Check out the new design

আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আল-বাক্বাৰাহ   আয়াত:

Al-Baqarah

الٓمٓ
Alif-Lâm-Mîm.[1]
[1] Sura iyi yayamba ndi malembo a Alifabeti, monga Alif, Laam, Miim. kusonyeza kuti Qur’an yalembedwa ndi malembo amenewa omwe anthu amawagwiritsa ntchito m’zoyankhula ndi m’zolembalemba zawo. Uku ndikuwauza osakhulupilira kuti abweretse buku lawo lolembedwa ndi malembo omwe akuwadziwawo pamene iwo amanena kuti Qur’an adangoipeka yekha Muhammadi (s.a.w) siidavumbulutsidwe ndi Allah. Choncho Allah adawachalenja kuti alembe buku lawo lofanana ndi Qur’an, koma adalephera. Choncho, kulephera kwawo ndi umboni wosonyeza kuti Qur’an ndi buku lovumbulutsidwa ndi Allah.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ذَٰلِكَ ٱلۡكِتَٰبُ لَا رَيۡبَۛ فِيهِۛ هُدٗى لِّلۡمُتَّقِينَ
Ili ndi Buku lopanda chipeneko mkati mwake, ndichiongoko cha (anthu) oopa Allah.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡغَيۡبِ وَيُقِيمُونَ ٱلصَّلَوٰةَ وَمِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ يُنفِقُونَ
Omwe amakhulupirira zosaoneka ndi maso (monga Munda wamtendere, Moto, Angelo ndi zina zotere zomwe Allah ndi Mtumiki (s.a.w) adazifotokoza, amapemphera Swala moyenera, ndiponso amapereka m’zimene tawapatsa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ وَمَآ أُنزِلَ مِن قَبۡلِكَ وَبِٱلۡأٓخِرَةِ هُمۡ يُوقِنُونَ
Ndi amene akukhulupirira zomwe zidavumbulutsidwa kwa iwe, ndi zomwe zidavumbulutsidwa kale iwe usadadze, nakhulupiriranso motsimikiza kuti lilipo tsiku lachimaliziro.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أُوْلَٰٓئِكَ عَلَىٰ هُدٗى مِّن رَّبِّهِمۡۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Iwowo (omwe ali ndi chikhalidwe chotere), ali pachiongoko chochokera kwa Mbuye wawo (Allah), ndipo iwowo ndi omwe ali opambana (pokapeza ulemelero wapamwamba ku Minda ya mtendere).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আল-বাক্বাৰাহ
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

ইয়াক অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহিম বিতালা।

বন্ধ