ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (37) سورة: الأحزاب
وَإِذۡ تَقُولُ لِلَّذِيٓ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِ وَأَنۡعَمۡتَ عَلَيۡهِ أَمۡسِكۡ عَلَيۡكَ زَوۡجَكَ وَٱتَّقِ ٱللَّهَ وَتُخۡفِي فِي نَفۡسِكَ مَا ٱللَّهُ مُبۡدِيهِ وَتَخۡشَى ٱلنَّاسَ وَٱللَّهُ أَحَقُّ أَن تَخۡشَىٰهُۖ فَلَمَّا قَضَىٰ زَيۡدٞ مِّنۡهَا وَطَرٗا زَوَّجۡنَٰكَهَا لِكَيۡ لَا يَكُونَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ حَرَجٞ فِيٓ أَزۡوَٰجِ أَدۡعِيَآئِهِمۡ إِذَا قَضَوۡاْ مِنۡهُنَّ وَطَرٗاۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ مَفۡعُولٗا
Ndipo (kumbuka) pamene udamuuza yemwe Allah adampatsa mtendere (pomuongolera ku Chisilamu, ndipo) iwenso udampatsa mtendere (pomulera ndi kumpatsa ufulu, yemwe ndi Zaid Bun Haritha, udati kwa iye): “Gwirizana ndi mkazi wako, ndipo wopa Allah.” Ukubisa mu mtima mwako chimene Allah afuna kuchisonyeza poyera (chomwe ndi kuti Allah akulamula kumkwatira mkazi ameneyo akamuleka Zaid Bun Haritha kuti chichoke chizolowezi choti mwana wongomulera chabe nkumuyesa mwana wako weniweni). Ndipo ukuopa anthu (kuti akudzudzula pa zimenezo), pomwe woyenera kumuopa ndi Allah. Choncho pamene Zaid adamaliza chilakolako chake pa mkazi ameneyo, tidakukwatitsa iwe kuti pasakhale masautso pa okhulupirira pokwatira akazi a ana awo akungowalera chabe ngati (anawo) atamaliza zilakolako zawo pa akaziwo, ndipo lamulo la Allah ndilochitika, (palibe chingalepheretse kuti lisachitike).[324]
[324] Polamula chinthu kuti chichitike kapena chisachitike, pafunika kuti iwe wolamula ukhale woyamba kutsata malamulowo. Ngati sutero, ndiye kuti malamulo akowo sangakhale ndi mphamvu. Mu ndime iyi muli chilolezo chomukwatira mkazi yemwe wasiyidwa ukwati ndi mwana yemwe adangoleredwa chabe ndi munthu amene amatcha mwanayo kuti ndi mwana wake chifukwa chomulera. Kalelo zoterezi sizimaloledwa. Choncho Mtumiki (s.a.w) adauzidwa kuti achite iye mwini zimenezi pofuna kuthetsa chikhalidwecho.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (37) سورة: الأحزاب
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق