ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (102) سورة: النساء
وَإِذَا كُنتَ فِيهِمۡ فَأَقَمۡتَ لَهُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَلۡتَقُمۡ طَآئِفَةٞ مِّنۡهُم مَّعَكَ وَلۡيَأۡخُذُوٓاْ أَسۡلِحَتَهُمۡۖ فَإِذَا سَجَدُواْ فَلۡيَكُونُواْ مِن وَرَآئِكُمۡ وَلۡتَأۡتِ طَآئِفَةٌ أُخۡرَىٰ لَمۡ يُصَلُّواْ فَلۡيُصَلُّواْ مَعَكَ وَلۡيَأۡخُذُواْ حِذۡرَهُمۡ وَأَسۡلِحَتَهُمۡۗ وَدَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَوۡ تَغۡفُلُونَ عَنۡ أَسۡلِحَتِكُمۡ وَأَمۡتِعَتِكُمۡ فَيَمِيلُونَ عَلَيۡكُم مَّيۡلَةٗ وَٰحِدَةٗۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن كَانَ بِكُمۡ أَذٗى مِّن مَّطَرٍ أَوۡ كُنتُم مَّرۡضَىٰٓ أَن تَضَعُوٓاْ أَسۡلِحَتَكُمۡۖ وَخُذُواْ حِذۡرَكُمۡۗ إِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٗا مُّهِينٗا
Ndipo ngati uli pamodzi (ndi Asilamu pankhondo) ndikuwatsogolera Swala, ndiye kuti gulu limodzi la iwo liimilire pamodzi ndi iwe ndikupemphera uku atagwirizira zida zawo. Ndipo akamaliza kulambira kwawo, apite kumbuyo kwanu (kuti akulondereni) ndipo lidze gulu lina lomwe silidapemphere, lipemphere nawe pamodzi; nawonso achenjere ndikugwirizira zida zawo (nkupemphera), chifukwa chakuti omwe sadakhulupirire akufuna kuti mutanyalanyaza zida zanu ndi katundu wanu angokuukirani nthawi imodzi. Koma sikulakwa kwa inu mutaika pansi zida zanu chifukwa chakuvutitsidwa ndi mvula kapena ngati mukudwala. Koma chenjeranaoni. Ndithudi Allah wawakonzera chilango choyalutsa osakhulupirira.[139]
[139] Swala yopemphera pagulu (jamaa) akuilimbikitsa zedi ngakhale kuti anthu ali pakati pa nkhondo. Ngati nthawi ya Swala yakwana akuwauza kuti apemphere pagulu, koma asapemphere onse nthawi imodzi. Anthuwo agawike m’magulu awiri. Gulu lina liyang’ane komwe kuli adani, ndipo gulu lina likhale likupemphera pamodzi ndi (Imamu) mtsogoleri wawo. Komatu Swala akunkhondo amaswali raka ziwiriziwiri (Swala iliyonse) kupatula Swala ya Magharibi. Tsono Imamu adzapemphera raka imodzi ndi awo omwe akupemphera nawo. Akaimilira kuti apemphere raka yachiwiri, aja omwe anali kupemphera naye aimilire ndi kupemphera raka yotsalayo mwachangu atamsiya imamu ali chiimilire. Ndipo apite kukalowa m’malo mwa anzawo omwe anali kuyang’ana komwe kuli adani. Tsono anzawowo adze nkudzapemphera ndi Imamu. Imamu akamaliza raka yake yachiwiri, iwo aimilire nkumaliza raka yawo yachiwiri. Komatu popempherapo zida zawo zikhale atazikoleka m’matupi mwawo pokhapokha ngati pali zifukwa zoikitsa zidazo pansi, zomwe azitchula kumapeto a ndimeyo
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (102) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق