Check out the new design

Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: əs-Saffat   Ayə:
وَجَعَلۡنَا ذُرِّيَّتَهُۥ هُمُ ٱلۡبَاقِينَ
Ndipo tidazichita zidzukulu zake kukhala zotsala (pa dziko, oipa ataonongeka).
Ərəbcə təfsirlər:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira mbiri yabwino kwa mibadwo yodza pambuyo pake.
Ərəbcə təfsirlər:
سَلَٰمٌ عَلَىٰ نُوحٖ فِي ٱلۡعَٰلَمِينَ
Mtendere ukhale pa Nuh pa zolengedwa zonse.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umu ndimomwe Ife tilipirira ochita zabwino.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye ndi mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
Ərəbcə təfsirlər:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo.
Ərəbcə təfsirlər:
۞ وَإِنَّ مِن شِيعَتِهِۦ لَإِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo ndithu m’gulu lake (la Nuh) muli Ibrahim.
Ərəbcə təfsirlər:
إِذۡ جَآءَ رَبَّهُۥ بِقَلۡبٖ سَلِيمٍ
Kumbuka pamene adadza kwa Mbuye wake ndi mtima wabwino (wogonjera malamulo).
Ərəbcə təfsirlər:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَاذَا تَعۡبُدُونَ
Pomwe adanena kwa bambo wake ndi anthu ake: “Mukupembedza chiyani?”
Ərəbcə təfsirlər:
أَئِفۡكًا ءَالِهَةٗ دُونَ ٱللَّهِ تُرِيدُونَ
“Ha! Milungu yopeka kusiya Allah, ndi imene mukuifuna?”
Ərəbcə təfsirlər:
فَمَا ظَنُّكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi maganizo anu ngotani pa Mbuye wa zolengedwa zonse?”
Ərəbcə təfsirlər:
فَنَظَرَ نَظۡرَةٗ فِي ٱلنُّجُومِ
Ndipo adayang’ana nyenyezi mozama.
Ərəbcə təfsirlər:
فَقَالَ إِنِّي سَقِيمٞ
Ndipo adanena: “Ine ndine wodwala!”
Ərəbcə təfsirlər:
فَتَوَلَّوۡاْ عَنۡهُ مُدۡبِرِينَ
Choncho iwo adatembenuka ndi kumsiya.
Ərəbcə təfsirlər:
فَرَاغَ إِلَىٰٓ ءَالِهَتِهِمۡ فَقَالَ أَلَا تَأۡكُلُونَ
(Ibrahim) adapita mozemba ku mafano awo, ndipo adawauza (mwachipongwe:) “Bwanji simukudya (chakudya chomwe chaikidwa patsogolo panupo)?”
Ərəbcə təfsirlər:
مَا لَكُمۡ لَا تَنطِقُونَ
“Bwanji simukuyankhula?”
Ərəbcə təfsirlər:
فَرَاغَ عَلَيۡهِمۡ ضَرۡبَۢا بِٱلۡيَمِينِ
Atatero adawatembenukira ndi kuwamenya (mwamphamvu) ndi dzanja lamanja.
Ərəbcə təfsirlər:
فَأَقۡبَلُوٓاْ إِلَيۡهِ يَزِفُّونَ
(Pamene adamva eni mafanowo) adadza kwa iye akuthamanga.
Ərəbcə təfsirlər:
قَالَ أَتَعۡبُدُونَ مَا تَنۡحِتُونَ
Anati: “Kodi mukupembedza (miyala) imene mwasema?”
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱللَّهُ خَلَقَكُمۡ وَمَا تَعۡمَلُونَ
“Chikhalirecho Allah ndiye adakulengani ndi zimene mukuchita!”
Ərəbcə təfsirlər:
قَالُواْ ٱبۡنُواْ لَهُۥ بُنۡيَٰنٗا فَأَلۡقُوهُ فِي ٱلۡجَحِيمِ
Iwo adati: “Mmangireni ng’anjo, ndipo mponyeni m’motowo.”
Ərəbcə təfsirlər:
فَأَرَادُواْ بِهِۦ كَيۡدٗا فَجَعَلۡنَٰهُمُ ٱلۡأَسۡفَلِينَ
Adafuna kumchita chiwembu (kuti amuphe ndi moto), koma tidawachita kukhala onyozeka.
Ərəbcə təfsirlər:
وَقَالَ إِنِّي ذَاهِبٌ إِلَىٰ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
Ndipo (Ibrahim) adati: “Ndithu ine ndikupita kwa Mbuye wanga, Iye andiongolera.”
Ərəbcə təfsirlər:
رَبِّ هَبۡ لِي مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni mwana yemwe adzakhale (mmodzi) mwa olungama!”
Ərəbcə təfsirlər:
فَبَشَّرۡنَٰهُ بِغُلَٰمٍ حَلِيمٖ
Ndipo tidamuuza nkhani yabwino ya mwana wofatsa, (mwanayo ndi Ismaila).
Ərəbcə təfsirlər:
فَلَمَّا بَلَغَ مَعَهُ ٱلسَّعۡيَ قَالَ يَٰبُنَيَّ إِنِّيٓ أَرَىٰ فِي ٱلۡمَنَامِ أَنِّيٓ أَذۡبَحُكَ فَٱنظُرۡ مَاذَا تَرَىٰۚ قَالَ يَٰٓأَبَتِ ٱفۡعَلۡ مَا تُؤۡمَرُۖ سَتَجِدُنِيٓ إِن شَآءَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلصَّٰبِرِينَ
Ndipo (adabadwa ndi kuyamba kukula.) Pamene adakwana nsinkhu woyenda pamodzi ndi tate wake pochitachita za m’dziko (Ibrahim adayesedwa mayeso kupyolera m’maloto omwe adalota). Adati: “E mwana wanga! Ine kutulo ndikuona maloto (owona ochokera kwa Allah omwe akundilamula) kuti ndikuzinge (monga nsembe yopereka kwa Allah). Nanga ukuti bwanji?” (Mwana wabwino) adanena: “Bambo wanga! Kwaniritsani chimene mukulamulidwa. Ngati Allah afuna, mundipeza ndili mmodzi mwa opirira.”
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: əs-Saffat
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. - Tərcumənin mündəricatı

Khalid İbrahim Beytala tərəfindən tərcümə.

Bağlamaq