ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (178) سورة: البقرة
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُتِبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡقِصَاصُ فِي ٱلۡقَتۡلَىۖ ٱلۡحُرُّ بِٱلۡحُرِّ وَٱلۡعَبۡدُ بِٱلۡعَبۡدِ وَٱلۡأُنثَىٰ بِٱلۡأُنثَىٰۚ فَمَنۡ عُفِيَ لَهُۥ مِنۡ أَخِيهِ شَيۡءٞ فَٱتِّبَاعُۢ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَأَدَآءٌ إِلَيۡهِ بِإِحۡسَٰنٖۗ ذَٰلِكَ تَخۡفِيفٞ مِّن رَّبِّكُمۡ وَرَحۡمَةٞۗ فَمَنِ ٱعۡتَدَىٰ بَعۡدَ ذَٰلِكَ فَلَهُۥ عَذَابٌ أَلِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Kwalamulidwa kwa inu Qiswas (kubwezerana) molingana kwa ophedwa; mfulu kwa mfulu, kapolo kwa kapolo, mkazi kwa mkazi. Koma amene wakhululukidwa ndi m’bale wakeyo pa chinthu Chilichonse, atsatire ndi kulonjelera dipolo mwaubwino. (Nayenso wolipa) apereke kwa iye mwa ubwino. Kumeneko ndikufewetsa kumene kwachokera kwa Mbuye wanu, ndiponso chifundo. Ndipo amene alumphe malire pambuyo pa izi, iye adzapeza chilango chopweteka.[15]
[15] Apa akunena kuti, “mfulu kwa mfulu” kuthanthauza kuti aliyense amene wapha nayenso aphedwe. Sikuti aphe munthu wina m’malo mwake.
Chisilamu chisanadze kudali kuponderezana zedi. Mfulu yochokera kufuko la pamwamba, ngati atapha mfulu yafuko la pansi eni a wakuphayo adali kukana kumpereka kuti aphedwe. M’malo mwake amapereka kapolo kuti ndiye aphedwe m’malo mwake. Kapolo wa mfulu wa fuko lapamwamba akapha kapolo wa mfulu wa fuko lapansi sadali kumpereka kuti akaphedwe. Amati: “Kapolo wathuyo ngwapamwamba pomwe wanuyo ngonyozeka. Choncho palibe kufanana pakati pa awiriwa.” Ndipo ngati zitachitika motere kuti kapolo wa onyozeka nkupha kapolo wa odzitukumula, odzitukumulawa amakana kupha kapolo uja m’malo mwake amafuna mfulu yochokera kufuko lonyozekalo. Tero Qur’ani idaletsa machitidwe oterewa. Anthu onse ngofanana, palibe kusiyana pakati pawo. Amene wapha aphedwe yemweyo osati wina, ngakhale atakhala mfulu kapena kapolo. Ili ndilo tanthauzo la Ayah (ndime) imeneyi.
Tsono gawo lina limene likuti: “Koma amene wakhululukidwa ndi m’bale wakeyo...” tanthauzo lake nkuti amene wamphera m’bale wake akamkhululukira wakuphayo amlipiritse dipo la ndalama. Tero apa akumuuza iyeyo kuti ngati atamkhululukira m’bale wakeyo nangomulipiritsa ndalama, alonjelere dipolo mwa ubwino. Nayenso wolipayo apereke mwa ubwino. Asachedwetse mwadala namzunguzazunguza. Tsono gawo lachitatu landime yokhayokhayi likutiuza za chifundo chimene Allah watichitira potilekera ife eni kusankha chiweruzo pankhaniyi.
Munthu yemwe amphera m’bale wake akhoza kuchita izi:
a) Kuliuza boma kuti liphenso yemwe adapha m’bale wakeyo.
b) Kapena kumlipiritsa dipo.
c) Kapena kumkhululukira popanda kulipa chilichonse. Ndipo gawo lomaliza landimeyi akumchenjeza wokhululukayo kuti asangomkhululukira munthuyo pamaso pa anthu kenako nkumuchita chiwembu mobisa.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (178) سورة: البقرة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق