Check out the new design

قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - شىيشىيۋاچە تەرجىمىسى - خالىد ئىبراھىم بىيتالا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: ئەئراپ   ئايەت:
وَٱذۡكُرُوٓاْ إِذۡ جَعَلَكُمۡ خُلَفَآءَ مِنۢ بَعۡدِ عَادٖ وَبَوَّأَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ تَتَّخِذُونَ مِن سُهُولِهَا قُصُورٗا وَتَنۡحِتُونَ ٱلۡجِبَالَ بُيُوتٗاۖ فَٱذۡكُرُوٓاْ ءَالَآءَ ٱللَّهِ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo kumbukirani pamene (Allah) adakupangani kukhala amlowammalo pambuyo pa mtundu wa Âdi. Ndipo adakukhazikani pa dziko (mwa ubwino). Mukudzimangira nyumba zikuluzikulu mchigwa, ndiponso kusema ndi kuboola mapiri kukhala nyumba. Choncho kumbukirani mtendere wa Allah, ndipo musaononge pa dziko pofalitsa chisokonezo.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
قَالَ ٱلۡمَلَأُ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ مِن قَوۡمِهِۦ لِلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِمَنۡ ءَامَنَ مِنۡهُمۡ أَتَعۡلَمُونَ أَنَّ صَٰلِحٗا مُّرۡسَلٞ مِّن رَّبِّهِۦۚ قَالُوٓاْ إِنَّا بِمَآ أُرۡسِلَ بِهِۦ مُؤۡمِنُونَ
Adanena akuluakulu omwe adali odzitukumula mwa anthu ake kuuza omwe adaponderezedwa kwa amene adakhulupirira mwa iwo: “Kodi muli ndi chitsimikizo kuti Swalih ngotumizidwa ndi Mbuye Wake (wapatsidwa utumiki)?” (Iwo) Adati: “Ndithu ife tikukhulupirira zomwe watumidwa nazo (kuzifikitsa kwa ife).”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
قَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُوٓاْ إِنَّا بِٱلَّذِيٓ ءَامَنتُم بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Omwe adadzitukumula adati: “Ndithu ife tikuzikana zomwe mwazikhulupirirazo.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَعَقَرُواْ ٱلنَّاقَةَ وَعَتَوۡاْ عَنۡ أَمۡرِ رَبِّهِمۡ وَقَالُواْ يَٰصَٰلِحُ ٱئۡتِنَا بِمَا تَعِدُنَآ إِن كُنتَ مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Choncho adaipha (adaizinga) ngamira ndi kunyoza lamulo la Mbuye wawo, nati: “E iwe Swaleh! Tibweletsere (chilango) chimene wakhala ukutilonjeza ngati ulidi mmodzi wa otumidwa.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلرَّجۡفَةُ فَأَصۡبَحُواْ فِي دَارِهِمۡ جَٰثِمِينَ
Choncho, chivomerezi chidawagwira mwadzidzidzi, adapezeka ali akufa chigwadire m’nyumba zawo.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
فَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰقَوۡمِ لَقَدۡ أَبۡلَغۡتُكُمۡ رِسَالَةَ رَبِّي وَنَصَحۡتُ لَكُمۡ وَلَٰكِن لَّا تُحِبُّونَ ٱلنَّٰصِحِينَ
Tero, Swalih adawasiya (nkupita kwina kwake) uku akunena: “E anthu anga! Ndidafikitsadi uthenga wa Mbuye wanga kwa inu. Ndipo Ndidakuchenjezani ndi kukulangizani. Koma inu simufuna alangizi.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
وَلُوطًا إِذۡ قَالَ لِقَوۡمِهِۦٓ أَتَأۡتُونَ ٱلۡفَٰحِشَةَ مَا سَبَقَكُم بِهَا مِنۡ أَحَدٖ مِّنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Nayenso Luti (tidamtuma, ndipo kumbuka) pamene adati kwa anthu ake: “Kodi mukuchita chonyansa chomwe sadakutsogolereni aliyense kuchichita mwa anthu akale m’zolengedwa zonse?”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
إِنَّكُمۡ لَتَأۡتُونَ ٱلرِّجَالَ شَهۡوَةٗ مِّن دُونِ ٱلنِّسَآءِۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٞ مُّسۡرِفُونَ
“Ndithu inu mukuwadzera amuna mwa chilakolako kusiya akazi! Ndithudi, inu ndinu anthu olumpha malire.”
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى سۈرە: ئەئراپ
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - شىيشىيۋاچە تەرجىمىسى - خالىد ئىبراھىم بىيتالا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

خالىد ئىبراھىم بېيتالا تەرجىمىسى.

تاقاش