የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (5) ምዕራፍ: ሱረቱ አል ፈለቅ
وَمِن شَرِّ حَاسِدٍ إِذَا حَسَدَ
Ndiponso ku zoipa za wansanje pamene akuchita nsanje.”[502]
[502] “Wanjiru” kapena “Wansanje” uyu ndi munthu amene amanyansidwa akamuona mnzake atadalitsidwa ndi dalitso la mtundu uliwonse. Ndipo amakhumba kuti dalitsolo limuchokere ngakhale kuti lisamufikire iye. Njiru ndi tchimo lalikulu ndiponso ndi nthenda yoipa kwambiri. Mwina munthu wanjiru amabisa njiru yake mu mtima mpaka kufa nayo. Apo amapuma iye pamodzi ndi anthu aja amene ankawachitira njiru. Mwina amalephera kuibisa mu mtima ndipo amaionetsera poyera kotero kuti amachita zotheka kuti amuchotsere mnzake uja dalitso lomwe wapatsidwa ndi Allah. Akalephera izi, amangoganiza za kumupha; njiru iyi ndi yoipa kwambiri.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (5) ምዕራፍ: ሱረቱ አል ፈለቅ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት