunsidwa ndi aliyense pa chimene wachita. Koma iwo amafunsidwa.
Arapça tefsirler:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ لَعَنَهُمُ ٱللَّهُۖ وَمَن يَلۡعَنِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ نَصِيرًا
Iwo ndi omwe Allah wawatembelera. Ndipo amene Allah wamtembelera, simungathe kumpezera wompulumutsa.
Arapça tefsirler:
أَمۡ لَهُمۡ نَصِيبٞ مِّنَ ٱلۡمُلۡكِ فَإِذٗا لَّا يُؤۡتُونَ ٱلنَّاسَ نَقِيرًا
Kodi ali ndi gawo la ufumu (wa Allah? Nchifukwa ninji akunyasidwa munthu wina akaninkhidwa utumiki)? Zikadatero ndiye kuti sakadawapatsa anthu ngakhale kochepa kwambiri monga khokho la tende.[128]
[128] Ndime 53-54 zikusonyeza kuti zonse zimene Ayuda ankawachitira Asilamu nchifukwa chadumbo basi. Ankawawidwa nawo mitima chifukwa choti Asilamu apeza chisomo cha Allah. Palibe chinthu chimene chimaletsa anthu kutsata choonadi kuposa dumbo. Ngati utamchitira dumbo munthu sungalole kutsata langizo lake lililonse ngakhale litakhala lopindulitsa pano pa dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro Dumbo ndi lomwe likuletsa anthu ambiri kutsata choonadi. Choncho tiyeni tipewe khalidwe limeneli kuti titsatire choonadi paliponse pamene chachokera. Ndikutinso tipeze mtendere m’mitima mwathu. Dziwani kuti dumbo nlomwe lidamchititsa Iblis kukhala wotembeleredwa.
Arapça tefsirler:
أَمۡ يَحۡسُدُونَ ٱلنَّاسَ عَلَىٰ مَآ ءَاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦۖ فَقَدۡ ءَاتَيۡنَآ ءَالَ إِبۡرَٰهِيمَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَءَاتَيۡنَٰهُم مُّلۡكًا عَظِيمٗا
Kodi akuchitira anthu dumbo pa zomwe Allah wawapatsa ndi ufulu wake? Choncho tidalipatsa banja la Ibrahim buku ndi nzeru. Ndipo tidawapatsa ufumu waukulu.
Arapça tefsirler:
فَمِنۡهُم مَّنۡ ءَامَنَ بِهِۦ وَمِنۡهُم مَّن صَدَّ عَنۡهُۚ وَكَفَىٰ بِجَهَنَّمَ سَعِيرًا
Choncho alipo ena mwa iwo amene anazikhulupirira izi, ndiponso alipo ena mwa iwo omwe adziika nazo kutali. Ndipo Jahannam ikukwanira kukhala Moto waukali wowatentha.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِـَٔايَٰتِنَا سَوۡفَ نُصۡلِيهِمۡ نَارٗا كُلَّمَا نَضِجَتۡ جُلُودُهُم بَدَّلۡنَٰهُمۡ جُلُودًا غَيۡرَهَا لِيَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَزِيزًا حَكِيمٗا
Ndithu amene sadakhulupirire zizindikiro Zathu, tidzawalowetsa ku Moto. Nthawi iliyonse yomwe makungu awo adzikapselera tidzidzawasinthira makungu ena kuti adzapitirize kulawa chilango. Ndithudi, Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.[129]
[129] (Ndime 56-57) Apa akutchula za malipiro a anthu ochita zabwino ndi malipiro a anthu ochita zoipa umu ndi momwe ulili ulaliki wa Qur’an. Qur’an ikafotokoza za anthu ochita zoipa imatsatiza pompo kufotokoza zotsatira za anthu ochita zabwino. Pamenepa akunena kuti aliyense adzalandira malipiro a zochita zake, abwino kapena oipa. Sakawomboledwa chifukwa cha ubwino wa munthu wina. Zochita zake ndizo zikamuombola kapena kukamponya kuchionongeko.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ سَنُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ لَّهُمۡ فِيهَآ أَزۡوَٰجٞ مُّطَهَّرَةٞۖ وَنُدۡخِلُهُمۡ ظِلّٗا ظَلِيلًا
Ndipo amene akhulupirira ndi kuchita zabwino, Tidzawalowetsa m’minda momwe mitsinje ikuyenda pansi (ndi patsogolo) pake. Adzakhala mmenemo muyaya. Ndipo iwo adzapeza mmenemo akazi oyeretsedwa (ku uve wamtundu uliwonse) ndi kuwalowetsa ku mithunzi yabwino kwambiri.
Arapça tefsirler:
۞ إِنَّ ٱللَّهَ يَأۡمُرُكُمۡ أَن تُؤَدُّواْ ٱلۡأَمَٰنَٰتِ إِلَىٰٓ أَهۡلِهَا وَإِذَا حَكَمۡتُم بَيۡنَ ٱلنَّاسِ أَن تَحۡكُمُواْ بِٱلۡعَدۡلِۚ إِنَّ ٱللَّهَ نِعِمَّا يَعِظُكُم بِهِۦٓۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ سَمِيعَۢا بَصِيرٗا
Ndithudi, Allah akukulamulani kubweza kwa eni zomwe mwakhulupirika nazo. Ndipo pamene mukuweruza pakati pa anthu, weruzani mwachilungamo. Ndithu malangizo amene Allah akukulangizani, ngabwino kwambiri. Ndithudi, Allah Ngwakumva, Ngoona.[130]
[130] Pali anthu ena amene amati anzawo akawasungitsa zinthu kuti akhulupirike pa zimenezo, mwini zinthu uja akafa kapena kuti panalibe umboni wokwanira, amazitenga zinthuzo poganizira kuti palibe chomwe chingawavute popeza mwini zinthuzo adamwalira ndipo umboni wokwanira palibe. Chikhalidwe chotere si cha Chisilamu, Chisilamu sichifuna machitidwe otere.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَ وَأُوْلِي ٱلۡأَمۡرِ مِنكُمۡۖ فَإِن تَنَٰزَعۡتُمۡ فِي شَيۡءٖ فَرُدُّوهُ إِلَى ٱللَّهِ وَٱلرَّسُولِ إِن كُنتُمۡ تُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ ذَٰلِكَ خَيۡرٞ وَأَحۡسَنُ تَأۡوِيلًا
E inu amene mwakhulupirira! Mumvereni Allah ndiponso mumvereni Mtumiki, ndi omwe ali ndi udindo pa inu. Ngati Mutatsutsana pa chinthu chilichonse, chibwezeni kwa Allah ndi Mtumiki Wake, ngatidi mukukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, kutero ndibwino; ndipo zotere zili ndi zotsatira zabwino.[131]
[131] Aliyense amene amdzoza utsogoleri nkofunika kuti anthu amumvere ngati iye akulamula zabwino. Pagulu la anthu ngati sipakhala mtsogoleri womumvera, ndiye kuti pamapezeka zisokonezo ndi ziwawa kotero kuti zinthu zawo siziyenda bwino. Chisilamu sichiloleza machitidwe achipolowe ndi ziwawa. Chisilamu chimakonda bata ndi mtendere ndi kuti pasapezeke anthu ena owachenjelera anzawo. Komatu atsogoleriwo awamvere akalamula mwa chilungamo popanda kulakwira Allah. Koma ngati akulakwira Allah asawamvere. Pamenepo atsate chomwe Allah wawalamula ndi Mtumiki Wake.
Arapça tefsirler:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ يَزۡعُمُونَ أَنَّهُمۡ ءَامَنُواْ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ وَمَآ أُنزِلَ مِن قَبۡلِكَ يُرِيدُونَ أَن يَتَحَاكَمُوٓاْ إِلَى ٱلطَّٰغُوتِ وَقَدۡ أُمِرُوٓاْ أَن يَكۡفُرُواْ بِهِۦۖ وَيُرِيدُ ٱلشَّيۡطَٰنُ أَن يُضِلَّهُمۡ ضَلَٰلَۢا بَعِيدٗا
Kodi sukuwaona omwe akungonena chabe kuti akhulupirira zomwe zavumbulutsidwa kwa iwe ndi zomwe zidavumbulutsidwa patsogolo pako, pomwe iwo akufuna kuti akaweruzidwe ndi maweruzo osagwirizana ndi Shariya, pomwenso alamulidwa kukana njira zotere? Koma satana akufuna kuwasokeretsa, kusokera kwakutali.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ تَعَالَوۡاْ إِلَىٰ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ وَإِلَى ٱلرَّسُولِ رَأَيۡتَ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ يَصُدُّونَ عَنكَ صُدُودٗا
Ndipo akauzidwa: “Idzani ku zomwe Allah wavumbulutsa, ndiponso (idzani) kwa Mtumiki.” Uwaona achinyengo akudziika kutali kwabasi ndi iwe.
Arapça tefsirler:
فَكَيۡفَ إِذَآ أَصَٰبَتۡهُم مُّصِيبَةُۢ بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيهِمۡ ثُمَّ جَآءُوكَ يَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ إِنۡ أَرَدۡنَآ إِلَّآ إِحۡسَٰنٗا وَتَوۡفِيقًا
Kodi zingakhale bwanji litawabwerera vuto chifukwa cha zomwe manja awo adatsogoza? Kenako nkukudzera (iwe Mtumiki) uku akulumbira: “Tikulumbira Allah; sitinafune china chilichonse koma zabwino zokha ndi chimvano.”
Arapça tefsirler:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ يَعۡلَمُ ٱللَّهُ مَا فِي قُلُوبِهِمۡ فَأَعۡرِضۡ عَنۡهُمۡ وَعِظۡهُمۡ وَقُل لَّهُمۡ فِيٓ أَنفُسِهِمۡ قَوۡلَۢا بَلِيغٗا
Iwo ndi omwe Allah akudziwa zomwe zili m’mitima mwawo. Choncho dzipatule kwa iwo, ndipo alangize ndi kuwauza mawu ogwira mtima.
Arapça tefsirler:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا مِن رَّسُولٍ إِلَّا لِيُطَاعَ بِإِذۡنِ ٱللَّهِۚ وَلَوۡ أَنَّهُمۡ إِذ ظَّلَمُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ جَآءُوكَ فَٱسۡتَغۡفَرُواْ ٱللَّهَ وَٱسۡتَغۡفَرَ لَهُمُ ٱلرَّسُولُ لَوَجَدُواْ ٱللَّهَ تَوَّابٗا رَّحِيمٗا
Ndipo sitidamtumize mtumiki aliyense koma kuti azimveredwa mwa lamulo la Allah. Ngati akadakudzera pamene adadzichitira okha zoipa, (chifukwa chokafuna chiweruzo cha satana) napempha chikhululuko kwa Allah (naye) Mtumiki nkuwapempheranso chikhululuko, ndithudi, akadampeza Allah ali Wolandira kulapa kwawo ali Wachisoni chosatha.
Arapça tefsirler:
فَلَا وَرَبِّكَ لَا يُؤۡمِنُونَ حَتَّىٰ يُحَكِّمُوكَ فِيمَا شَجَرَ بَيۡنَهُمۡ ثُمَّ لَا يَجِدُواْ فِيٓ أَنفُسِهِمۡ حَرَجٗا مِّمَّا قَضَيۡتَ وَيُسَلِّمُواْ تَسۡلِيمٗا
Ndikulumbira (m’choonadi cha) Mbuye wako, iwo sangakhale okhulupirira moona pokhapokha akuyese muweruzi wawo pa zomwe akukangana pakati pawo. Kenako asaone vuto m’mitima yawo pa zomwe waweruza, ndipo adzipereke kwathunthu (pogonjera chiweruzo chako).[132]
[132] Ngati anthu atakangana pachinthu ena nati chimenechi nchofunika pomwe ena akuti nchosafunika, onsewo abwere nkuyang’ana kuti mawu a Allah ndi mawu a Mtumiki akunena chiyani pachinthu choterecho. Tsono akapeza malangizo a Allah ndi Mtumiki pachimenecho awatsatire. Aliyense wa iwo asakhumudwe poona kuti zomwe amalimbikira sindizo zomwe Mtumiki (s.a.w) adaphunzitsa. Koma agonjere kwathunthu kuzophunzitsa za Mtumikizo. Chilichonse chimene Mtumiki walangiza asawiringule nacho. Koma angotsatira basi.
Arapça tefsirler:
وَلَوۡ أَنَّا كَتَبۡنَا عَلَيۡهِمۡ أَنِ ٱقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡ أَوِ ٱخۡرُجُواْ مِن دِيَٰرِكُم مَّا فَعَلُوهُ إِلَّا قَلِيلٞ مِّنۡهُمۡۖ وَلَوۡ أَنَّهُمۡ فَعَلُواْ مَا يُوعَظُونَ بِهِۦ لَكَانَ خَيۡرٗا لَّهُمۡ وَأَشَدَّ تَثۡبِيتٗا
Ndipo ngati tikadawalamula kuti: “Dzipheni nokha,” kapena: “Tulukani m’nyumba zanu; (mupite kunkhondo kapena musamuke),” sakadachita zimenezo kupatula ochepa mwa iwo. Koma akadachita zomwe auzidwa, zikadakhala zabwino kwa iwo. Ndipo zikadawalimbikitsa kwambiri (Chisilamu chawo).
Arapça tefsirler:
وَإِذٗا لَّأٓتَيۡنَٰهُم مِّن لَّدُنَّآ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Ndipo zikadatero, tikadawapatsa malipiro aakulu ochokera kwa Ife.
Arapça tefsirler:
وَلَهَدَيۡنَٰهُمۡ صِرَٰطٗا مُّسۡتَقِيمٗا
Ndiponso tikadawatsogolera ku njira yoongoka (yokawafikitsa ku Munda wamtendere).
Arapça tefsirler:
وَمَن يُطِعِ ٱللَّهَ وَٱلرَّسُولَ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَعَ ٱلَّذِينَ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلنَّبِيِّـۧنَ وَٱلصِّدِّيقِينَ وَٱلشُّهَدَآءِ وَٱلصَّٰلِحِينَۚ وَحَسُنَ أُوْلَٰٓئِكَ رَفِيقٗا
Ndipo amene angamvere Allah ndi Mtumiki wake, iwowo ndi omwe adzakhale pamodzi ndi omwe Allah adawadalitsa, kuyambira aneneri, olungama, mashahidi (asilamu ofela ku nkhondo) ndi anthu abwino. Taonani ubwino wokhala nawo pamodzi iwowo!
Arapça tefsirler:
ذَٰلِكَ ٱلۡفَضۡلُ مِنَ ٱللَّهِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ عَلِيمٗا
Umenewo ndiubwino wochokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa mokwanira.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ خُذُواْ حِذۡرَكُمۡ فَٱنفِرُواْ ثُبَاتٍ أَوِ ٱنفِرُواْ جَمِيعٗا
E inu amene mwakhulupirira! Khalani ochenjera (ndi adani anu; musanyengedwe nawo). Pitani (kunkhondo) gulu limodzilimodzi, kapena pitaniko nonsenu pamodzi (monga momwe Mtumiki angakulangizireni).
Arapça tefsirler:
وَإِنَّ مِنكُمۡ لَمَن لَّيُبَطِّئَنَّ فَإِنۡ أَصَٰبَتۡكُم مُّصِيبَةٞ قَالَ قَدۡ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيَّ إِذۡ لَمۡ أَكُن مَّعَهُمۡ شَهِيدٗا
Ndipo ndithu alipo ena mwa inu otsalira m’mbuyo sapita ku nkhondo, (ndiponso amaletsa anzawo). Ngati vuto litakupezani, (yense wa iwo) amanena: “Allah wandichitira chisomo posakhala m’gulu lawo kumeneko.”
Arapça tefsirler:
وَلَئِنۡ أَصَٰبَكُمۡ فَضۡلٞ مِّنَ ٱللَّهِ لَيَقُولَنَّ كَأَن لَّمۡ تَكُنۢ بَيۡنَكُمۡ وَبَيۡنَهُۥ مَوَدَّةٞ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ مَعَهُمۡ فَأَفُوزَ فَوۡزًا عَظِيمٗا
Koma ngati utakupezani ubwino wochokera kwa Allah (monga kupeza chuma chambiri chosiidwa ndi adani, kapena kupambana kumene) amanena ngati kuti padalibe chikondi pakati panu ndi pakati pake: “Kalanga ine! Ndikadakhala nawo pamodzi pa nkhondo imeneyi, (ndiye kuti) ndikadapambana; kupambana kwakukulu.”
Arapça tefsirler:
۞ فَلۡيُقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ٱلَّذِينَ يَشۡرُونَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا بِٱلۡأٓخِرَةِۚ وَمَن يُقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَيُقۡتَلۡ أَوۡ يَغۡلِبۡ فَسَوۡفَ نُؤۡتِيهِ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Choncho, amenye nkhondo pa njira ya Allah omwe akugulitsa moyo (wawo) wadziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo amene angamenye nkhondo pa njira ya Allah, kenako ndikuphedwa kapena kupambana tidzampatsa malipiro aakulu.
Arapça tefsirler:
وَمَا لَكُمۡ لَا تُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلرِّجَالِ وَٱلنِّسَآءِ وَٱلۡوِلۡدَٰنِ ٱلَّذِينَ يَقُولُونَ رَبَّنَآ أَخۡرِجۡنَا مِنۡ هَٰذِهِ ٱلۡقَرۡيَةِ ٱلظَّالِمِ أَهۡلُهَا وَٱجۡعَل لَّنَا مِن لَّدُنكَ وَلِيّٗا وَٱجۡعَل لَّنَا مِن لَّدُنكَ نَصِيرًا
Mwatani inu osamenyana pa njira ya Allah, ndi (kuwapulumutsa) omwe ali ofooka, aamuna ndi aakazi ndi ana, omwe akunena: “Mbuye wathu! Titulutseni m’mudzi uwu omwe anthu ake ndiopondereza; ndipo tipatseni mtetezi wochokera kwa Inu; ndiponso tipatseni mthandizi wochokera kwa Inu.”[133]
[133] Pamene Mtumiki (s.a.w) adasamuka ku Makka kukakhala ku Madina, Asilamu ena aamuna ndi aakazi adatsalira ku Makka chifukwa chakuti abale awo adawaletsa. Ndipo chifukwa chakufooka kwawo sadathe kuthawa mozemba namangokhala konko ku Makka akuwachitira zoipa zambiri ndi kumawanyoza. Choncho Asilamu adawauza kuti ngati kuzakhale kololezedwa kuchita nawo nkhondo Aquraish a m’Makka adzamenyane nawo Aquraishwo molimba kufikira adzawapulumutse. Asilamu adakwaniritsa lonjezolo. Adamenya nkhondo mpaka kugonjetsa mzinda wa Makka ndi kuwapulumutsa anzawo amene adali kupempha Allah kwa nthawi yaitali kuti awapulumutse ku anthu oipa.
Arapça tefsirler:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۖ وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱلطَّٰغُوتِ فَقَٰتِلُوٓاْ أَوۡلِيَآءَ ٱلشَّيۡطَٰنِۖ إِنَّ كَيۡدَ ٱلشَّيۡطَٰنِ كَانَ ضَعِيفًا
Amene akhulupirira, akumenya nkhondo pa njira ya Allah. Koma amene sadakhulupirire, akumenya nkhondo panjira ya satana. Choncho menyanani ndi abwenzi a satana. Ndithudi, ndale za satana nzofooka.
Arapça tefsirler:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ قِيلَ لَهُمۡ كُفُّوٓاْ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَ فَلَمَّا كُتِبَ عَلَيۡهِمُ ٱلۡقِتَالُ إِذَا فَرِيقٞ مِّنۡهُمۡ يَخۡشَوۡنَ ٱلنَّاسَ كَخَشۡيَةِ ٱللَّهِ أَوۡ أَشَدَّ خَشۡيَةٗۚ وَقَالُواْ رَبَّنَا لِمَ كَتَبۡتَ عَلَيۡنَا ٱلۡقِتَالَ لَوۡلَآ أَخَّرۡتَنَآ إِلَىٰٓ أَجَلٖ قَرِيبٖۗ قُلۡ مَتَٰعُ ٱلدُّنۡيَا قَلِيلٞ وَٱلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لِّمَنِ ٱتَّقَىٰ وَلَا تُظۡلَمُونَ فَتِيلًا
Kodi sukuwaona omwe adauzidwa kuti: “Aletseni manja anu (kumenyana ndi osakhulupirira mpaka lidze lamulo lakumenyana)? Koma tsono pempherani Swala ndikupereka chopereka basi. Koma pamene adalamulidwa kumenyana, pompo gulu lina la iwo lidaopa anthu (osakhulupirira) ngati likuopa Allah kapena kuposerapo. Ndipo adati: “Mbuye Wathu! chifukwa ninji mwatilamula kumenyana? Ha! Mukadatichedwetsa kufikira nyengo yochepa, (zikadakhala bwino).” Nena: “Chisangalalo cha m’dziko n’chochepa. Koma tsiku lachimaliziro ndilabwino kwambiri kwa amene akuopa (Allah). Ndipo simudzaponderezedwa ngakhale pa chinthu chaching’ono monga ulusi wakhokho la tende!”
Arapça tefsirler:
أَيۡنَمَا تَكُونُواْ يُدۡرِككُّمُ ٱلۡمَوۡتُ وَلَوۡ كُنتُمۡ فِي بُرُوجٖ مُّشَيَّدَةٖۗ وَإِن تُصِبۡهُمۡ حَسَنَةٞ يَقُولُواْ هَٰذِهِۦ مِنۡ عِندِ ٱللَّهِۖ وَإِن تُصِبۡهُمۡ سَيِّئَةٞ يَقُولُواْ هَٰذِهِۦ مِنۡ عِندِكَۚ قُلۡ كُلّٞ مِّنۡ عِندِ ٱللَّهِۖ فَمَالِ هَٰٓؤُلَآءِ ٱلۡقَوۡمِ لَا يَكَادُونَ يَفۡقَهُونَ حَدِيثٗا
Paliponse pamene mungakhale imfa ikupezani ngakhale mutakhala m’malinga olimba, ndipo ngati ubwino utawafika (opembedza mafano ndi achiphamaso) amati: “Ubwinowu, ukuchokera kwa Allah.” Koma choipa chikawafikira, amati: “Ichi chachitika chifukwa cha iwe (Muhammad).” Nena: “Zonse zachokera kwa Allah.” Kodi ngotani anthu awa, sangathe kuzindikira nkhani?
Arapça tefsirler:
مَّآ أَصَابَكَ مِنۡ حَسَنَةٖ فَمِنَ ٱللَّهِۖ وَمَآ أَصَابَكَ مِن سَيِّئَةٖ فَمِن نَّفۡسِكَۚ وَأَرۡسَلۡنَٰكَ لِلنَّاسِ رَسُولٗاۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ شَهِيدٗا
Chabwino chimene chakufikira (iwe munthu) ndiye kuti chachokera kwa Allah. Koma choipa chimene chakufikira ndiye kuti chachokera kwa iwe mwini (chifukwa cha zochita zako zoipa). Ndipo takutumiza (iwe Muhammad) kwa anthu kukhala Mtumiki. Ndipo Allah ndimboni yokwana.
Arapça tefsirler:
مَّن يُطِعِ ٱلرَّسُولَ فَقَدۡ أَطَاعَ ٱللَّهَۖ وَمَن تَوَلَّىٰ فَمَآ أَرۡسَلۡنَٰكَ عَلَيۡهِمۡ حَفِيظٗا
Yemwe angamvere Mtumiki ndiye kuti wamvera Allah, (chifukwa chakuti zonse zomwe iye akulamula nzotumidwa ndi Allah). Ndipo amene atembenukire kutali (kunyoza iwe, ndiye kuti zoipa zili pa iye mwini). Sitidakutumize iweyo kukhala muyang’anili pa iwo.
Arapça tefsirler:
وَيَقُولُونَ طَاعَةٞ فَإِذَا بَرَزُواْ مِنۡ عِندِكَ بَيَّتَ طَآئِفَةٞ مِّنۡهُمۡ غَيۡرَ ٱلَّذِي تَقُولُۖ وَٱللَّهُ يَكۡتُبُ مَا يُبَيِّتُونَۖ فَأَعۡرِضۡ عَنۡهُمۡ وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱللَّهِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلًا
Amati: “Tikumvera.” Koma akachoka kwa iwe, gulu lina la iwo limapangana usiku zosagwirizana ndi zomwe ukunena (pamaso pawo). Koma Allah akulemba zonse zomwe akupangana. Choncho apatukire ndipo yadzamira kwa Allah. Ndipo Allah wakwanira kukhala Mtetezi.
Arapça tefsirler:
أَفَلَا يَتَدَبَّرُونَ ٱلۡقُرۡءَانَۚ وَلَوۡ كَانَ مِنۡ عِندِ غَيۡرِ ٱللَّهِ لَوَجَدُواْ فِيهِ ٱخۡتِلَٰفٗا كَثِيرٗا
Kodi bwanji sakuilingalira Qur’an? Ndipo ikadakhala kuti siikuchokera kwa Allah, ndithudi, mmenemo akadapeza kusiyana kwambiri.[134]
[134] M’ndime iyi akuti Qur’an iyi mawu ake ngolingana. Siotsutsana ayi. Ndipo palibe amene angabweretse mtsutso wakuti mawu ena omwe ali m’bukuli ngabodza pa chifukwa chakutichakuti. Palibe buku lomwe munthu adalemba lomwe lidabweretsa mtsutso weniweni wakuti Qur’an simawu a Allah pachifukwa chakutichakuti. Ndipo silidzapezeka buku lotero mpaka dziko lapansi lidzatha. Koma mwina anthu akhoza kumayankhula chabe popanda kubwera ndi mtsutso weniweni wokhala ndi umboni wooneka. Kuona kwa Qur’an kwatsimikizika pa zinthu izi:- Qur’an idafotokoza nkhani zakale zomwe zidachitika Mtumiki Muhammad (s.a.w) asanabadwe pomwe iye sankadziwa kulemba ndi kuwerenga mabuku. Quran idafotokozanso zamtsogolo. Ndipo zina mwa izo zaonekera kale poyera: Qur’an idati: (1) “Chinthu chilichonse pali chachimuna ndi chachikazi”. Yang’anani ndime ya 36 ya Sûrat Yasin. (2) Kuti dziko lapansili lidalumikizana ndi kumwamba monga ikufotokozera Sûrat Anbiyaa ndime ya 30. (3) Kuti moyo umadalira madzi, monga momwe ndime ya 30 ya m’Sûrat Anbiyaa ikulongosolera. (4) Kuti anthu amene ali kutali kwambiri adzatha kumva zimene anthu ena akutali akunena. Monga momwe yafotokozera ndime ya 44 ya m’Sûrat Aaraf. (5) Ndi kuti anthu adzakwera kumwamba monga momwe ikulongosolera ndime ya 13 ya m’Sûrat Jathiya. Mu Qur’an muli zambiri zimene adafotokoza kuti zidzachitika mtsogolo. Ndipo zambiri mwa izo zachitikadi, anthu aziona. Ndipo zonsezi zikutsimikizira kuti Qur’an ndi mawu a Allah.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا جَآءَهُمۡ أَمۡرٞ مِّنَ ٱلۡأَمۡنِ أَوِ ٱلۡخَوۡفِ أَذَاعُواْ بِهِۦۖ وَلَوۡ رَدُّوهُ إِلَى ٱلرَّسُولِ وَإِلَىٰٓ أُوْلِي ٱلۡأَمۡرِ مِنۡهُمۡ لَعَلِمَهُ ٱلَّذِينَ يَسۡتَنۢبِطُونَهُۥ مِنۡهُمۡۗ وَلَوۡلَا فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ وَرَحۡمَتُهُۥ لَٱتَّبَعۡتُمُ ٱلشَّيۡطَٰنَ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndipo chikawadzera chinthu chilichonse chokhuza chitetezo kapena mantha, amachifalitsa. Koma akadachibwezera kwa Mtumiki ndi kwa omwe ali ndi udindo pa iwo, akadachidziwa omwe amafufuzafufuza zinthu mwa iwo (kuti kodi nzoyenera kuzifalitsa kapena ayi). Pakadapanda ubwino wa Allah ndi chifundo chake pa inu, ndithudi, mukadamtsatira satana kupatula ochepa.
Arapça tefsirler:
فَقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ لَا تُكَلَّفُ إِلَّا نَفۡسَكَۚ وَحَرِّضِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۖ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَكُفَّ بَأۡسَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۚ وَٱللَّهُ أَشَدُّ بَأۡسٗا وَأَشَدُّ تَنكِيلٗا
Choncho menya nkhondo pa njira ya Allah, suukukakamizidwa (za anthu ena) koma iwe mwini, ndipo akhwirizire Asilamu. Ndithu Allah angatsekereze mtopola wa omwe sadakhulupirire. Ndipo Allah Ngwaukali kwambiri pomenya nkhondo ndiponso Wolanga kwabasi.
Arapça tefsirler:
مَّن يَشۡفَعۡ شَفَٰعَةً حَسَنَةٗ يَكُن لَّهُۥ نَصِيبٞ مِّنۡهَاۖ وَمَن يَشۡفَعۡ شَفَٰعَةٗ سَيِّئَةٗ يَكُن لَّهُۥ كِفۡلٞ مِّنۡهَاۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ مُّقِيتٗا
Amene angampemphere (mnzake) pempho labwino (lothandizira pa zabwino) adzapeza gawo mmenemo. Ndipo amene angampemphelere pemphero loipa, adzapeza gawo m’zoipazo. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.[135]
[135] M’ndime iyi akuwalangiza anthu kuti azithandizana pa zabwino zokha. Azithandizana pa zochita ndi zonena. Munthu akokere anzake kuzinthu zabwino mmene angathere. lyenso mwini athandize ena pazinthu zabwino. Akachita izi adzalandira mphoto yaikulu kwa Allah.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا حُيِّيتُم بِتَحِيَّةٖ فَحَيُّواْ بِأَحۡسَنَ مِنۡهَآ أَوۡ رُدُّوهَآۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٍ حَسِيبًا
Ndipo pamene mwalonjeredwa; kulonjeredwa kwamtundu uliwonse (Salam) vomerani ndi malonje abwino oposa amenewo, kapena bwezani ofanana nawo. Ndithudi, Allah Ngowerengera chinthu chilichonse.
Arapça tefsirler:
ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۚ لَيَجۡمَعَنَّكُمۡ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ لَا رَيۡبَ فِيهِۗ وَمَنۡ أَصۡدَقُ مِنَ ٱللَّهِ حَدِيثٗا
Allah! Palibe wopembedzedwa mwa choonadi koma Iye basi. Ndithudi, adzakusonkhanitsani tsiku la chiweruziro lopanda chikaiko mwa ilo. Kodi ndani ali onena zoona kuposa Allah?
Arapça tefsirler:
۞ فَمَا لَكُمۡ فِي ٱلۡمُنَٰفِقِينَ فِئَتَيۡنِ وَٱللَّهُ أَرۡكَسَهُم بِمَا كَسَبُوٓاْۚ أَتُرِيدُونَ أَن تَهۡدُواْ مَنۡ أَضَلَّ ٱللَّهُۖ وَمَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ سَبِيلٗا
Kodi mwatani inu pokhala magulu awiri pa nkhani ya achiphamaso (achinyengo) pomwe Allah wawatembenuza chifukwa cha (zoipa) zomwe achita? Kodi mukufuna kuti mumuongole amene Allah wamlekelera kusokera? Ndipo amene Allah wamulekelera kusokera, simungathe kumpezera njira (yomuikira ku chilungamo).
Arapça tefsirler:
وَدُّواْ لَوۡ تَكۡفُرُونَ كَمَا كَفَرُواْ فَتَكُونُونَ سَوَآءٗۖ فَلَا تَتَّخِذُواْ مِنۡهُمۡ أَوۡلِيَآءَ حَتَّىٰ يُهَاجِرُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۚ فَإِن تَوَلَّوۡاْ فَخُذُوهُمۡ وَٱقۡتُلُوهُمۡ حَيۡثُ وَجَدتُّمُوهُمۡۖ وَلَا تَتَّخِذُواْ مِنۡهُمۡ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرًا
Ndipo akufuna kuti mukadakhala osakhulupirira monga momwe iwo sadakhulupirire tero kuti mukhale ofanana. Musawachite kukhala abwenzi mpaka asamukire panjira ya Allah. Koma ngati anyoza, agwireni ndi kuwapha paliponse mwawapeza (monga momwe akukuchitirani inu). Ndipo musamuyese mtetezi ngakhale mthandizi aliyense wa iwo.
Arapça tefsirler:
إِلَّا ٱلَّذِينَ يَصِلُونَ إِلَىٰ قَوۡمِۭ بَيۡنَكُمۡ وَبَيۡنَهُم مِّيثَٰقٌ أَوۡ جَآءُوكُمۡ حَصِرَتۡ صُدُورُهُمۡ أَن يُقَٰتِلُوكُمۡ أَوۡ يُقَٰتِلُواْ قَوۡمَهُمۡۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ لَسَلَّطَهُمۡ عَلَيۡكُمۡ فَلَقَٰتَلُوكُمۡۚ فَإِنِ ٱعۡتَزَلُوكُمۡ فَلَمۡ يُقَٰتِلُوكُمۡ وَأَلۡقَوۡاْ إِلَيۡكُمُ ٱلسَّلَمَ فَمَا جَعَلَ ٱللَّهُ لَكُمۡ عَلَيۡهِمۡ سَبِيلٗا
Kupatula omwe akugwirizana ndi anthu amene pali pangano pakati panu ndi iwo, kapena omwe akudza kwa inu uku zifuwa zawo zili zobanika kumenyana nanu, kapena kumenyana ndi anthu awo. (Oterewo musamenyane nawo). Ngati Allah akadafuna, akadawapatsa mphamvu yokugonjetserani, choncho akadakumenyani. Ngati atakupewani, osamenyana nanu ndipo nkukupatsani mtendere, ndiye kuti Allah sadakupangireni njira pa iwo (yakuti mumenyane nawo).
Arapça tefsirler:
سَتَجِدُونَ ءَاخَرِينَ يُرِيدُونَ أَن يَأۡمَنُوكُمۡ وَيَأۡمَنُواْ قَوۡمَهُمۡ كُلَّ مَا رُدُّوٓاْ إِلَى ٱلۡفِتۡنَةِ أُرۡكِسُواْ فِيهَاۚ فَإِن لَّمۡ يَعۡتَزِلُوكُمۡ وَيُلۡقُوٓاْ إِلَيۡكُمُ ٱلسَّلَمَ وَيَكُفُّوٓاْ أَيۡدِيَهُمۡ فَخُذُوهُمۡ وَٱقۡتُلُوهُمۡ حَيۡثُ ثَقِفۡتُمُوهُمۡۚ وَأُوْلَٰٓئِكُمۡ جَعَلۡنَا لَكُمۡ عَلَيۡهِمۡ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينٗا
Muzawapeza ena omwe akufuna kupeza chitetezo kwa inu ndi kupeza chitetezo kwa anthu awo. Nthawi iliyonse akabwezedwa ku ukafiri (ndi anzawo osakhulupirira), amagweramo mwamtheradi (nkuyamba kumenyananso ndi inu), ngati sadzipatula kwa inu ndipo osakupatsani mtendere ndi kutsekereza manja awo, agwireni ndi kuwapha paliponse pamene mwawapeza (monga momwe iwo akuchitira kwa inu) ndipo takupangirani chisonyezo choonekera pa iwo
Arapça tefsirler:
وَمَا كَانَ لِمُؤۡمِنٍ أَن يَقۡتُلَ مُؤۡمِنًا إِلَّا خَطَـٔٗاۚ وَمَن قَتَلَ مُؤۡمِنًا خَطَـٔٗا فَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖ وَدِيَةٞ مُّسَلَّمَةٌ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦٓ إِلَّآ أَن يَصَّدَّقُواْۚ فَإِن كَانَ مِن قَوۡمٍ عَدُوّٖ لَّكُمۡ وَهُوَ مُؤۡمِنٞ فَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖۖ وَإِن كَانَ مِن قَوۡمِۭ بَيۡنَكُمۡ وَبَيۡنَهُم مِّيثَٰقٞ فَدِيَةٞ مُّسَلَّمَةٌ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ وَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖۖ فَمَن لَّمۡ يَجِدۡ فَصِيَامُ شَهۡرَيۡنِ مُتَتَابِعَيۡنِ تَوۡبَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Ndipo sikoyenera kwa wokhulupirira kupha wokhulupilila (mnzake mwadala) pokhapokha mwangozi. Ndipo yemwe wapha wokhulupilila mwangozi, apereke ufulu kwa kapolo wa Chisilamu ndi dipo lomwe alipereke kwa ofedwawo pokhapokha akakana okha (amulowa mmalo a womwalilayo), monga m’njira ya sadaka. Ngati wophedwayo ndi mnansi wa adani anu pomwe ali wokhulupilila, perekani ufulu kwa kapolo wa Chisilamu, (palibenso dipo lina). Ngati wophedwayo ndi mmodzi wa anthu omwe pakati panu ndi iwo pali chipangano (chosamenyana nkhondo), ndiye kuti amulowammalo ake apatsidwe dipo; apatsidwenso ufulu kapolo wa Chisilamu. Ndipo ngati sadapeze (zoterozo), asale miyezi iwiri yotsatana. Iyo ndiyo njira yolapira (pa uchimo wotere) yochokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَقۡتُلۡ مُؤۡمِنٗا مُّتَعَمِّدٗا فَجَزَآؤُهُۥ جَهَنَّمُ خَٰلِدٗا فِيهَا وَغَضِبَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِ وَلَعَنَهُۥ وَأَعَدَّ لَهُۥ عَذَابًا عَظِيمٗا
Ndipo amene angaphe wokhulupilila mwadala, mphoto yake ndi Jahannam; mmenemo adzakhala nthawi yaitali. Ndipo Allah amkwiira ndi kumtembelera ndi kumkonzera chilango chachikulu.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا ضَرَبۡتُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَتَبَيَّنُواْ وَلَا تَقُولُواْ لِمَنۡ أَلۡقَىٰٓ إِلَيۡكُمُ ٱلسَّلَٰمَ لَسۡتَ مُؤۡمِنٗا تَبۡتَغُونَ عَرَضَ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا فَعِندَ ٱللَّهِ مَغَانِمُ كَثِيرَةٞۚ كَذَٰلِكَ كُنتُم مِّن قَبۡلُ فَمَنَّ ٱللَّهُ عَلَيۡكُمۡ فَتَبَيَّنُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Mukayenda pa njira ya Allah, musachite chinthu pokhapokha mutaonetsetsa bwino. Ndipo musanene kwa amene akukulonjerani Salamu (kuti): “Sindiwe wokhulupirira,” (nkumupha). Mukufuna zinthu zamdziko lapansi komatu kwa Allah kuli zopeza zambiri. Umo ndi momwe inunso mudalili kale; koma Allah adakuchitirani chifundo (choncho mudalowa m’Chisilamu. Penyetsetsani bwinobwino). Ndithu Allah Ngodziwa bwinobwino nkhani zonse zimene muchita.
Arapça tefsirler:
لَّا يَسۡتَوِي ٱلۡقَٰعِدُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ غَيۡرُ أُوْلِي ٱلضَّرَرِ وَٱلۡمُجَٰهِدُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡۚ فَضَّلَ ٱللَّهُ ٱلۡمُجَٰهِدِينَ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ عَلَى ٱلۡقَٰعِدِينَ دَرَجَةٗۚ وَكُلّٗا وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡحُسۡنَىٰۚ وَفَضَّلَ ٱللَّهُ ٱلۡمُجَٰهِدِينَ عَلَى ٱلۡقَٰعِدِينَ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Sangafanane okhulupirira omwe akukhala osapita kunkhondo pomwe sali ovutika, ndi amene akumenya nkhondo yoyera pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo. Allah wawatukula pa ubwino ndi pa nyota amene akuchita Jihâd ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo kuposa okhala. Koma onsewo Allah wawalonjeza zabwino. Koma wawapambanitsa ochita Jihâd malipiro aakulu kuposa ongokhala.
Arapça tefsirler:
دَرَجَٰتٖ مِّنۡهُ وَمَغۡفِرَةٗ وَرَحۡمَةٗۚ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمًا
Adzapata nyota zazikulu zochokera kwa Iye ndi chikhululuko ndi chisoni. Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ تَوَفَّىٰهُمُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ ظَالِمِيٓ أَنفُسِهِمۡ قَالُواْ فِيمَ كُنتُمۡۖ قَالُواْ كُنَّا مُسۡتَضۡعَفِينَ فِي ٱلۡأَرۡضِۚ قَالُوٓاْ أَلَمۡ تَكُنۡ أَرۡضُ ٱللَّهِ وَٰسِعَةٗ فَتُهَاجِرُواْ فِيهَاۚ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَسَآءَتۡ مَصِيرًا
Ndithudi amene angelo atenga miyoyo yawo, ali odzichitira okha zoipa (posasamuka ku Makka), adzawauza kuti: “Mudachitanji (pachipembedzo chanu?)” Iwo adzati: “Tidali ofooka ndi oponderezedwa padziko; (choncho sitidathe kuchita mapemphero athu).” (Angelo) adzati: “Kodi dziko la Allah silidali lotambasuka kotero kuti inu nkusamukira kwina m’menemo?” Iwowo malo awo ndi Jahannam. Taonani kuipa kwa malo obwerera.[136]
[136] (Ndime 97-99) Kalelo Mtumiki (s.a.w) atasamukira ku Madina pamodzi ndi omtsatira ake, Asilamu adawalamula kuti asamukire ku Madinako kusiya nyumba zawo, chuma chawo, abale awo ndi ana awo. Izi zidali chonchi chifukwa iwo akanakhalabe m’midzi yawo pansi pautsogoleri wa anthu osakhulupilira sakanatha kukwaniritsa malamulo a Chisilamu. Tero Chisilamu chake sichikanakhala ndi ntchito. Ndipo Chisilamu chopanda ntchito si Chisilamunso. Tero nchifukwa chake apa akuwadzudzula amene sanasamuke kuti adzafa ndi imfa yoipa kupatula okhawo amene sanapeze njira yosamukira ku Madina chifukwa chakufooka kwa matupi awo. Amenewa madandaulo awo akhoza kuwavomera. Koma chachikulu nkuti ayesetse kusamukira ku Madina.
Arapça tefsirler:
إِلَّا ٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلرِّجَالِ وَٱلنِّسَآءِ وَٱلۡوِلۡدَٰنِ لَا يَسۡتَطِيعُونَ حِيلَةٗ وَلَا يَهۡتَدُونَ سَبِيلٗا
Kupatula omwe adali ofooka kwenikweni amuna, akazi ndi ana omwe sangathe kuchita ndale yamtundu uliwonse, ndipo sangathe kulondola njira (yonkera ku Madina).
Arapça tefsirler:
فَأُوْلَٰٓئِكَ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَعۡفُوَ عَنۡهُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَفُوًّا غَفُورٗا
Choncho iwo ndithudi Allah angawafafanizire machimo, pakuti Allah Ngofafaniza machimo, Wokhululuka.
Arapça tefsirler:
۞ وَمَن يُهَاجِرۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ يَجِدۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُرَٰغَمٗا كَثِيرٗا وَسَعَةٗۚ وَمَن يَخۡرُجۡ مِنۢ بَيۡتِهِۦ مُهَاجِرًا إِلَى ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ ثُمَّ يُدۡرِكۡهُ ٱلۡمَوۡتُ فَقَدۡ وَقَعَ أَجۡرُهُۥ عَلَى ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo amene angasamuke pa njira ya Allah (chifukwa cha chipembedzo chake,) apeza malo ambiri m’dzikomo othawira ndikupeza bwino. Ndipo amene angatuluke m’nyumba mwake kuti asamuke chifukwa cha Allah ndi Mtumiki Wake, kenako nkumpeza imfa (m’njira), ndithu malipiro ake atsimikizika kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[137]
[137] Apa akuwalimbikitsa za kusamuka ndi kuwauza kuti kumene akupitako akapeza bwino. Akuwalimbikitsanso okalamba ndi odwala kuti asamuke. Ngati atafera pa njira kuwerengedwa kuti adasamukabe ndipo adzapeza mphoto yonga ya yemwe adasamuka nkukakhala ku Madina pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kukathandiza kukamenya nkhondo yoteteza Chisilamu kwa adani. Ndichimodzomodzi munthu akapita ku Makka kukachita Hajj ndipo nkumwalira Hajjiyo asanachite, kapena asanamalize zina zofunika pa Hajj, kwa Allah amamuwerenga kuti wachita mapemphero a Hajj. Komabe abale ake akhoza kukamchitiranso mapemphero a Hajj.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا ضَرَبۡتُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَلَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٌ أَن تَقۡصُرُواْ مِنَ ٱلصَّلَوٰةِ إِنۡ خِفۡتُمۡ أَن يَفۡتِنَكُمُ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْۚ إِنَّ ٱلۡكَٰفِرِينَ كَانُواْ لَكُمۡ عَدُوّٗا مُّبِينٗا
Ndipo ngati mukuyenda pa dziko, sikulakwa kwa inu kufupikitsa Swala ngati mukuopa kuti angakusokonezeni omwe sadakhulupirire. Ndithudi, osakhulupirira ndi adani anu oonekera.[138]
[138] Pamene Asilamu adawalamulira zakusamuka, adawafupikitsira Swala chifukwa cha mavuto am’njira monga kuti (a) Swala zokhala ndi raka zinayi akhoza kuziswali ndi raka ziwiriziwiri. (b) Akhoza kuswali katatu kokha patsiku m’malo mwakasanu. Izi zili motere: Swala ya Dhuhr nkuiphatikiza pamodzi ndi Swala ya Asr; kuzipemphera panthawi ya Dhuhr kapena kuzipemphera panthawi ya Asr. Swala ya Maghrib nkuipemphera pamodzi ndi Swala ya Isha. Adzayamba kupemphera Swala ya Maghrib raka zitatu kenako nkupemphera Isha raka ziwiri. Koma Swala ya Subh yokha njomwe imapempheredwa payokha ndiponso m’nthawi yake. Lamuloli analikhazikitsa pamene Asilamu adali ndi mantha ndi masautso am’njira. Ndipo lidasiidwa momwemo losasinthika mpaka lero m’nthawi yomwe anthu akukwera galimoto, sitima ndi ndege.
Arapça tefsirler:
وَإِذَا كُنتَ فِيهِمۡ فَأَقَمۡتَ لَهُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَلۡتَقُمۡ طَآئِفَةٞ مِّنۡهُم مَّعَكَ وَلۡيَأۡخُذُوٓاْ أَسۡلِحَتَهُمۡۖ فَإِذَا سَجَدُواْ فَلۡيَكُونُواْ مِن وَرَآئِكُمۡ وَلۡتَأۡتِ طَآئِفَةٌ أُخۡرَىٰ لَمۡ يُصَلُّواْ فَلۡيُصَلُّواْ مَعَكَ وَلۡيَأۡخُذُواْ حِذۡرَهُمۡ وَأَسۡلِحَتَهُمۡۗ وَدَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَوۡ تَغۡفُلُونَ عَنۡ أَسۡلِحَتِكُمۡ وَأَمۡتِعَتِكُمۡ فَيَمِيلُونَ عَلَيۡكُم مَّيۡلَةٗ وَٰحِدَةٗۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن كَانَ بِكُمۡ أَذٗى مِّن مَّطَرٍ أَوۡ كُنتُم مَّرۡضَىٰٓ أَن تَضَعُوٓاْ أَسۡلِحَتَكُمۡۖ وَخُذُواْ حِذۡرَكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا
Ndipo ngati uli pamodzi (ndi Asilamu pankhondo) ndikuwatsogolera Swala, ndiye kuti gulu limodzi la iwo liimilire pamodzi ndi iwe ndikupemphera uku atagwirizira zida zawo. Ndipo akamaliza kulambira kwawo, apite kumbuyo kwanu (kuti akulondereni) ndipo lidze gulu lina lomwe silidapemphere, lipemphere nawe pamodzi; nawonso achenjere ndikugwirizira zida zawo (nkupemphera), chifukwa chakuti omwe sadakhulupirire akufuna kuti mutanyalanyaza zida zanu ndi katundu wanu angokuukirani nthawi imodzi. Koma sikulakwa kwa inu mutaika pansi zida zanu chifukwa chakuvutitsidwa ndi mvula kapena ngati mukudwala. Koma chenjeranaoni. Ndithudi Allah wawakonzera chilango choyalutsa osakhulupirira.[139]
[139] Swala yopemphera pagulu (jamaa) akuilimbikitsa zedi ngakhale kuti anthu ali pakati pa nkhondo. Ngati nthawi ya Swala yakwana akuwauza kuti apemphere pagulu, koma asapemphere onse nthawi imodzi. Anthuwo agawike m’magulu awiri. Gulu lina liyang’ane komwe kuli adani, ndipo gulu lina likhale likupemphera pamodzi ndi (Imamu) mtsogoleri wawo. Komatu Swala akunkhondo amaswali raka ziwiriziwiri (Swala iliyonse) kupatula Swala ya Magharibi. Tsono Imamu adzapemphera raka imodzi ndi awo omwe akupemphera nawo. Akaimilira kuti apemphere raka yachiwiri, aja omwe anali kupemphera naye aimilire ndi kupemphera raka yotsalayo mwachangu atamsiya imamu ali chiimilire. Ndipo apite kukalowa m’malo mwa anzawo omwe anali kuyang’ana komwe kuli adani. Tsono anzawowo adze nkudzapemphera ndi Imamu. Imamu akamaliza raka yake yachiwiri, iwo aimilire nkumaliza raka yawo yachiwiri. Komatu popempherapo zida zawo zikhale atazikoleka m’matupi mwawo pokhapokha ngati pali zifukwa zoikitsa zidazo pansi, zomwe azitchula kumapeto a ndimeyo
Arapça tefsirler:
فَإِذَا قَضَيۡتُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ قِيَٰمٗا وَقُعُودٗا وَعَلَىٰ جُنُوبِكُمۡۚ فَإِذَا ٱطۡمَأۡنَنتُمۡ فَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَۚ إِنَّ ٱلصَّلَوٰةَ كَانَتۡ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ كِتَٰبٗا مَّوۡقُوتٗا
Mukamaliza Swala, pitirizani kumkumbukira Allah muli chiimire, chikhalire kapena mutagona chammbali. Ngati mutapeza chitetezo (chifukwa chakuti nkhondo palibe), pempherani Swala zanu mwa chilamulo. Ndithudi, Swala ndilamulo lokhala ndi nthawi kwa okhulupirira.[140]
[140] Nkofunika nthawi zonse Msilamu kukumbukira Allah.osati panthawi yokha yopemphera koma amkumbukire m’chikhalidwe chake chonse ndi m’zochita zake zonse. Nthawi zonse apewe zomwe Allah waletsa ndi kutsata malamulo ake.
Arapça tefsirler:
وَلَا تَهِنُواْ فِي ٱبۡتِغَآءِ ٱلۡقَوۡمِۖ إِن تَكُونُواْ تَأۡلَمُونَ فَإِنَّهُمۡ يَأۡلَمُونَ كَمَا تَأۡلَمُونَۖ وَتَرۡجُونَ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا يَرۡجُونَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمًا
Ndipo musachite ulesi kutsata anthu (omwe ndi adani), ngati mukumva kupweteka, iwonso akumva kupweteka monga momwe inu mukumvera kupweteka. Koma inu mukuyembekezera kwa Allah chomwe iwo sakuyembekezera. Ndipotu Allah Ngodziwa, Ngwanzeru.[141]
[141] Apa akuwalamula Asilamu kuti amenyere chipembedzo chawo ngakhale atapeza mavuto amtundumtundu. Chifukwa chomwe akupezera mavutowo nchachikulu zedi kuposa mavutowo palibe chinthu chachikulu chimene munthu angachipeze chabe popanda kuvutikira.
Arapça tefsirler:
إِنَّآ أَنزَلۡنَآ إِلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ بِٱلۡحَقِّ لِتَحۡكُمَ بَيۡنَ ٱلنَّاسِ بِمَآ أَرَىٰكَ ٱللَّهُۚ وَلَا تَكُن لِّلۡخَآئِنِينَ خَصِيمٗا
Ndithudi, takuvumbulutsira buku mwa choonadi kuti uweruzire pakati pa anthu, monga momwe Allah wakuphunzitsira. Ndipo usakhale mtetezi wa achinyengo.
Arapça tefsirler:
وَٱسۡتَغۡفِرِ ٱللَّهَۖ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo mpemphe chikhululuko Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha.
Arapça tefsirler:
وَلَا تُجَٰدِلۡ عَنِ ٱلَّذِينَ يَخۡتَانُونَ أَنفُسَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ مَن كَانَ خَوَّانًا أَثِيمٗا
Ndipo usawaikile kumbuyo omwe akudzichitira okha chinyengo. Allah sakonda yemwe ali wachinyengo, wamachimo.
Arapça tefsirler:
يَسۡتَخۡفُونَ مِنَ ٱلنَّاسِ وَلَا يَسۡتَخۡفُونَ مِنَ ٱللَّهِ وَهُوَ مَعَهُمۡ إِذۡ يُبَيِّتُونَ مَا لَا يَرۡضَىٰ مِنَ ٱلۡقَوۡلِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِمَا يَعۡمَلُونَ مُحِيطًا
Akudzibisa kwa anthu (pochita za machimo) koma sakuzibisa kwa Allah pomwe Iye adali nawo pamodzi pamene adali kupangana usiku mawu osakondweretsa. Allah akudziwa bwinobwino zimene akuchita.[142]
[142] Achiphamaso amabisa zochita zawo kwa anthu kuti asazione. Koma salabadira kuonedwa ndi Allah pomwe Allah Njemwe adzawalipira. Pomwe Allah akudziwa zonse zimene zikuyenda m’mitima mwawo ndiponso akumva ndi kuziona zonse zimene akuchita. Kunali kofunika kwa iwo kumuopa Allah amene ali ndi mphamvu zochitira chilichonse chimene wafuna.
Arapça tefsirler:
هَٰٓأَنتُمۡ هَٰٓؤُلَآءِ جَٰدَلۡتُمۡ عَنۡهُمۡ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا فَمَن يُجَٰدِلُ ٱللَّهَ عَنۡهُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ أَم مَّن يَكُونُ عَلَيۡهِمۡ وَكِيلٗا
Taonani! Inu ndi amene mwaayikira kumbuyo pa moyo wa pa dziko lapansi. Kodi ndani amene adzatsutsana ndi Allah pa iwo tsiku lachimaliziro, kapena ndani adzakhale mtetezi wawo.[143]
[143] M’ndime iyi Allah akuletsa anthu kuti asakhalire kumbuyo anthu oipa koma awaleke kuti awalange chifukwa cha zoipa zawo ndi kuti amene adamuchitirapo zoipa apeze bwino muntima mwake. Choncho aweruzi amilandu achenjere kukhalira kumbuyo anthu oipa omwe ali nawo chitsimikizo kuti adachenjelera anzawo. Asaone ulemelero wa munthu mmene ulili ngakhale ali ndi chuma chotani. Koma m’malomwake akhalire kumbuyo amene ali oponderezedwa. Akatero adzapeza mphoto yomwe Allah walonjeza chifukwa cha kusonyeza choonadi poyera. Aweruzi akagwira njira imeneyi ndiye kuti adzapambana pano padziko lapansi mpaka patsiku la chiweruziro.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَعۡمَلۡ سُوٓءًا أَوۡ يَظۡلِمۡ نَفۡسَهُۥ ثُمَّ يَسۡتَغۡفِرِ ٱللَّهَ يَجِدِ ٱللَّهَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo amene angachite choipa (povutitsa ena), kapena kudzichitira yekha zoipa, kenako nkupempha chikhululuko kwa Allah, adzampeza Allah ali Wokhululuka kwabasi, Wachisoni chosatha. [144]
[144] Allah akuwalimbikitsa ochimwa: Kuti (a) atembenukire kwa Iye mwachangu ndi kusiya zimene akuchitazo. (b) Atsimikize mu mtima kuti sadzachitanso uchimowo. (c) Adandaule pa uchimo umene adauchitawo. (d) Awabwezere eni zinthu zomwe adazitenga mwachinyengo. (e) Akawapemphe kuti awakhululukire. Akakwaniritsa zonsezi ndiye kuti kulapa kwawo Allah akuvomera.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَكۡسِبۡ إِثۡمٗا فَإِنَّمَا يَكۡسِبُهُۥ عَلَىٰ نَفۡسِهِۦۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Ndipo amene angachite tchimo, ndiye kuti akudzichitira yekha. Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.[145]
[145] M’ndime iyi akuti munthu wochitira anthu anzake zoipa.akudzipha yekha pakuti Allah sadzamleka koma amkhaulitsa pompano pa dziko lapansi kapena pakutha kwa dziko.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَكۡسِبۡ خَطِيٓـَٔةً أَوۡ إِثۡمٗا ثُمَّ يَرۡمِ بِهِۦ بَرِيٓـٔٗا فَقَدِ ٱحۡتَمَلَ بُهۡتَٰنٗا وَإِثۡمٗا مُّبِينٗا
Ndipo amene angachite cholakwa (chaching’ono) kapena tchimo (lalikulu) kenako nkumponyera nalo yemwe sadalakwe (momunamizira), ndithudi wasenza bodza lamkunkhuniza ndi uchimo woonekera.[146]
[146] Pali anthu ena amene amaukwera uchimo. Kenako nkumnamizira wina wake. Munthu wamakhalidwe awa, chiweruzo chake chidzakhala choopsa tsiku lachimaliziro, ngakhale wadzipulumutsa pano pa dziko lapansi chifukwa chakuthyathyalika kwake. Kapena pompano pa dziko lapansi amachiona chomwe chinameta nkhanga mpala.
Arapça tefsirler:
وَلَوۡلَا فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ وَرَحۡمَتُهُۥ لَهَمَّت طَّآئِفَةٞ مِّنۡهُمۡ أَن يُضِلُّوكَ وَمَا يُضِلُّونَ إِلَّآ أَنفُسَهُمۡۖ وَمَا يَضُرُّونَكَ مِن شَيۡءٖۚ وَأَنزَلَ ٱللَّهُ عَلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَعَلَّمَكَ مَا لَمۡ تَكُن تَعۡلَمُۚ وَكَانَ فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكَ عَظِيمٗا
Ndipo pakadapanda ubwino wa Allah ndi chisoni chake pa iwe, ndithudi, gulu limodzi la iwo likadalinga kukusokeretsa. Ndipo iwo palibe yemwe akadamsokeretsa koma iwo okha basi. Ndipo sangathe kukuvutitsa ndi chilichonse. Ndipo Allah wakuvumbulutsira buku, kudzanso luntha. Ndipo wakuphunzitsa zomwe sudali kuzidziwa. Ndipo ubwino wa Allah umene uli pa iwe ngwaukulu zedi.[147]
[147] Apa Allah akunena kuti palibe chisomo chimene Allah wapatsa munthu chachikulu ndi chopindulitsa kuposa luntha. Chilichonse chabwino cha pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro chimapezeka chifukwa cha kudziwa zinthu. Qur’an yonse ndi hadisi za Mtumiki zikulimbikitsa zakufunafuna luntha lodziwira zinthu zakuti zimkonzere munthu za dziko lapansi ndi za tsiku lachimaliziro, kotero kuti Qur’an ndi hadisizo zikunena kuti munthu apite kunja kunka nafunafuna maphunziro.
Arapça tefsirler:
۞ لَّا خَيۡرَ فِي كَثِيرٖ مِّن نَّجۡوَىٰهُمۡ إِلَّا مَنۡ أَمَرَ بِصَدَقَةٍ أَوۡ مَعۡرُوفٍ أَوۡ إِصۡلَٰحِۭ بَيۡنَ ٱلنَّاسِۚ وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ ٱبۡتِغَآءَ مَرۡضَاتِ ٱللَّهِ فَسَوۡفَ نُؤۡتِيهِ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Palibe ubwino m’zambiri zimene akunong’onezana kupatula amene akulamulira ena kupereka sadaka, kapena kuchita zabwino, kapenanso kuyanjanitsa pakati pa anthu (pakunong’onezana mawu). Amene angachite zimenezi, chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah, tidzampatsa malipiro aakulu.
Arapça tefsirler:
وَمَن يُشَاقِقِ ٱلرَّسُولَ مِنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُ ٱلۡهُدَىٰ وَيَتَّبِعۡ غَيۡرَ سَبِيلِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ نُوَلِّهِۦ مَا تَوَلَّىٰ وَنُصۡلِهِۦ جَهَنَّمَۖ وَسَآءَتۡ مَصِيرًا
Ndipo amene anyoza Mtumiki pambuyo pomuonekera chiongoko, nkutsata njira yosakhala ya okhulupirira, timtembenuzira kumene watembenukira mwini wakeko. Ndipo tidzamulowetsa ku Jahannam. Taonani kuipa malo ofikira.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَغۡفِرُ أَن يُشۡرَكَ بِهِۦ وَيَغۡفِرُ مَا دُونَ ذَٰلِكَ لِمَن يَشَآءُۚ وَمَن يُشۡرِكۡ بِٱللَّهِ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا
Ndithudi, Allah sakhululuka (uchimo) womphatikiza ndi chinthu china, (pochiyesa kuti ndi mnzake wa Allah). Koma Iye amakhululukira machimo ena omwe sali amenewo kwa yemwe wamfuna. Ndipo yemwe angamphatikize Allah (ndi milungu yabodza), ndithudi, wasokera kusokera konka nako kutali (ndi njira yachoonadi).
Arapça tefsirler:
إِن يَدۡعُونَ مِن دُونِهِۦٓ إِلَّآ إِنَٰثٗا وَإِن يَدۡعُونَ إِلَّا شَيۡطَٰنٗا مَّرِيدٗا
Sapembedza Allah koma mafano achikazi, ndiponso sapembedza china koma satana wonyoza (wamachimo)
Arapça tefsirler:
لَّعَنَهُ ٱللَّهُۘ وَقَالَ لَأَتَّخِذَنَّ مِنۡ عِبَادِكَ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا
(Yemwe) Allah adamtembelera. Ndipo iye (satana) adati (kwa Allah): “Ndithudi, ndikadzipezera gawo lodziwika mwa akapolo anu.”[148]
[148] Iblis pamene adampirikitsa kumwamba iye adauza Allah kuti akazikometsera zolengedwa zake machimo. Allah adamuuza kuti sangathe kuzisokereza mwamphamvu, mozikakamiza, zifune zisafune. Aliyense amene akamtsata ndiye kuti akamtsata mwachifuniro chake. Sikuti mogonjetsedwa ndi mphamvu za satana kotero kuti iye sangathe kulimbana naye iyayi. Satana alibe mphamvu zokakamizira anthu.
Arapça tefsirler:
وَلَأُضِلَّنَّهُمۡ وَلَأُمَنِّيَنَّهُمۡ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُبَتِّكُنَّ ءَاذَانَ ٱلۡأَنۡعَٰمِ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُغَيِّرُنَّ خَلۡقَ ٱللَّهِۚ وَمَن يَتَّخِذِ ٱلشَّيۡطَٰنَ وَلِيّٗا مِّن دُونِ ٱللَّهِ فَقَدۡ خَسِرَ خُسۡرَانٗا مُّبِينٗا
“Ndipo ndikawasokeretsa ndi kuwapatsa ziyembekezo (zabodza) ndithu ndikawalamula kuti azikadula makutu a ziweto, ndipo ndikawalamulanso kuti azikasintha chilengedwe cha Allah.” Ndipo amene angamulole satana kukhala mtetezi wake kusiya Allah, ndiye kuti wataika koonekera.[149]
[149] (1) Kukhala ndi chiyembekezo choti Allah adzawakhululukira pakuti iye ngokhululuka, Ngwachifundo. (2) Kuti ukachita zakutizakuti kapena ukawerenga duwa yakutiyakuti machimo ako onse adzakufafanizira ngakhale kuti udakwatula zinthu za anthu. (3) Kuti wolemekezeka uje adzatiwombola ngati tilumikizana naye. (4) Kuti mneneri wakutiwakuti adzaitana omtsatira ake kuti akalowe ku Munda wa mtendere. (5) Kuti Mtumiki sadzakhala wokondwa kuona anthu ake akuponyedwa ku Moto. (6) Kukhala ndi chiyembekezo choti ngati munthu ndiwe Msilamu basi sukalowa ku Jahannam. Ndipo satanayu amanyenganso Akhrisitu kuti ngati akhulupilira Isa (Yesu) basi sakalowa ku Moto. Ndipo Ayuda amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati akhulupilira m’chipembedzo cha chiyuda sakalowa ku Moto. Nawonso opembedza moto ndi Abudha amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati atsata chibudha basi apulumuka.
Arapça tefsirler:
يَعِدُهُمۡ وَيُمَنِّيهِمۡۖ وَمَا يَعِدُهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ إِلَّا غُرُورًا
(Satana) akuwalonjeza ndikuwapatsa chiyembekezo (pa zinthu zomwe sizingachitike). Ndithudi, satana sawalonjeza china koma chinyengo basi.
Arapça tefsirler:
أُوْلَٰٓئِكَ مَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُ وَلَا يَجِدُونَ عَنۡهَا مَحِيصٗا
Iwowo malo awo ndi ku Jahannam ndipo sadzapeza pothawira kutuluka mmenemo.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ سَنُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ وَعۡدَ ٱللَّهِ حَقّٗاۚ وَمَنۡ أَصۡدَقُ مِنَ ٱللَّهِ قِيلٗا
Ndipo omwe akhulupirira ndi kumachita zabwino, tidzawalowetsa ku Minda yomwe pansi (ndi patsogolo) pake mitsinje ikuyenda. Adzakhala m’menemo muyaya. Ili ndilonjezo loona la Allah. Kodi ndani woona ponena kuposa Allah?
Arapça tefsirler:
لَّيۡسَ بِأَمَانِيِّكُمۡ وَلَآ أَمَانِيِّ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِۗ مَن يَعۡمَلۡ سُوٓءٗا يُجۡزَ بِهِۦ وَلَا يَجِدۡ لَهُۥ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
(Kulowa ku Munda wamtendere) sikuli pa kukhumba kwanu ngakhalenso pa kukhumba kwa anthu a buku (Ayuda ndi Akhrisitu). Amene angachite choipa, adzalipidwa (nacho), ndipo sadzapeza mtetezi ngakhale mpulumutsi kupatula Allah.
Arapça tefsirler:
وَمَن يَعۡمَلۡ مِنَ ٱلصَّٰلِحَٰتِ مِن ذَكَرٍ أَوۡ أُنثَىٰ وَهُوَ مُؤۡمِنٞ فَأُوْلَٰٓئِكَ يَدۡخُلُونَ ٱلۡجَنَّةَ وَلَا يُظۡلَمُونَ نَقِيرٗا
Ndipo amene angachite ntchito zabwino, mwamuna kapena mkazi, pomwe iye ali wokhulupirira, iwo ndiamene adzalowa ku Munda wamtendere. Ndipo sadzaponderezedwa pa chilichonse, ngakhale chochepetsetsa kwambiri ngati kamphako ka nthangala ya tende.
Arapça tefsirler:
وَمَنۡ أَحۡسَنُ دِينٗا مِّمَّنۡ أَسۡلَمَ وَجۡهَهُۥ لِلَّهِ وَهُوَ مُحۡسِنٞ وَٱتَّبَعَ مِلَّةَ إِبۡرَٰهِيمَ حَنِيفٗاۗ وَٱتَّخَذَ ٱللَّهُ إِبۡرَٰهِيمَ خَلِيلٗا
Kodi ndani yemwe ali ndi chipembedzo chabwino choposa yemwe walunjika nkhope yake kwa Allah, iye ali wochita zabwino ndipo akutsata njira ya Ibrahim woona pa chikhulupiliro. Ndipo Allah adasankha Ibrahim kukhala bwenzi.
Arapça tefsirler:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٖ مُّحِيطٗا
Ndipo zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah; ndipo Allah ndi amene wazungulira chinthu chilichonse kuchidziwa.
Arapça tefsirler:
وَيَسۡتَفۡتُونَكَ فِي ٱلنِّسَآءِۖ قُلِ ٱللَّهُ يُفۡتِيكُمۡ فِيهِنَّ وَمَا يُتۡلَىٰ عَلَيۡكُمۡ فِي ٱلۡكِتَٰبِ فِي يَتَٰمَى ٱلنِّسَآءِ ٱلَّٰتِي لَا تُؤۡتُونَهُنَّ مَا كُتِبَ لَهُنَّ وَتَرۡغَبُونَ أَن تَنكِحُوهُنَّ وَٱلۡمُسۡتَضۡعَفِينَ مِنَ ٱلۡوِلۡدَٰنِ وَأَن تَقُومُواْ لِلۡيَتَٰمَىٰ بِٱلۡقِسۡطِۚ وَمَا تَفۡعَلُواْ مِنۡ خَيۡرٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِهِۦ عَلِيمٗا
Ndipo akukufunsa zomwe zikukhudza azimayi nena: “Allah akukuuzani nkhani za iwo ndi zomwe zikuwerengedwa kwa inu m’buku (ili) za akazi amasiye omwe simukuwapatsa (chiwongo chawo) chomwe chidalamulidwa kwa iwo, komabe mukufuna kuwakwatira, ndi za ana omwe ali ofooka ndi oponderezedwa; ndipo (akukuuzani) kuti limbikirani kuwayang’anira ana amasiye mwachilungamo. Ndipo chabwino chilichonse chimene muchita, Allah akuchidziwa.[150]
[150] Mukuuzidwa nkhanizi zomwe akuwerengerani mu ndime ya 2 ndi 12 M’sura yomweyi.
Arapça tefsirler:
وَإِنِ ٱمۡرَأَةٌ خَافَتۡ مِنۢ بَعۡلِهَا نُشُوزًا أَوۡ إِعۡرَاضٗا فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِمَآ أَن يُصۡلِحَا بَيۡنَهُمَا صُلۡحٗاۚ وَٱلصُّلۡحُ خَيۡرٞۗ وَأُحۡضِرَتِ ٱلۡأَنفُسُ ٱلشُّحَّۚ وَإِن تُحۡسِنُواْ وَتَتَّقُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا
Ndipo ngati mkazi ataona kwa mwamuna wake nkhanza ndi kumusala, palibe kulakwa pa iwo kuyanjana pakati pawo mwachimvano. Ndipo chimvano ndichabwino. (Munthu aliyense amaumilira chimene afuna) chifukwa chakuti mitima ya anthu imaumilira umbombo. Koma ngati muchita zabwino ndi kuopa Allah, ndithudi, Allah Ngodziwa nkhani zanu zonse zomwe muchita.
Arapça tefsirler:
وَلَن تَسۡتَطِيعُوٓاْ أَن تَعۡدِلُواْ بَيۡنَ ٱلنِّسَآءِ وَلَوۡ حَرَصۡتُمۡۖ فَلَا تَمِيلُواْ كُلَّ ٱلۡمَيۡلِ فَتَذَرُوهَا كَٱلۡمُعَلَّقَةِۚ وَإِن تُصۡلِحُواْ وَتَتَّقُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo inu simungathe kuchita chilungamo (chenicheni) pakati pa akazi ngakhale mutayesetsa chotani. Koma musapendekere (mbali imodzi); kupendekera kwathunthu kotero kuti nkumusiya (yemwe simukumfunayo) ngati kuti wapachikidwa (osadziwika kuti ngokwatiwa kapena ayi). Ndipo ngati mutayanjana ndi kuopa Allah (zingakhale bwino). Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.
Arapça tefsirler:
وَإِن يَتَفَرَّقَا يُغۡنِ ٱللَّهُ كُلّٗا مِّن سَعَتِهِۦۚ وَكَانَ ٱللَّهُ وَٰسِعًا حَكِيمٗا
Koma ngati atalekana, Allah angalemeretse aliyense wa iwo kuchokera m’zabwino zake zochuluka ndipo Allah ali nazo zambiri, Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ وَلَقَدۡ وَصَّيۡنَا ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ مِن قَبۡلِكُمۡ وَإِيَّاكُمۡ أَنِ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَۚ وَإِن تَكۡفُرُواْ فَإِنَّ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ غَنِيًّا حَمِيدٗا
Zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah. Ndithudi, tidawalangiza omwe adapatsidwa buku patsogolo panu ndi inunso kuti muopeni Allah. Koma ngati mungakane, ndithudi, zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah. Ndipo Allah Ngokhupuka kwabasi Wotamandidwa.
Arapça tefsirler:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلًا
Zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah; ndipo Allah akukwana kukhala Mtetezi (kwa anthu Ake).
Arapça tefsirler:
إِن يَشَأۡ يُذۡهِبۡكُمۡ أَيُّهَا ٱلنَّاسُ وَيَأۡتِ بِـَٔاخَرِينَۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ ذَٰلِكَ قَدِيرٗا
Ngati atafuna, akuchotsani, inu anthu, ndi kubweretsa ena. Ndipo Allah ali Wokhoza pazimenezo.
Arapça tefsirler:
مَّن كَانَ يُرِيدُ ثَوَابَ ٱلدُّنۡيَا فَعِندَ ٱللَّهِ ثَوَابُ ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ سَمِيعَۢا بَصِيرٗا
Amene afuna mphoto ya dziko lapansi, (afunefune kwa Allah). Kwa Allah ndikumene kuli mphoto ya pa dziko lapansi ndi ya tsiku lachimaliziro. Ndipo Allah Ngwakumva, Ngopenya.
Arapça tefsirler:
۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُونُواْ قَوَّٰمِينَ بِٱلۡقِسۡطِ شُهَدَآءَ لِلَّهِ وَلَوۡ عَلَىٰٓ أَنفُسِكُمۡ أَوِ ٱلۡوَٰلِدَيۡنِ وَٱلۡأَقۡرَبِينَۚ إِن يَكُنۡ غَنِيًّا أَوۡ فَقِيرٗا فَٱللَّهُ أَوۡلَىٰ بِهِمَاۖ فَلَا تَتَّبِعُواْ ٱلۡهَوَىٰٓ أَن تَعۡدِلُواْۚ وَإِن تَلۡوُۥٓاْ أَوۡ تُعۡرِضُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Khalani oimiritsa chilungamo, opereka umboni chifukwa cha Allah; ngakhale kuti ubwere ndi masautso kwa inu, kapena kwa makolo anu, kapena kwa abale anu, ngakhale ali olemera kapena osauka, (musayang’ane zimenezo). Allah ndiye woyenera kuyang’ana za awiriwo. Choncho musatsate zilakolako ndi kusiya chilungamo. Ngati mukhotetsa (umboni), kapena kupewa (kupereka umboni) ndithudi nkhani zonse zomwe mukuchita Allah akuzidziwa.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ ءَامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلَّذِي نَزَّلَ عَلَىٰ رَسُولِهِۦ وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلَّذِيٓ أَنزَلَ مِن قَبۡلُۚ وَمَن يَكۡفُرۡ بِٱللَّهِ وَمَلَٰٓئِكَتِهِۦ وَكُتُبِهِۦ وَرُسُلِهِۦ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا
E inu amene mwakhulupirira! Khulupirirani Allah ndi Mtumiki Wake, ndi buku lomwe analivumbulutsa pa Mtumiki Wake, ndi mabuku omwe adawavumbulutsa kale. Ndipo amene akane Allah, angelo Ake, mabuku Ake, atumiki Ake ndi tsiku lachimaliziro, ndiye kuti wasokera; kusokera konkera nako kutali.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ ثُمَّ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ ثُمَّ ٱزۡدَادُواْ كُفۡرٗا لَّمۡ يَكُنِ ٱللَّهُ لِيَغۡفِرَ لَهُمۡ وَلَا لِيَهۡدِيَهُمۡ سَبِيلَۢا
Ndithudi, amene adakhulupirira, kenako nkusakhulupirira, nadzakhulupiriranso, kenako nkusakhulupiriranso, naonjezera kusakhulupirira, Allah sadzawakhululukira, ndipo sadzawawongolera m’njira (yabwino).
Arapça tefsirler:
بَشِّرِ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ بِأَنَّ لَهُمۡ عَذَابًا أَلِيمًا
Auze achiphamaso kuti adzapeza chilango chowawa.
Arapça tefsirler:
ٱلَّذِينَ يَتَّخِذُونَ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ أَيَبۡتَغُونَ عِندَهُمُ ٱلۡعِزَّةَ فَإِنَّ ٱلۡعِزَّةَ لِلَّهِ جَمِيعٗا
Omwe amaachita osakhulupirira kukhala abwenzi awo kusiya Asilamu. Kodi akufuna kupeza ulemelero kwa iwo? Ndithudi ulemelero wonse ngwa Allah; (suli m’manja mwa anthu).
Arapça tefsirler:
وَقَدۡ نَزَّلَ عَلَيۡكُمۡ فِي ٱلۡكِتَٰبِ أَنۡ إِذَا سَمِعۡتُمۡ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ يُكۡفَرُ بِهَا وَيُسۡتَهۡزَأُ بِهَا فَلَا تَقۡعُدُواْ مَعَهُمۡ حَتَّىٰ يَخُوضُواْ فِي حَدِيثٍ غَيۡرِهِۦٓ إِنَّكُمۡ إِذٗا مِّثۡلُهُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ جَامِعُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡكَٰفِرِينَ فِي جَهَنَّمَ جَمِيعًا
Ndithudi Iye wakuvumbulutsirani m’buku (ili) kuti mukamva ma Ayah (ndime) a Allah akukanidwa ndi kuchitiridwa chipongwe, musakhale pamodzi nawo mpaka alowe m’zokamba zina. (Ngati mutakhala nawo) ndiye kuti mukhala chimodzimodzi ndi iwo. Ndithudi, Allah adzawasonkhanitsa achiphamaso ndi osakhulupirira onse m’moto wa Jahannam.
Arapça tefsirler:
ٱلَّذِينَ يَتَرَبَّصُونَ بِكُمۡ فَإِن كَانَ لَكُمۡ فَتۡحٞ مِّنَ ٱللَّهِ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَكُن مَّعَكُمۡ وَإِن كَانَ لِلۡكَٰفِرِينَ نَصِيبٞ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَسۡتَحۡوِذۡ عَلَيۡكُمۡ وَنَمۡنَعۡكُم مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ فَٱللَّهُ يَحۡكُمُ بَيۡنَكُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۚ وَلَن يَجۡعَلَ ٱللَّهُ لِلۡكَٰفِرِينَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ سَبِيلًا
(A chiphamaso) omwe akukuyembekezerani (kuti mavuto akugwereni), ngati mutapeza kupambana kochokera kwa Allah, amakuuzani: “Kodi sitidali nanu limodzi?” Koma ngati osakhulupirira atapeza gawo (lopambana), amanena (kwa osakhulupirira): “Kodi Sitidayandikire kukugonjetsani pamene tidali m’gulu lankhondo la okhulupirira koma timakutsekerezani kwa okhulupirira?” Koma Allah adzaweruza pakati panu tsiku la chiweruziro. Ndipo Allah sangawaikire njira osakhulupirira pa okhulupirira (kuti awagonjetse kotheratu).
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ يُخَٰدِعُونَ ٱللَّهَ وَهُوَ خَٰدِعُهُمۡ وَإِذَا قَامُوٓاْ إِلَى ٱلصَّلَوٰةِ قَامُواْ كُسَالَىٰ يُرَآءُونَ ٱلنَّاسَ وَلَا يَذۡكُرُونَ ٱللَّهَ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndithu achiphamaso akufuna kunyenga Allah koma Iye awalanga (chifukwa cha chinyengo chawocho). Ndipo akaimilira kupemphera Swala, amaimilira mwaulesi ndikungoonetsa anthu (kuti akupemphera). Ndipo satchula Allah koma pang’ono pokha.
Arapça tefsirler:
مُّذَبۡذَبِينَ بَيۡنَ ذَٰلِكَ لَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِ وَلَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِۚ وَمَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ سَبِيلٗا
Akungoyendayenda pakati pa awa ndi awa (pakati pa Asilamu ndi osakhulupirira). Iwo sali mbali iyi kapena mbali inayo. Ndipo amene Allah wamlekelera kuti asokere sungampezere njira yolungama.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ أَتُرِيدُونَ أَن تَجۡعَلُواْ لِلَّهِ عَلَيۡكُمۡ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينًا
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite osakhulupirira kukhala abwenzi anu kusiya okhulupirira (Asilamu), kodi mukufuna kuti Allah akhale ndi umboni woonekera pa inu (kuti ndinu oyipa?)
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ فِي ٱلدَّرۡكِ ٱلۡأَسۡفَلِ مِنَ ٱلنَّارِ وَلَن تَجِدَ لَهُمۡ نَصِيرًا
Ndithu achiphamaso adzakhala pansi penipeni pa Moto; ndipo sudzampeza mthandizi woimira iwo.
Arapça tefsirler:
إِلَّا ٱلَّذِينَ تَابُواْ وَأَصۡلَحُواْ وَٱعۡتَصَمُواْ بِٱللَّهِ وَأَخۡلَصُواْ دِينَهُمۡ لِلَّهِ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَعَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۖ وَسَوۡفَ يُؤۡتِ ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Kupatula amene alapa (pambuyo pa uchiphamaso wawo); nakonza (makhalidwe awo) nadziphatika kwa Allah; namuyeretseranso Allah chipembedzo chawo. Choncho iwo ali pamodzi ndi okhulupirira. Ndipo Allah adzapatsa okhulupirira malipiro akulu.
Arapça tefsirler:
مَّا يَفۡعَلُ ٱللَّهُ بِعَذَابِكُمۡ إِن شَكَرۡتُمۡ وَءَامَنتُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ شَاكِرًا عَلِيمٗا
Allah sangakulangeni ngati mumthokoze ndi kumkhulupirira. Ndithudi, Allah Ngolandira kuthokoza kwanu, ndiponso Ngodziwa.
Arapça tefsirler:
۞ لَّا يُحِبُّ ٱللَّهُ ٱلۡجَهۡرَ بِٱلسُّوٓءِ مِنَ ٱلۡقَوۡلِ إِلَّا مَن ظُلِمَۚ وَكَانَ ٱللَّهُ سَمِيعًا عَلِيمًا
۞ Allah sakonda kutulutsa mawu ofalitsa kuipa (kwa anthu) kupatula yekhayo wachitiridwa zoipa. Ndipo Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[151]
[151] Indedi, Allah sakonda anthu ofalitsa zoipa za anzawo popanda choipa chilichonse chimene awachitira. Koma munthu amene ena amchitira choipa akumlola kutchula kuipa komwe ena amchitira pokamnenera kwa muweruzi kuti muweruziyo amuthandize pa amene amchitira zoipawo. Koma kulengeza kuipa kwa anthu ena nkosaloledwa m’chisilamu. Ndipo ndi uchimo waukulu.
Arapça tefsirler:
إِن تُبۡدُواْ خَيۡرًا أَوۡ تُخۡفُوهُ أَوۡ تَعۡفُواْ عَن سُوٓءٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَفُوّٗا قَدِيرًا
Ngati mungaonetse chabwino, kapena kuchibisa, kapena kukhululukira zoipa, (zoterozo ndizo zofunika), ndithu Allah Ngokhululuka ndiponso Ngokhoza.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَكۡفُرُونَ بِٱللَّهِ وَرُسُلِهِۦ وَيُرِيدُونَ أَن يُفَرِّقُواْ بَيۡنَ ٱللَّهِ وَرُسُلِهِۦ وَيَقُولُونَ نُؤۡمِنُ بِبَعۡضٖ وَنَكۡفُرُ بِبَعۡضٖ وَيُرِيدُونَ أَن يَتَّخِذُواْ بَيۡنَ ذَٰلِكَ سَبِيلًا
Ndithudi amene sakhulupirira Allah ndi atumiki Ake, ndikumafuna kulekanitsa pakati pa Allah ndi atumiki Ake, ndikumanena kuti: “Ena tikuwakhulupirira, koma ena tikuwakana,” ndikumafunanso kukhonza njira yapakati pa zimenezo,[152]
[152] Aliyense mwa anthu yemwe Allah wamuvomereza kuti ndi mtumiki Wake, ndipo iwe nkukana kumkhulupilira, monga Ayuda mmene amamkanira mneneri Isa (Yesu), ndi Akhrisitu mmene amamkanira mneneri Muhammad (s.a.w), kutereko nkusakhulupilira Allah. Asilamu amavomereza aneneri onse owona amene adadza Muhammad (s.a.w) asadabadwe. Asilamu akuvomereza aneneri onse monga momwe Allah wafotokozera m’Qur’an. Ndipo savomereza omwe Allah sadawavomereze kuti ndi aneneri ake, monga Mirza Gulam Ahmad ndi Bahai. Oterewa ndi amene akunama kuti adapatsidwa uneneri pambuyo pa Mneneri Muhammad (s.a.w). Amene akukhulupilira amenewa ndiye kuti ngopandukira Allah. Tero tichenjere ndi udyerekezi wa Akadiani ndi Abahai ndi ena otere.
Arapça tefsirler:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَٰفِرُونَ حَقّٗاۚ وَأَعۡتَدۡنَا لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا
Iwowo ndiosakhulupirira enieni. Ndipo osakhulupirira tawakonzera chilango choyalutsa.
Arapça tefsirler:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ بِٱللَّهِ وَرُسُلِهِۦ وَلَمۡ يُفَرِّقُواْ بَيۡنَ أَحَدٖ مِّنۡهُمۡ أُوْلَٰٓئِكَ سَوۡفَ يُؤۡتِيهِمۡ أُجُورَهُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Tsopano amene akhulupirira Allah ndi atumiki Ake, napanda kulekanitsa pakati pa aliyense wa iwo (koma nkuwakhulupirira onse), iwo adzawapatsa malipiro awo. Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri, Wachisoni chosatha.
Arapça tefsirler:
يَسۡـَٔلُكَ أَهۡلُ ٱلۡكِتَٰبِ أَن تُنَزِّلَ عَلَيۡهِمۡ كِتَٰبٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِۚ فَقَدۡ سَأَلُواْ مُوسَىٰٓ أَكۡبَرَ مِن ذَٰلِكَ فَقَالُوٓاْ أَرِنَا ٱللَّهَ جَهۡرَةٗ فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلصَّٰعِقَةُ بِظُلۡمِهِمۡۚ ثُمَّ ٱتَّخَذُواْ ٱلۡعِجۡلَ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ فَعَفَوۡنَا عَن ذَٰلِكَۚ وَءَاتَيۡنَا مُوسَىٰ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينٗا
Anthu amene adapatsidwa buku (Ayuda) akukupempha (iwe Mtumiki) kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi, adampemphanso Mûsa zazikulu kuposa zimenezi pomwe adati: “Tiwonetse Allah poyera.” Choncho udawagwira moto wamphenzi chifukwa cha kuipitsa kwao (motowo udachotsa miyoyo yawo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Zitatero Allah adawapatsa moyo kachiwiri). Kenako iwo adapanga thole (mwana wang’ombe monga mulungu wawo) pambuyo powafikira chisonyezo choonekera. Koma tidawakhululukira zimenezo, ndipo tidampatsa Mûsa chisonyezo choonekera poyera.[153]
[153] Ayuda adauza mtumiki Muhammad (s.a.w) kuti sangakhulupirire pokhapokha amuone akukwera kumwamba popanda kugwilira chilichonse ndi kubwera pansi pano buku lili m’manja mwake mutalembedwa umboni wa Allah woti iye Muhammad ndi Mtumiki Wakedi. Ndipo Allah akuti makhalidwe otsutsana ndi aneneri siachilendo kwa Ayuda. Ndipo Musa atalephera kuchita zimenezo adamuda. Tero adapanga fano (lamwana wang’ombe ‘thole’) naliyesa mulungu wawo.
Arapça tefsirler:
وَرَفَعۡنَا فَوۡقَهُمُ ٱلطُّورَ بِمِيثَٰقِهِمۡ وَقُلۡنَا لَهُمُ ٱدۡخُلُواْ ٱلۡبَابَ سُجَّدٗا وَقُلۡنَا لَهُمۡ لَا تَعۡدُواْ فِي ٱلسَّبۡتِ وَأَخَذۡنَا مِنۡهُم مِّيثَٰقًا غَلِيظٗا
Ndipo tidatukula phiri la Al-Tur pamwamba pawo (Ayudawo) polandira pangano lawo; tidati kwa iwo: “Lowani pachipata (cha dziko ili la Sham) mutawerama.” Tidatinso kwa iwo: “Musalumphe malire pa nkhani ya Sabata.” Ndipo tidalandira kwa iwo pangano lokhwima.[154]
[154] (Ndime 154-156) Allah akupitiriza kufotokoza zoipa zawo. Ndipo zina mwa izo ndiizi: (a) Adakana kutsatira malamulo am’Taurat. Ndipo Allah adazula phiri naliimitsa pamwamba pa mitu yawo nawauza kuti: “Ngati simulola kulonjeza kuti mdzatsata zomwe zili m’Taurat, likusinjani phiri ili. (b) Adakana kulowera pachipata kudziko la Shamu (Kenani) monga momwe Allah adawalangizira. Ndipo adalowa monga momwe iwo amafunira. Shamu ndi dziko lomwe Allah adawapatsa kuti akalowemo ndi kukhazikika pambuyo posamuka ku Eguputo (Egypt). Koma iwo sadathokoze chisomochi potsata zomwe Allah adawauza. (c) Pambuyo polowa m’dzikolo adawauza kuti alemekeze tsiku la Sabata kuti likhale tsiku lamapemphero okhaokha. Lisakhale tsiku logwira ntchito. Koma iwo adachitachita ndale zawo mpaka lidasanduka tsiku logwira ntchito. (d) Ena mwa aneneri awo pamene adawaletsa iwo machitidwe amenewa mwaukali adawapha. (e) Mneneri Muhammad pamene adawafotokozera zizindikiro zomwe zinali m’mabuku mwawo zimene zimasonyeza utumiki wake sadamulabadire. Nanena kuti :“Mitima yathu yakutidwa. Siikumvetsa chilichonse chimene ukunena”. (f) Mneneri Isa (Yesu) pamene adawafotokozera za utumiki wake ndi kuwasonyeza zozizwitsa ndi zonse zomwe zidachitika m’kubadwa kwake, iwo adati Mariya adatenga pakati m’njira yachiwerewere pomwe iwo amadziwa kuti akungonama. (g) Adakonza chiwembu kuti aphe Isa (Yesu). Koma Allah adachiononga chiwembu chawocho pomuveka munthu wina nkhope ya Isa (Yesu) amene adali wamkulu wawo yemwe ankafunisitsa kupha Isa (Yesu). Tero adampachika mnzawoyo pamtanda. Pambuyo pake, akuluakulu aChiyuda adazindikira zonse zomwe zidachitikazi. Ndipo adangonyozera ngati kuti sichidachitike chilichonse chododometsa chifukwa choopa kuti anthu angawaukire. M’malomwake ankangodzidzudzula okha m’mtima mwawo.
Arapça tefsirler:
فَبِمَا نَقۡضِهِم مِّيثَٰقَهُمۡ وَكُفۡرِهِم بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ وَقَتۡلِهِمُ ٱلۡأَنۢبِيَآءَ بِغَيۡرِ حَقّٖ وَقَوۡلِهِمۡ قُلُوبُنَا غُلۡفُۢۚ بَلۡ طَبَعَ ٱللَّهُ عَلَيۡهَا بِكُفۡرِهِمۡ فَلَا يُؤۡمِنُونَ إِلَّا قَلِيلٗا
Choncho (tidawalanga) chifukwa chakuswa mapangano awo, ndi kukana kwawo zisonyezo za Allah, ndi kupha kwawo aneneri popanda choonadi, ndi kunena kwawo kwakuti: “Mitima yathu yakutidwa (siingathe kuzindikira zomwe ukunena iwe Muhammad {s.a.w}).” (Ai, Siinakutidwe ndi chilichonse), koma Allah waidinda zidindo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo; tero sakhulupirira koma pang’ono pokha.
Arapça tefsirler:
وَبِكُفۡرِهِمۡ وَقَوۡلِهِمۡ عَلَىٰ مَرۡيَمَ بُهۡتَٰنًا عَظِيمٗا
Chifukwanso cha kusakhulupirira kwawo ndi kumnamizira kwawo Mariya bodza lalikulu (kuti wabala Isa (Yesu) m’njira ya chiwerewere);
Arapça tefsirler:
وَقَوۡلِهِمۡ إِنَّا قَتَلۡنَا ٱلۡمَسِيحَ عِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ رَسُولَ ٱللَّهِ وَمَا قَتَلُوهُ وَمَا صَلَبُوهُ وَلَٰكِن شُبِّهَ لَهُمۡۚ وَإِنَّ ٱلَّذِينَ ٱخۡتَلَفُواْ فِيهِ لَفِي شَكّٖ مِّنۡهُۚ مَا لَهُم بِهِۦ مِنۡ عِلۡمٍ إِلَّا ٱتِّبَاعَ ٱلظَّنِّۚ وَمَا قَتَلُوهُ يَقِينَۢا
Ndikuyankhula kwawo (kwakuti): “Ife tamupha Mesiya Isa (Yesu) mwana wa Mariya, Mtumiki wa Allah; pomwe sadamuphe ndipo sadampachike pa mtanda. Koma adasokonezedwa (ndi munthu wina namuganizira kuti ndi Isa (Yesu). Ndithudi, amene akutsutsana pankhaniyi (Ayuda ndi Akhrisitu) ali m’chikaiko pa iyo; alibe kudziwa kotsimikizika, koma akungotsatira zongoganizira. Ndipo, sadamuphe mosimikiza (kuti ndi iye).
Arapça tefsirler:
بَل رَّفَعَهُ ٱللَّهُ إِلَيۡهِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَزِيزًا حَكِيمٗا
Koma Allah adamkweza kwa Iye ndipo Allah Ndimwini mphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
وَإِن مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ إِلَّا لَيُؤۡمِنَنَّ بِهِۦ قَبۡلَ مَوۡتِهِۦۖ وَيَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ يَكُونُ عَلَيۡهِمۡ شَهِيدٗا
Palibe aliyense mwa anthu omwe adapatsidwa buku (Ayuda ndi Akhrisitu) koma kuti azamkhulupirira iye (Yesu kuti sadali mulungu) imfa yake (Yesuyo) isadadze (izi zizachitika pamene Yesuyo azabwerenso padziko lapansi kumapeto kwa dziko). Nayenso (Yesu) pa siku la chiweruziro adzaikira umboni pa iwo (kuti iye adali chabe kapolo wa Allah).
Arapça tefsirler:
فَبِظُلۡمٖ مِّنَ ٱلَّذِينَ هَادُواْ حَرَّمۡنَا عَلَيۡهِمۡ طَيِّبَٰتٍ أُحِلَّتۡ لَهُمۡ وَبِصَدِّهِمۡ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ كَثِيرٗا
Chifukwa chakuchita kwawo zoipa, awo Ayuda, tidaletsa kwa iwo zinthu zabwino (zakudya) zomwe zidali zovomerezeka kwa iwo; ndiponso chifukwa cha kutsekereza kwawo anthu ambiri kuyenda panjira ya Allah.
Arapça tefsirler:
وَأَخۡذِهِمُ ٱلرِّبَوٰاْ وَقَدۡ نُهُواْ عَنۡهُ وَأَكۡلِهِمۡ أَمۡوَٰلَ ٱلنَّاسِ بِٱلۡبَٰطِلِۚ وَأَعۡتَدۡنَا لِلۡكَٰفِرِينَ مِنۡهُمۡ عَذَابًا أَلِيمٗا
Ndi kudya kwawo riba (katapira) pomwe adaletsedwa kuti asadye; ndiponso chifukwa chakudya kwawo chuma cha anthu mwachinyengo. Ndipo osakhulupirira mwa iwo tawakonzera chilango chopweteka.
Arapça tefsirler:
لَّٰكِنِ ٱلرَّٰسِخُونَ فِي ٱلۡعِلۡمِ مِنۡهُمۡ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ يُؤۡمِنُونَ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ وَمَآ أُنزِلَ مِن قَبۡلِكَۚ وَٱلۡمُقِيمِينَ ٱلصَّلَوٰةَۚ وَٱلۡمُؤۡتُونَ ٱلزَّكَوٰةَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ أُوْلَٰٓئِكَ سَنُؤۡتِيهِمۡ أَجۡرًا عَظِيمًا
Koma mwa iwo amene azama pa maphunziro, ndi okhulupirira (onsewo) akukhulupirira zimene zavumbulutsidwa kwa iwe ndi zimene zidavumbulutsidwa patsogolo pako. Ndipo omwe akupitiriza kupemphera Swala, ndi kupereka Zakaati, ndi kukhulupirira Allah komanso tsiku lachimaliziro, iwo tidzawapatsa malipiro aakulu.
Arapça tefsirler:
۞ إِنَّآ أَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡكَ كَمَآ أَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ نُوحٖ وَٱلنَّبِيِّـۧنَ مِنۢ بَعۡدِهِۦۚ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰٓ إِبۡرَٰهِيمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَ وَٱلۡأَسۡبَاطِ وَعِيسَىٰ وَأَيُّوبَ وَيُونُسَ وَهَٰرُونَ وَسُلَيۡمَٰنَۚ وَءَاتَيۡنَا دَاوُۥدَ زَبُورٗا
Ndithudi, takuvumbulutsira (chivumbulutso) monga momwe tidamuvumbulutsira Nuh (Nowa) ndi aneneri amene anadza pambuyo pake. Ndipo tidamuvumbulutsiranso Ibrahim, Ismail, Ishâq, Ya’qub ndi mbumba yake. Ndipo (tidamuvumbulutsiranso) Isa (Yesu), Ayyub (Yobu), Yunus (Yona), Haarun (Aroni) ndi Sulaiman, ndipo Daud tidampatsa Zabur (Masalimo).
Arapça tefsirler:
وَرُسُلٗا قَدۡ قَصَصۡنَٰهُمۡ عَلَيۡكَ مِن قَبۡلُ وَرُسُلٗا لَّمۡ نَقۡصُصۡهُمۡ عَلَيۡكَۚ وَكَلَّمَ ٱللَّهُ مُوسَىٰ تَكۡلِيمٗا
Ndipo (tidavumbulutsanso chivumbulutso) kwa atumiki omwe takusimbira kale nkhani zawo komanso kwa atumiki ena omwe sitinakusimbire (nkhani zawo); ndipo Allah adayankhula ndi Mûsa mwachindunji.
Arapça tefsirler:
رُّسُلٗا مُّبَشِّرِينَ وَمُنذِرِينَ لِئَلَّا يَكُونَ لِلنَّاسِ عَلَى ٱللَّهِ حُجَّةُۢ بَعۡدَ ٱلرُّسُلِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَزِيزًا حَكِيمٗا
(Iwo ndi) atumiki omwe adauza nkhani zabwino (kwa anthu abwino) ndi kuwachenjeza (oipa) kuti anthu asadzakhale ndi mtsutso pa Allah pambuyo pa (kudza kwa) atumikiwa. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
لَّٰكِنِ ٱللَّهُ يَشۡهَدُ بِمَآ أَنزَلَ إِلَيۡكَۖ أَنزَلَهُۥ بِعِلۡمِهِۦۖ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ يَشۡهَدُونَۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ شَهِيدًا
Koma Allah akuikira umboni zimene wakuvumbulutsira kuti (nzoona), adavumbulutsa mwanzeru Zake. Nawonso angelo akuikira umboni. Ndipo Allah akukwana kukhala mboni.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ قَدۡ ضَلُّواْ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا
Ndithu amene sadakhulupirire, nawatsekereza (anthu) kuyenda pa njira ya Allah, ndithudi asokera; kusokera kwakukulu.
Arapça tefsirler:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَظَلَمُواْ لَمۡ يَكُنِ ٱللَّهُ لِيَغۡفِرَ لَهُمۡ وَلَا لِيَهۡدِيَهُمۡ طَرِيقًا
Ndithudi, amene sadakhulupirire, namachita zoipa, sali Allah owakhululukira iwowo ndi kuwaongolera njira.
Arapça tefsirler:
إِلَّا طَرِيقَ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا
Kupatula njira yomka ku Jahannam, mmenemo akakhala muyaya. Ndipo zimenezo nzopepuka kwa Allah.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ قَدۡ جَآءَكُمُ ٱلرَّسُولُ بِٱلۡحَقِّ مِن رَّبِّكُمۡ فَـَٔامِنُواْ خَيۡرٗا لَّكُمۡۚ وَإِن تَكۡفُرُواْ فَإِنَّ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
E inu anthu! Ndithu Mtumiki wakudzerani ndi choonadi chochokera kwa Mbuye wanu. Choncho khulupirirani; ndi bwino kwa inu kutero. Koma ngati mukana, (dziwani kuti) zonse zakumwamba ndi zapansi nza Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru zakuya.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ لَا تَغۡلُواْ فِي دِينِكُمۡ وَلَا تَقُولُواْ عَلَى ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡحَقَّۚ إِنَّمَا ٱلۡمَسِيحُ عِيسَى ٱبۡنُ مَرۡيَمَ رَسُولُ ٱللَّهِ وَكَلِمَتُهُۥٓ أَلۡقَىٰهَآ إِلَىٰ مَرۡيَمَ وَرُوحٞ مِّنۡهُۖ فَـَٔامِنُواْ بِٱللَّهِ وَرُسُلِهِۦۖ وَلَا تَقُولُواْ ثَلَٰثَةٌۚ ٱنتَهُواْ خَيۡرٗا لَّكُمۡۚ إِنَّمَا ٱللَّهُ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞۖ سُبۡحَٰنَهُۥٓ أَن يَكُونَ لَهُۥ وَلَدٞۘ لَّهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلٗا
E inu anthu a buku! Musamalumphe malire pa chipembedzo chanu. Ndipo musamamnenere Allah koma zowona (zokhazokha). Ndithu Mesiya Isa (Yesu) mwana wa Mariya, ndi mtumiki wa Allah (ndiponso ndi munthu wolengedwa) ndi liwu Lake lomwe adaliyika mwa Mariya ndiponso (ali) ndi mzimu (moyo) wochokera kwa Iye (Allah, monga mizimu ina yonse imachokera kwa Iye). Choncho Khulupirirani Allah ndi atumiki Ake. Musamanene: “Utatu wa Mulungu;” siyani, (zikhululupiliro za utatu wa Mulungu), kutero ndibwino kwa inu. Ndithudi, Allah ndi Mulungu m’modzi (basi). Ulemelero wake ngotukuka kutali ndi kukhala ndi mwana. Nzake zonse za kumwamba ndi pansi. Ndipo Allah ndiMtetezi Wokwanira.
Arapça tefsirler:
لَّن يَسۡتَنكِفَ ٱلۡمَسِيحُ أَن يَكُونَ عَبۡدٗا لِّلَّهِ وَلَا ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ ٱلۡمُقَرَّبُونَۚ وَمَن يَسۡتَنكِفۡ عَنۡ عِبَادَتِهِۦ وَيَسۡتَكۡبِرۡ فَسَيَحۡشُرُهُمۡ إِلَيۡهِ جَمِيعٗا
Mesiya (Mneneri Isa {Yesu}) sangaone kunyozeka kukhala kapolo wa Allah, ngakhalenso angelo oyandikitsidwa (kwa Allah). Ndipo amene angaone kunyozeka pa ukapolo wake kwa Allah nadzitukumula, onse adzawasonkhanitsa kwa Iye (ndipo kenako nkuwalonga kung’anjo ya Moto).
Arapça tefsirler:
فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ فَيُوَفِّيهِمۡ أُجُورَهُمۡ وَيَزِيدُهُم مِّن فَضۡلِهِۦۖ وَأَمَّا ٱلَّذِينَ ٱسۡتَنكَفُواْ وَٱسۡتَكۡبَرُواْ فَيُعَذِّبُهُمۡ عَذَابًا أَلِيمٗا وَلَا يَجِدُونَ لَهُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
Koma amene adamkhulupirira (Yesuyo) ndi kuchita zabwino adzawapatsa malipiro ao mokwanira ndi kuwaonjezera mu zabwino Zake. Koma amene adaona kunyozeka (pokhala kapolo wa Allah) nadzitukumula, adzawalanga chilango chowawa; ndipo sadzapeza bwenzi ngakhale mtetezi kupatula Allah.
Arapça tefsirler:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ قَدۡ جَآءَكُم بُرۡهَٰنٞ مِّن رَّبِّكُمۡ وَأَنزَلۡنَآ إِلَيۡكُمۡ نُورٗا مُّبِينٗا
E inu anthu! Ndithudi, wakudzerani umboni wochokera kwa Mbuye wanu. Ndipo takuvumbulutsirani kuunika koonekera poyera.
Arapça tefsirler:
فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ بِٱللَّهِ وَٱعۡتَصَمُواْ بِهِۦ فَسَيُدۡخِلُهُمۡ فِي رَحۡمَةٖ مِّنۡهُ وَفَضۡلٖ وَيَهۡدِيهِمۡ إِلَيۡهِ صِرَٰطٗا مُّسۡتَقِيمٗا
Tsono amene akhulupirira Allah ndi kudziphatika kwa Iye, iwo adzawalowetsa ku chifundo ndi kuzabwino zochokera kwa Iye, ndikuwatsogolera kwa Iye njira yoongoka.
Arapça tefsirler:
يَسۡتَفۡتُونَكَ قُلِ ٱللَّهُ يُفۡتِيكُمۡ فِي ٱلۡكَلَٰلَةِۚ إِنِ ٱمۡرُؤٌاْ هَلَكَ لَيۡسَ لَهُۥ وَلَدٞ وَلَهُۥٓ أُخۡتٞ فَلَهَا نِصۡفُ مَا تَرَكَۚ وَهُوَ يَرِثُهَآ إِن لَّمۡ يَكُن لَّهَا وَلَدٞۚ فَإِن كَانَتَا ٱثۡنَتَيۡنِ فَلَهُمَا ٱلثُّلُثَانِ مِمَّا تَرَكَۚ وَإِن كَانُوٓاْ إِخۡوَةٗ رِّجَالٗا وَنِسَآءٗ فَلِلذَّكَرِ مِثۡلُ حَظِّ ٱلۡأُنثَيَيۡنِۗ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ لَكُمۡ أَن تَضِلُّواْۗ وَٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمُۢ
Akukufunsa (iwe Mneneri, za malamulo a chuma cha munthu yemwe wafa osasiya mwana kapena kholo). Nena: “Allah akukulamulani pa zayemwe sadasiye mwana ndi kholo (kuti) ngati munthu atamwalira pomwe alibe mwana, koma ali ndi mlongo wake (wa bambo amodzi), choncho (mlongo wakeyo) alandire theka (½) la zomwe wasiya (womwalirayo). Nayenso angalandire chuma (chamlongo wake) ngati alibe mwana. Ndipo ngati iwo ali (alongo) awiri, ndiye kuti adzalandira magawo awiri mmagawo atatu (2/3) a zomwe wasiya. Ndipo ngati ali abale (angapo) amuna ndi akazi, ndiye kuti mwamuna aliyense alandire gawo lolingana ndi la akazi awiri. Umo ndi momwe Allah akukufotokozerani (malamulo Ake) mwatsatanetsatane kuti musasokere. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Sure: Sûratu'n-Nisâ
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat