Check out the new design

قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - شىيشىيۋاچە تەرجىمىسى - خالىد ئىبراھىم بىيتالا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: مائىدە   ئايەت:
يُرِيدُونَ أَن يَخۡرُجُواْ مِنَ ٱلنَّارِ وَمَا هُم بِخَٰرِجِينَ مِنۡهَاۖ وَلَهُمۡ عَذَابٞ مُّقِيمٞ
Adzafuna (mwanjira iliyonse) kuti atuluke ku Moto, koma sadzatulukamo. Ndipo adzakhala ndi chilango chamuyaya.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَٱلسَّارِقُ وَٱلسَّارِقَةُ فَٱقۡطَعُوٓاْ أَيۡدِيَهُمَا جَزَآءَۢ بِمَا كَسَبَا نَكَٰلٗا مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo wakuba wamwamuna ndi wakuba wamkazi, aduleni manja awo; kukhala mphoto ya zomwe achita ndi chilango chochokera kwa Allah. Allah Ngwanyonga zoposa, Ngwanzeru zakuya.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَمَن تَابَ مِنۢ بَعۡدِ ظُلۡمِهِۦ وَأَصۡلَحَ فَإِنَّ ٱللَّهَ يَتُوبُ عَلَيۡهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ
Koma amene walapa pambuyo pakuchita kwake zoipa, namachita zabwino, Allah alandira kulapa kwake. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwabasi Ngwachisoni chosatha.[165]
[165] Taona chifundo cha Allah! Iye akulonjeza wochimwa kuti ngati asiya machimo ake amlandira. Tero munthu asadzione kuti waonongeka kotero kuti Allah sangamlandire. Iyayi! Abwelere ndi mtima wake wonse kwa Allah ndipo Allah amlandira.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
أَلَمۡ تَعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ يُعَذِّبُ مَن يَشَآءُ وَيَغۡفِرُ لِمَن يَشَآءُۗ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Kodi sukudziwa kuti Allah Ngwake ufumu wa kumwamba ndi pansi? amamulanga yemwe wamfuna (akalakwa), ndipo amamukhululukira amene wamfuna. Ndipo Allah Ngokhoza chilichonse.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلرَّسُولُ لَا يَحۡزُنكَ ٱلَّذِينَ يُسَٰرِعُونَ فِي ٱلۡكُفۡرِ مِنَ ٱلَّذِينَ قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِأَفۡوَٰهِهِمۡ وَلَمۡ تُؤۡمِن قُلُوبُهُمۡۛ وَمِنَ ٱلَّذِينَ هَادُواْۛ سَمَّٰعُونَ لِلۡكَذِبِ سَمَّٰعُونَ لِقَوۡمٍ ءَاخَرِينَ لَمۡ يَأۡتُوكَۖ يُحَرِّفُونَ ٱلۡكَلِمَ مِنۢ بَعۡدِ مَوَاضِعِهِۦۖ يَقُولُونَ إِنۡ أُوتِيتُمۡ هَٰذَا فَخُذُوهُ وَإِن لَّمۡ تُؤۡتَوۡهُ فَٱحۡذَرُواْۚ وَمَن يُرِدِ ٱللَّهُ فِتۡنَتَهُۥ فَلَن تَمۡلِكَ لَهُۥ مِنَ ٱللَّهِ شَيۡـًٔاۚ أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ لَمۡ يُرِدِ ٱللَّهُ أَن يُطَهِّرَ قُلُوبَهُمۡۚ لَهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا خِزۡيٞۖ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابٌ عَظِيمٞ
E iwe Mtumiki! Asakudandaulitse amene akuchita changu kukana Allah mwa omwe akunena ndi pakamwa pawo chabe: “Takhulupirira,” pomwe mitima yawo siikukhulupirira. Namonso mwa Ayuda, alipo amene amamvetsera (zimene ukunena) kuti azikanena bodza, amamvetsera mmalo mwa anthu ena amene sadadze kwa iwe (omwe ndi akuluakulu awo), amasintha mawu (a m’buku la Taurat) m’malo mwake, omwenso amanena (kuuza otsatira awo kuti): “Ngati mukapatsidwe (ndi Muhammad {s.a.w}) izi (takuuzanizi), kalandireni, koma ngati musakapatsidwe zimenezi kachenjereni.” Ndipo munthu yemwe Allah akufuna kuti amuyese mayeso sungathe kumpezera chilichonse kwa Allah. Iwowo ndiomwe Allah sadafune kuyeretsa mitima yawo. Apeza kuyaluka pa dziko lapansi. Ndipo tsiku lachimaliziro adzapeza chilango chachikulu.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: مائىدە
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - شىيشىيۋاچە تەرجىمىسى - خالىد ئىبراھىم بىيتالا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

خالىد ئىبراھىم بېيتالا تەرجىمىسى.

تاقاش