Check out the new design

የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አት-ተውባህ   አንቀጽ:
كَيۡفَ يَكُونُ لِلۡمُشۡرِكِينَ عَهۡدٌ عِندَ ٱللَّهِ وَعِندَ رَسُولِهِۦٓ إِلَّا ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّمۡ عِندَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۖ فَمَا ٱسۡتَقَٰمُواْ لَكُمۡ فَٱسۡتَقِيمُواْ لَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُتَّقِينَ
Chingakhalepo bwanji chipangano pakati pa Amushirikina (oswa mapangano nthawi ndi nthawi) ndi Allah ndi Mthenga Wake, kupatula okhawo amene mudapangana nawo mapangano pa Msikiti Wopatulika? (Amene adakwaniritsa mapangano awo). Ngati iwo akupitiriza kulungama (posunga mapanganowo) kwa inu, nanunso pitirizani kulungama kwa iwo. Ndithu Allah akukonda amene akumuopa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كَيۡفَ وَإِن يَظۡهَرُواْ عَلَيۡكُمۡ لَا يَرۡقُبُواْ فِيكُمۡ إِلّٗا وَلَا ذِمَّةٗۚ يُرۡضُونَكُم بِأَفۡوَٰهِهِمۡ وَتَأۡبَىٰ قُلُوبُهُمۡ وَأَكۡثَرُهُمۡ فَٰسِقُونَ
(Kodi inu ndiye osunga malonjezo?) Bwanji? Pomwe iwo akakhala ndi mphamvu pa inu sakusungirani chibale kapena pangano? Amakusangalatsani ndi pakamwa pawo pomwe mitima yawo ikukana (kukukondani). Ndipo ambiri a iwo ngoukira malamulo (a Allah).[205]
[205] Allah akuti kodi mungapangane nawo mapangano anthu oti akapeza mwawi wokugonjetsani inu sasunga chibale chomwe chidali pakati panu ngakhale pangano? Iwo amakunenerani mawu otsekemera ngati uchi pomwe mitima yawo ndi yodzadzidwa ndi mkwiyo ndi inu.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ٱشۡتَرَوۡاْ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ ثَمَنٗا قَلِيلٗا فَصَدُّواْ عَن سَبِيلِهِۦٓۚ إِنَّهُمۡ سَآءَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Asinthanitsa Ayah za Allah (ndi zinthu za dziko lapansi) ndi mtengo wochepa, ndipo atsekereza (anthu) kunjira Yake. Ndithu nzoipa kwabasi zomwe iwo akhala akuchita.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَا يَرۡقُبُونَ فِي مُؤۡمِنٍ إِلّٗا وَلَا ذِمَّةٗۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُعۡتَدُونَ
Sasunga chibale pa okhulupirira ngakhale pangano. Awo ndiwo opyola malire.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِن تَابُواْ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَوُاْ ٱلزَّكَوٰةَ فَإِخۡوَٰنُكُمۡ فِي ٱلدِّينِۗ وَنُفَصِّلُ ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
Koma ngati alapa nayamba kupemphera Swala ndikupereka chopereka (Zakaat), ndiye kuti ndi abale anu pa chipembedzo. Ndipo tikuzifotokoza Ayah zi (mwabwino) kwa anthu odziwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِن نَّكَثُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُم مِّنۢ بَعۡدِ عَهۡدِهِمۡ وَطَعَنُواْ فِي دِينِكُمۡ فَقَٰتِلُوٓاْ أَئِمَّةَ ٱلۡكُفۡرِ إِنَّهُمۡ لَآ أَيۡمَٰنَ لَهُمۡ لَعَلَّهُمۡ يَنتَهُونَ
Ndipo ngati aswa malumbiro awo pambuyo pomanga chipangano chawo, ndi kuyamba kutukwana chipembedzo chanu, menyanani nawo atsogoleri a kusakhulupirira. Ndithu iwo alibe mapangano, (sasunga mapangano. Menyanani nawo) kuti iwo aleke (machitidwe awo oipa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَلَا تُقَٰتِلُونَ قَوۡمٗا نَّكَثُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُمۡ وَهَمُّواْ بِإِخۡرَاجِ ٱلرَّسُولِ وَهُم بَدَءُوكُمۡ أَوَّلَ مَرَّةٍۚ أَتَخۡشَوۡنَهُمۡۚ فَٱللَّهُ أَحَقُّ أَن تَخۡشَوۡهُ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Kodi nchotani kuti musamenyane nawo anthu omwe aswa malonjezo awo, natsimikiza kumtulutsa (kumpirikitsa mu mzinda wa Makka, kapena kumupha) Mtumiki? Iwo ndi amene adayamba kukuputani pachiyambi, nanga mukuwaopa chotani? Allah ndiye wofunika kumuopa, ngati inu mulidi okhulupirira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አት-ተውባህ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ - የትርጉሞች ማዉጫ

በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ ተተረጎመ

መዝጋት