ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (91) سورة: الأنعام
وَمَا قَدَرُواْ ٱللَّهَ حَقَّ قَدۡرِهِۦٓ إِذۡ قَالُواْ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ عَلَىٰ بَشَرٖ مِّن شَيۡءٖۗ قُلۡ مَنۡ أَنزَلَ ٱلۡكِتَٰبَ ٱلَّذِي جَآءَ بِهِۦ مُوسَىٰ نُورٗا وَهُدٗى لِّلنَّاسِۖ تَجۡعَلُونَهُۥ قَرَاطِيسَ تُبۡدُونَهَا وَتُخۡفُونَ كَثِيرٗاۖ وَعُلِّمۡتُم مَّا لَمۡ تَعۡلَمُوٓاْ أَنتُمۡ وَلَآ ءَابَآؤُكُمۡۖ قُلِ ٱللَّهُۖ ثُمَّ ذَرۡهُمۡ فِي خَوۡضِهِمۡ يَلۡعَبُونَ
Koma (Ayuda) sadamulemekeze Allah monga momwe zikufunikira pomulemekeza pomwe adati: “Allah Sadavumbulutsepo chilichonse kwa munthu aliyense.” (Adanena izi pamene mtumiki adawauza kuti Qur’an ndi buku lomwe Allah wavumbulutsa). Nena: “Kodi ndani adavumbulutsa buku lomwe lidadza ndi Mûsa? Lomwe lidali kuunika ndi chiwongoko kwa anthu, lomwe mwalipanga kukhala magawo-magawo; zimene mwafuna kuonetsa kwa anthu mukuzionetsa. Koma zambiri mukubisa (zomwe sizigwirizana ndi zofuna zanu). Ndipo mwaphunzitsidwa (ndi iyi Qur’an) zomwe simudali kuzidziwa, inu ngakhale makolo anu. Nena: “Allah (ndi Yemwe wavumbulutsa iyi Qur’an ndi mabuku ena.”) Kenako asiye azingosewera m’kubwebweta kwawo (kopanda pake).
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (91) سورة: الأنعام
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق