የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (12) ምዕራፍ: ሱረቱ ሁድ
فَلَعَلَّكَ تَارِكُۢ بَعۡضَ مَا يُوحَىٰٓ إِلَيۡكَ وَضَآئِقُۢ بِهِۦ صَدۡرُكَ أَن يَقُولُواْ لَوۡلَآ أُنزِلَ عَلَيۡهِ كَنزٌ أَوۡ جَآءَ مَعَهُۥ مَلَكٌۚ إِنَّمَآ أَنتَ نَذِيرٞۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ وَكِيلٌ
Mwina usiya zina mwa zomwe zikuvumbulutsidwa kwa iwe ndikubanika nazo mchifuwa mwako chifukwa chakuti akunena: “Bwanji sizidatsitsidwe kwa iye nkhokwe za chuma kapena bwanji mngelo osadza pamodzi ndi iye?” Koma ndithu iwe ndiwe mchenjezi basi ndipo Allah ndiye muyang’aniri wa chinthu chilichonse.[221]
[221] Ophatikiza Allah ndi zina zake adali kupereka maganizo kwa Mtumiki akuti ampemphe Allah kuti adzetse milumilu ya chuma kapena amutumizire angelo kuti aziyenda naye limodzi. Ndipo adalinso kumaichitira Qur’an chibwana Mtumiki akawawerengera. Potero Mtumiki (s.a.w) adali kubanika mu mtima mwake akafuna kufikitsa uthenga kwa iwo chifukwa chakuopa kutsutsidwa ndi kumchitira chibwana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (12) ምዕራፍ: ሱረቱ ሁድ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት