قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (187) سۈرە: سۈرە بەقەرە
أُحِلَّ لَكُمۡ لَيۡلَةَ ٱلصِّيَامِ ٱلرَّفَثُ إِلَىٰ نِسَآئِكُمۡۚ هُنَّ لِبَاسٞ لَّكُمۡ وَأَنتُمۡ لِبَاسٞ لَّهُنَّۗ عَلِمَ ٱللَّهُ أَنَّكُمۡ كُنتُمۡ تَخۡتَانُونَ أَنفُسَكُمۡ فَتَابَ عَلَيۡكُمۡ وَعَفَا عَنكُمۡۖ فَٱلۡـَٰٔنَ بَٰشِرُوهُنَّ وَٱبۡتَغُواْ مَا كَتَبَ ٱللَّهُ لَكُمۡۚ وَكُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ حَتَّىٰ يَتَبَيَّنَ لَكُمُ ٱلۡخَيۡطُ ٱلۡأَبۡيَضُ مِنَ ٱلۡخَيۡطِ ٱلۡأَسۡوَدِ مِنَ ٱلۡفَجۡرِۖ ثُمَّ أَتِمُّواْ ٱلصِّيَامَ إِلَى ٱلَّيۡلِۚ وَلَا تُبَٰشِرُوهُنَّ وَأَنتُمۡ عَٰكِفُونَ فِي ٱلۡمَسَٰجِدِۗ تِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِ فَلَا تَقۡرَبُوهَاۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ ءَايَٰتِهِۦ لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَّقُونَ
Kwaloledwa kwa inu mu usiku wosala kukumana ndi akazi anu. Iwo ali ngati chovala chanu, inunso muli ngati chovala chawo. Allah wadziwa kuti mudali kudzichitira chinyengo nokha. Choncho walandira kulapa kwanu ndipo wakukhululukirani. Tsopano khudzanani nawo ndipo funani chimene Allah wakulamulirani, ndipo idyani ndi kumwa mpaka udziwike bwinobwino kwa inu ulusi woyera kuchokera ku ulusi wakuda kum’bandakucha (kufikira mudziwe kuti kucha kwalowa, usiku watha). Kenako kwaniritsani kusala mpaka dzuwa litalowa. Ndipo musakhudzane nawo (akazi anu) pamene inu mukuchita mbindikiro m’misikiti. Amenewo ndi malire a Allah; choncho musaayandikire. Motere ndimo Allah akulongosolera mwatsatanetsatane zisonyezo zake kwa anthu kuti akhale oopa Allah (potsatira malamulo ake ndi kusiya zoletsedwa). [22]
[22] Pachiyambi pomwe lamulo la kusala lidakhazikitsidwa adawaletsa anthu kukumana ndi akazi awo usiku pambuyo poti iwo agona tulo ngakhale kuti angogona pang’ono pokha. Kukumana ndi mkazi akumane asanagone. Tero lamuloli lidali lovuta kwambiri kwa iwo kulitsata. Ena a iwo adalakwa pang’ono. Choncho kudalengezedwa kuti: “Tsopano pali chilolezo choti akhoza kuchita chilichonse mpaka m’bandakucha. Ndipo kunena koti: “Funani chimene Allah wakulamulani”, ndikulilimbikitsa lamulo kuchilolezocho. Musati kuti poti kale adakuletsani kukumana ndi akazi anu pambuyo pogona tulo ndiye mupitirize kutero - iyayi. Koma tsatirani chilolezocho.
“Itikafu” ndikuchita chitsimikizo munthu chokhala mu msikiti kwamasiku akutiakuti kapena nthawi yakutiyakuti. Ndipo pempheroli limachitika nthawi zambiri m’mwezi wa Ramadan. Akachita chitsimikizocho (niya) saloledwa kutuluka mu msikitimo pokhapokha patakhala chifukwa chachikulu chotulukira, monga kupita kukadzithandiza.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (187) سۈرە: سۈرە بەقەرە
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش