ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (158) سورة: الأنعام
هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّآ أَن تَأۡتِيَهُمُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ أَوۡ يَأۡتِيَ رَبُّكَ أَوۡ يَأۡتِيَ بَعۡضُ ءَايَٰتِ رَبِّكَۗ يَوۡمَ يَأۡتِي بَعۡضُ ءَايَٰتِ رَبِّكَ لَا يَنفَعُ نَفۡسًا إِيمَٰنُهَا لَمۡ تَكُنۡ ءَامَنَتۡ مِن قَبۡلُ أَوۡ كَسَبَتۡ فِيٓ إِيمَٰنِهَا خَيۡرٗاۗ قُلِ ٱنتَظِرُوٓاْ إِنَّا مُنتَظِرُونَ
Kodi chilipo chimene akudikira kuposa kuwadzera angelo (kudzawachotsa miyoyo yawo?) Kapena kudza Mbuye wako (tsiku la Qiyâma kuzaweruza)? Kapena kudza zina mwa zizindikiro za Mbuye wako (zomwe adati zidzadza)? Tsiku lakudza zina mwa zizindikiro za Mbuye wako, munthu (wosakhulupirira) chikhulupiliro chake (panthawiyo) sichidzamthandiza, yemwe sadakhulupirirepo kale, kapena (msilamu) yemwe sanapindule nacho chikhulupiliro chake. Nena: “Dikirani. Nafenso tikudikira.”[175]
[175] Chisilamu kuti chikamthandize munthu nkofunika kuti achigwiritsire ntchito pa moyo wake wonse. Chisilamu chokha popanda kuchigwiritsira ntchito sichikwanira ndiponso sichingamtchinjirize munthu kuchilango cha Moto. Ndipo yemwe sali msilamu kuti Chisilamu chikamthandize nkofunika kuti alowe m’Chisilamu ali ndi moyo, osati pamene imfa yamufika. Ndipo nayenso msilamu wochita zoipa, akalapa imfa itamufika kale kulapa kwakeko sikungamthandize. Koma alape pamene ali ndi moyo wangwiro. Pamenepo ndiye kuti Allah alandira kulapa kwake. Osati kulapa uku imfa akuiona ndi maso ake.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (158) سورة: الأنعام
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق