قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (37) سۈرە: سۈرە تەۋبە
إِنَّمَا ٱلنَّسِيٓءُ زِيَادَةٞ فِي ٱلۡكُفۡرِۖ يُضَلُّ بِهِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُحِلُّونَهُۥ عَامٗا وَيُحَرِّمُونَهُۥ عَامٗا لِّيُوَاطِـُٔواْ عِدَّةَ مَا حَرَّمَ ٱللَّهُ فَيُحِلُّواْ مَا حَرَّمَ ٱللَّهُۚ زُيِّنَ لَهُمۡ سُوٓءُ أَعۡمَٰلِهِمۡۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndithu kutalikitsa ndi kuchedwetsa (mwezi wopatulika kuti usafike mwamsanga), kumaonjezera kusakhulupirira (mwa Allah), zoterozo akusokerezedwa nazo amene sadakhulupirire. Chaka china amauyesa wosapatulika pomwe chaka china amauyesa wopatulika ndi cholinga chokwaniritsa chiwerengero cholingana ndi miyezi yomwe Allah adaipatula kukhala yopatulika. Choncho, chimene Allah adaletsa, amachiyesa chololedwa. Zakometsedwa kwa iwo zochita zawo zoipa. Ndipo Allah sawatsogolera anthu osakhulupirira.[209]
[209] Kuichedwetsa miyezi yopatulika, kapena ina mwa iyo ndi kuichotsa mu mndondomeko wake umene Allah adaiika monga momwe ankachitira anthu am’nyengo ya umbuli, kumawaonjezera kusakhulupilira anthu osakhulupilira mwa Allah. Arabu m’nyengo ya umbuli amauyesa mwezi wopatulika kukhala wosapatulika akafuna kuti achite nkhondo m’mweziwo. Ndipo mwezi wosapatulika amauyesa wopatulika ncholinga choti akwaniritse chiwerengero cha miyezi yopatulika yomwe Allah adaipatula. Zonsezi zimachitika pofuna kukwaniritsa zilakolako zawo zoipa.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (37) سۈرە: سۈرە تەۋبە
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش