የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (33) ምዕራፍ: ሱረቱ አል-ማኢዳህ
إِنَّمَا جَزَٰٓؤُاْ ٱلَّذِينَ يُحَارِبُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَيَسۡعَوۡنَ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَسَادًا أَن يُقَتَّلُوٓاْ أَوۡ يُصَلَّبُوٓاْ أَوۡ تُقَطَّعَ أَيۡدِيهِمۡ وَأَرۡجُلُهُم مِّنۡ خِلَٰفٍ أَوۡ يُنفَوۡاْ مِنَ ٱلۡأَرۡضِۚ ذَٰلِكَ لَهُمۡ خِزۡيٞ فِي ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابٌ عَظِيمٌ
Ndithu mphoto ya amene akulimbana ndi Allah ndi Mtumiki Wake (pochita zomwe waletsa) ndi kudzetsa chionongeko pa dziko, aphedwe kapena apachikidwe pa mtanda, kapena adulidwe manja awo ndi miyendo yawo mosemphanitsa (dzanja lakumanja ndi phazi lakumanzere, ndipo dzanja lakumanzere ndi phazi lakumanja); kapena apirikitsidwe mdzikomo. Uku ndikuyaluka kwawo pa dziko lapansi. Ndipo iwo pa tsiku lachimaliziro adzalandira chilango chachikulu.[164]
[164] Apa atchula chilango chowapatsa anthu owononga, amene amafwamba anthu m’njira zawo. Anthu otere alandire zilango izi:- (a) Ngati akungopha oyenda m’njiramo popanda kuwatengera chuma chawo akawapha, iwo akagwidwa chiweruzo chawo nkuphedwa nawonso. (b) Ngati akupha ndi kulanda chuma, atagwidwa chiweruzo chawo nkuphedwa. Ndipo akaphedwa choncho awapachike pa mtanda kwamasiku atatu asanawaike m’manda. Kapena choyamba awaweruze kuti apachikidwe ali moyo. Ndipo akatsala pang’ono kufa, awatsitse ndi kuwamaliza. (c) Ngati amangolanda chuma chokha popanda kupha, akagwidwa chiweruzo chawo nkuti adulidwe dzanja lakudzanjadzanja aliyense ndi phazi lakumanzere. Kapena dzanja lamanzere ndi phazi ladzanjadzanja (d) Ngati saapha ndiponso salanda chuma, koma amangovutitsa anthu ndi kuwaopseza, chiweruzo chawo nkuwachotsa m’dzikomo kuwapititsa kwina nkuwapatsa ukaidi kumeneko, kapena kuwanjata m’dziko momwemo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (33) ምዕራፍ: ሱረቱ አል-ማኢዳህ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት