Check out the new design

আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আলে ইমৰাণ   আয়াত:
وَكَيۡفَ تَكۡفُرُونَ وَأَنتُمۡ تُتۡلَىٰ عَلَيۡكُمۡ ءَايَٰتُ ٱللَّهِ وَفِيكُمۡ رَسُولُهُۥۗ وَمَن يَعۡتَصِم بِٱللَّهِ فَقَدۡ هُدِيَ إِلَىٰ صِرَٰطٖ مُّسۡتَقِيمٖ
Kodi mukukanira bwanji pomwe ndime za Allah zikuwerengedwa kwa inu, pomwenso Mtumiki Wake ali pamodzi nanu? Ndipo amene agwiritse mwa Allah (bwinobwino), ndithudi iye wawongoleredwa kunjira yoongoka.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ حَقَّ تُقَاتِهِۦ وَلَا تَمُوتُنَّ إِلَّا وَأَنتُم مُّسۡلِمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah; kuopa kwenikweni. Ndipo musafe pokhapokha mutakhala Asilamu (ogonjera).[76]
[76] Pa ndime iyi akulangiza kuti nthawi iliyonse munthu akhale m’chikhalidwe cha Chisilamu chokwanira popewa zoletsedwa ndi kumachita zimene alamulidwa kuchita mmene angathere, chifukwa chakuti munthu sangadziwe nthawi imene imfa ingamufikire.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱعۡتَصِمُواْ بِحَبۡلِ ٱللَّهِ جَمِيعٗا وَلَا تَفَرَّقُواْۚ وَٱذۡكُرُواْ نِعۡمَتَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ إِذۡ كُنتُمۡ أَعۡدَآءٗ فَأَلَّفَ بَيۡنَ قُلُوبِكُمۡ فَأَصۡبَحۡتُم بِنِعۡمَتِهِۦٓ إِخۡوَٰنٗا وَكُنتُمۡ عَلَىٰ شَفَا حُفۡرَةٖ مِّنَ ٱلنَّارِ فَأَنقَذَكُم مِّنۡهَاۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ لَكُمۡ ءَايَٰتِهِۦ لَعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Ndipo gwiritsani chingwe (chipembedzo) cha Allah nonsenu, ndipo musagawikane. Kumbukirani mtendere wa Allah womwe uli pa inu; pamene mudali odana ndipo Iye adalunzanitsa pakati pa mitima yanu, tero mwa mtendere Wake mudakhala abale; ndipo mudali m’mphepete mwa dzenje la moto (wa Jahanama), ndipo Iye adakupulumutsanimo. Umo ndi momwe Allah akukufotokozerani ma Ayah Ake (ndime Zake) kuti muongoke.[77]
[77] Ndime izi zikuwauza Asilamu onse kuti akhale ogwirizana pamodzi m’dzina lachipembedzo chawo cha Chisilamu. Asapatukane popatsana maina atsopano kapena kuti awa akuchokera ku dziko lakutilakuti, awa ngamtundu wakutiwakuti. Kuchita zimenezo nkulakwa kwambiri. Koma pakati pa Asilamu pakhale chimvano.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَلۡتَكُن مِّنكُمۡ أُمَّةٞ يَدۡعُونَ إِلَى ٱلۡخَيۡرِ وَيَأۡمُرُونَ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلۡمُنكَرِۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Ndipo mwa inu lipezeke gulu la anthu oitanira ku zabwino (Chisilamu) ndipo alamule (kuchita) zabwino ndikuletsa zoipa. Iwo ndiwo opambana.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَلَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ تَفَرَّقُواْ وَٱخۡتَلَفُواْ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ عَذَابٌ عَظِيمٞ
Ndipo musakhale monga aja amene adagawikana nasiyana pambuyo powadzera zisonyezo zoonekera poyera (zowaletsa kutero). Ndipo iwo adzakhala ndichilango chachikulu.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
يَوۡمَ تَبۡيَضُّ وُجُوهٞ وَتَسۡوَدُّ وُجُوهٞۚ فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ٱسۡوَدَّتۡ وُجُوهُهُمۡ أَكَفَرۡتُم بَعۡدَ إِيمَٰنِكُمۡ فَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَ بِمَا كُنتُمۡ تَكۡفُرُونَ
Patsikulo nkhope zina zidzakhala zowala pomwe nkhope zina zidzakhala zakuda. Tsono amene nkhope zawo zidzakhala zakuda, (adzauzidwa): “Kodi mudakana ( Allah) pambuyo pa chikhulupiliro chanu? Choncho, lawani chilango (chopweteka) chifukwa cha zomwe mudali kuzikana.”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَمَّا ٱلَّذِينَ ٱبۡيَضَّتۡ وُجُوهُهُمۡ فَفِي رَحۡمَةِ ٱللَّهِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Tsono (anthu odala) omwe nkhope zawo zidzawale, adzakhala m’chifundo cha Allah. Iwo mmenemo adzakhala nthawi yaitali.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱللَّهِ نَتۡلُوهَا عَلَيۡكَ بِٱلۡحَقِّۗ وَمَا ٱللَّهُ يُرِيدُ ظُلۡمٗا لِّلۡعَٰلَمِينَ
Awo ndi ma Ayah (ndime) a Allah; tikukuwerengera mwa choonadi. Ndipo Allah safuna kupondereza zolengedwa (Zake).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আলে ইমৰাণ
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

ইয়াক অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহিম বিতালা।

বন্ধ