Check out the new design

የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አት ተህሪም   አንቀጽ:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ تُوبُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِ تَوۡبَةٗ نَّصُوحًا عَسَىٰ رَبُّكُمۡ أَن يُكَفِّرَ عَنكُمۡ سَيِّـَٔاتِكُمۡ وَيُدۡخِلَكُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ يَوۡمَ لَا يُخۡزِي ٱللَّهُ ٱلنَّبِيَّ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَهُۥۖ نُورُهُمۡ يَسۡعَىٰ بَيۡنَ أَيۡدِيهِمۡ وَبِأَيۡمَٰنِهِمۡ يَقُولُونَ رَبَّنَآ أَتۡمِمۡ لَنَا نُورَنَا وَٱغۡفِرۡ لَنَآۖ إِنَّكَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
E inu amene mwakhulupirira! Lapani kwa Allah; kulapa koona; ndithu Mbuye wanu akufafanizirani zoipa zanu ndi kukakulowetsani m’minda momwe mitsinje ikuyenda pansi pake, tsiku limene Allah sadzayalutsa mneneli ndi amene adakhulupirira pamodzi naye. Dangalira lawo lidzayenda chapatsogolo pawo ndi mbali yakumanja kwawo, uku akunena: “Mbuye wathu! Tikwanitsireni dangalira lathu (mpaka likatifikitse ku Munda wamtendere), ndiponso tikhululukireni ndithu Inu ndi Wokhoza chilichonse.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ جَٰهِدِ ٱلۡكُفَّارَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱغۡلُظۡ عَلَيۡهِمۡۚ وَمَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
E iwe Mneneri! Limbana ndi akafiri (osakhulupirira) ndi Amunafikina (Achiphamaso), aumire mtima. Ndipo malo awo ndi ku Jahannam, taonani kuipa kobwerera (kwawo)!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ضَرَبَ ٱللَّهُ مَثَلٗا لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱمۡرَأَتَ نُوحٖ وَٱمۡرَأَتَ لُوطٖۖ كَانَتَا تَحۡتَ عَبۡدَيۡنِ مِنۡ عِبَادِنَا صَٰلِحَيۡنِ فَخَانَتَاهُمَا فَلَمۡ يُغۡنِيَا عَنۡهُمَا مِنَ ٱللَّهِ شَيۡـٔٗا وَقِيلَ ٱدۡخُلَا ٱلنَّارَ مَعَ ٱلدَّٰخِلِينَ
Allah wapereka fanizo la osakhulupirira monga mkazi wa Nuh ndi mkazi wa Luti. Awiriwa adali pansi pa akapolo Athu awiri abwino, koma adali osakhulupirika kwa amuna awo, (ndipo amuna awo) sadawateteze kalikonse ku chilango cha Allah, ndipo kudanenedwa kwa iwo “Lowani ku Moto pamodzi (ndi ena) olowa.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَضَرَبَ ٱللَّهُ مَثَلٗا لِّلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱمۡرَأَتَ فِرۡعَوۡنَ إِذۡ قَالَتۡ رَبِّ ٱبۡنِ لِي عِندَكَ بَيۡتٗا فِي ٱلۡجَنَّةِ وَنَجِّنِي مِن فِرۡعَوۡنَ وَعَمَلِهِۦ وَنَجِّنِي مِنَ ٱلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndiponso Allah wapereka fanizo la amene akhulupirira monga mkazi wa Firiauna (Farawo) pamene adanena: “Mbuye wanga! Ndimangireni kwa inu Nyumba mu Jannah, ndipo ndipulumutseni kwa Firiauna ndi zochita zake, ndiponso ndipulumutseni kwa anthu oipa (ndi amtopola.)”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَرۡيَمَ ٱبۡنَتَ عِمۡرَٰنَ ٱلَّتِيٓ أَحۡصَنَتۡ فَرۡجَهَا فَنَفَخۡنَا فِيهِ مِن رُّوحِنَا وَصَدَّقَتۡ بِكَلِمَٰتِ رَبِّهَا وَكُتُبِهِۦ وَكَانَتۡ مِنَ ٱلۡقَٰنِتِينَ
Ndi (fanizo lina la wokhulupirira monga) Mariya mwana wa Imran amene adasunga umaliseche wake; ndipo tidauzira mmenemo Mzimu Wathu ndipo adavomereza mawu a Mbuye wake (omwe adali zolamula Zake ndi zoletsa Zake) ndi mabuku Ake (amene adavumbulutsidwa kwa Aneneri Ake); ndipo adali mmodzi wa opitiriza kudzichepetsa (ndi kumvera Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አት ተህሪም
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ - የትርጉሞች ማዉጫ

ተርጓሙ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ።

መዝጋት