ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (82) سورة: النساء
أَفَلَا يَتَدَبَّرُونَ ٱلۡقُرۡءَانَۚ وَلَوۡ كَانَ مِنۡ عِندِ غَيۡرِ ٱللَّهِ لَوَجَدُواْ فِيهِ ٱخۡتِلَٰفٗا كَثِيرٗا
Kodi bwanji sakuilingalira Qur’an? Ndipo ikadakhala kuti siikuchokera kwa Allah, ndithudi, mmenemo akadapeza kusiyana kwambiri.[134]
[134] M’ndime iyi akuti Qur’an iyi mawu ake ngolingana. Siotsutsana ayi. Ndipo palibe amene angabweretse mtsutso wakuti mawu ena omwe ali m’bukuli ngabodza pa chifukwa chakutichakuti. Palibe buku lomwe munthu adalemba lomwe lidabweretsa mtsutso weniweni wakuti Qur’an simawu a Allah pachifukwa chakutichakuti. Ndipo silidzapezeka buku lotero mpaka dziko lapansi lidzatha. Koma mwina anthu akhoza kumayankhula chabe popanda kubwera ndi mtsutso weniweni wokhala ndi umboni wooneka. Kuona kwa Qur’an kwatsimikizika pa zinthu izi:- Qur’an idafotokoza nkhani zakale zomwe zidachitika Mtumiki Muhammad (s.a.w) asanabadwe pomwe iye sankadziwa kulemba ndi kuwerenga mabuku. Quran idafotokozanso zamtsogolo. Ndipo zina mwa izo zaonekera kale poyera: Qur’an idati: (1) “Chinthu chilichonse pali chachimuna ndi chachikazi”. Yang’anani ndime ya 36 ya Sûrat Yasin. (2) Kuti dziko lapansili lidalumikizana ndi kumwamba monga ikufotokozera Sûrat Anbiyaa ndime ya 30. (3) Kuti moyo umadalira madzi, monga momwe ndime ya 30 ya m’Sûrat Anbiyaa ikulongosolera. (4) Kuti anthu amene ali kutali kwambiri adzatha kumva zimene anthu ena akutali akunena. Monga momwe yafotokozera ndime ya 44 ya m’Sûrat Aaraf. (5) Ndi kuti anthu adzakwera kumwamba monga momwe ikulongosolera ndime ya 13 ya m’Sûrat Jathiya. Mu Qur’an muli zambiri zimene adafotokoza kuti zidzachitika mtsogolo. Ndipo zambiri mwa izo zachitikadi, anthu aziona. Ndipo zonsezi zikutsimikizira kuti Qur’an ndi mawu a Allah.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (82) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق