للإطلاع على الموقع بحلته الجديدة

ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: الرعد   آية:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ طُوبَىٰ لَهُمۡ وَحُسۡنُ مَـَٔابٖ
Amene akhulupirira ndi kumachita zabwino, chisangalalo nchawo ndi mabwelero abwino.
التفاسير العربية:
كَذَٰلِكَ أَرۡسَلۡنَٰكَ فِيٓ أُمَّةٖ قَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِهَآ أُمَمٞ لِّتَتۡلُوَاْ عَلَيۡهِمُ ٱلَّذِيٓ أَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡكَ وَهُمۡ يَكۡفُرُونَ بِٱلرَّحۡمَٰنِۚ قُلۡ هُوَ رَبِّي لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ عَلَيۡهِ تَوَكَّلۡتُ وَإِلَيۡهِ مَتَابِ
Momwemo takutuma kwa anthu omwe adapita patsogolo pawo anthu ena (ndipo amva nkhani zawo zonse); kuti uwawerengere zimene tikukuvumbulutsira; koma iwo akumkana (Allah) Wachifundo chambiri. Nena: “Iyeyo ndi Mbuye wanga! Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye; ndatsamira kwa Iye, ndipo kobwerera kwanga nkwa Iye basi.”
التفاسير العربية:
وَلَوۡ أَنَّ قُرۡءَانٗا سُيِّرَتۡ بِهِ ٱلۡجِبَالُ أَوۡ قُطِّعَتۡ بِهِ ٱلۡأَرۡضُ أَوۡ كُلِّمَ بِهِ ٱلۡمَوۡتَىٰۗ بَل لِّلَّهِ ٱلۡأَمۡرُ جَمِيعًاۗ أَفَلَمۡ يَاْيۡـَٔسِ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَن لَّوۡ يَشَآءُ ٱللَّهُ لَهَدَى ٱلنَّاسَ جَمِيعٗاۗ وَلَا يَزَالُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ تُصِيبُهُم بِمَا صَنَعُواْ قَارِعَةٌ أَوۡ تَحُلُّ قَرِيبٗا مِّن دَارِهِمۡ حَتَّىٰ يَأۡتِيَ وَعۡدُ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُخۡلِفُ ٱلۡمِيعَادَ
Ndipo ikadakhalapo Qur’an yomwe chifukwa cha iyo mapiri akadayendetsedwa (panthawi yoiwerenga), kapena chifukwa cha iyo, nthaka ikadang’ambidwa, kapena chifukwa cha iyo, akufa akadayankhulitsidwa, (yochititsa zimenezi ikadakhala Qur’an iyi. Koma ntchito ya Qur’an siimeneyo)! Zinthu zonse nza Allah. Kodi sadadziwebe amene akhulupirira, kuti Allah akadafuna akadawaongolera anthu onse (ku Chisilamu; akadawalenga monga angelo opanda zilakolako, koma wawapatsa nzeru ndi zilakolako kuti alimbane ndi ziwirizi; ena apambane ndi kulowa ku Munda wamtendere). Ndipo tsoka silisiya kuwapeza amene sadakhulupirire chifukwa cha zomwe achita, kapena litsika pafupi ndi dziko lawo kufikira lonjezo la Allah lifike (lowachotsa moyo), ndithudi, Allah saswa malonjezo (Ake).
التفاسير العربية:
وَلَقَدِ ٱسۡتُهۡزِئَ بِرُسُلٖ مِّن قَبۡلِكَ فَأَمۡلَيۡتُ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ ثُمَّ أَخَذۡتُهُمۡۖ فَكَيۡفَ كَانَ عِقَابِ
Ndipo ndithu adachitidwa chipongwe atumiki akale iwe usanadze koma ndidawalekelera amene sadakhulupirire (sindidawalange mwachangu), ndipo kenako ndidawalanga. Kodi chilango changa chidali chotani!
التفاسير العربية:
أَفَمَنۡ هُوَ قَآئِمٌ عَلَىٰ كُلِّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡۗ وَجَعَلُواْ لِلَّهِ شُرَكَآءَ قُلۡ سَمُّوهُمۡۚ أَمۡ تُنَبِّـُٔونَهُۥ بِمَا لَا يَعۡلَمُ فِي ٱلۡأَرۡضِ أَم بِظَٰهِرٖ مِّنَ ٱلۡقَوۡلِۗ بَلۡ زُيِّنَ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ مَكۡرُهُمۡ وَصُدُّواْ عَنِ ٱلسَّبِيلِۗ وَمَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَمَا لَهُۥ مِنۡ هَادٖ
Kodi amene akuimilira mzimu uliwonse pa zimene udapeza (kuti adzaulipire, sindiye woyenera kupembedzedwa)? Ndipo ampangira Allah anzake. Nena: “Atchuleni (anzakewo).” Kodi kapena mukumuuza zomwe sakuzidziwa pa dziko, kapena (zomwe mukunenazo) ndimawu chabe (opanda cholinga chilichonse)? Koma amene sadakhulupirire akometsedwa ndi bodza lawoli lamkunkhuniza, ndipo atsekerezedwa kunjira (ya choonadi). Ndipo amene Allah wamulekelera kusokera alibe muongoli (wina womuongolera).
التفاسير العربية:
لَّهُمۡ عَذَابٞ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَعَذَابُ ٱلۡأٓخِرَةِ أَشَقُّۖ وَمَا لَهُم مِّنَ ٱللَّهِ مِن وَاقٖ
Ali nacho chilango m’moyo wa dziko lapansi, koma chilango chapambuyo pa imfa nchokhwima zedi; ndipo sadzakhala ndi mtetezi kwa Allah.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: الرعد
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا - فهرس التراجم

ترجمها خالد إبراهيم بيتالا.

إغلاق