Check out the new design

আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আচ-চা-ফফা-ত   আয়াত:
وَجَعَلۡنَا ذُرِّيَّتَهُۥ هُمُ ٱلۡبَاقِينَ
Ndipo tidazichita zidzukulu zake kukhala zotsala (pa dziko, oipa ataonongeka).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira mbiri yabwino kwa mibadwo yodza pambuyo pake.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
سَلَٰمٌ عَلَىٰ نُوحٖ فِي ٱلۡعَٰلَمِينَ
Mtendere ukhale pa Nuh pa zolengedwa zonse.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umu ndimomwe Ife tilipirira ochita zabwino.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye ndi mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
۞ وَإِنَّ مِن شِيعَتِهِۦ لَإِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo ndithu m’gulu lake (la Nuh) muli Ibrahim.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِذۡ جَآءَ رَبَّهُۥ بِقَلۡبٖ سَلِيمٍ
Kumbuka pamene adadza kwa Mbuye wake ndi mtima wabwino (wogonjera malamulo).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَاذَا تَعۡبُدُونَ
Pomwe adanena kwa bambo wake ndi anthu ake: “Mukupembedza chiyani?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَئِفۡكًا ءَالِهَةٗ دُونَ ٱللَّهِ تُرِيدُونَ
“Ha! Milungu yopeka kusiya Allah, ndi imene mukuifuna?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَمَا ظَنُّكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi maganizo anu ngotani pa Mbuye wa zolengedwa zonse?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَنَظَرَ نَظۡرَةٗ فِي ٱلنُّجُومِ
Ndipo adayang’ana nyenyezi mozama.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَقَالَ إِنِّي سَقِيمٞ
Ndipo adanena: “Ine ndine wodwala!”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَتَوَلَّوۡاْ عَنۡهُ مُدۡبِرِينَ
Choncho iwo adatembenuka ndi kumsiya.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَرَاغَ إِلَىٰٓ ءَالِهَتِهِمۡ فَقَالَ أَلَا تَأۡكُلُونَ
(Ibrahim) adapita mozemba ku mafano awo, ndipo adawauza (mwachipongwe:) “Bwanji simukudya (chakudya chomwe chaikidwa patsogolo panupo)?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
مَا لَكُمۡ لَا تَنطِقُونَ
“Bwanji simukuyankhula?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَرَاغَ عَلَيۡهِمۡ ضَرۡبَۢا بِٱلۡيَمِينِ
Atatero adawatembenukira ndi kuwamenya (mwamphamvu) ndi dzanja lamanja.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَأَقۡبَلُوٓاْ إِلَيۡهِ يَزِفُّونَ
(Pamene adamva eni mafanowo) adadza kwa iye akuthamanga.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
قَالَ أَتَعۡبُدُونَ مَا تَنۡحِتُونَ
Anati: “Kodi mukupembedza (miyala) imene mwasema?”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱللَّهُ خَلَقَكُمۡ وَمَا تَعۡمَلُونَ
“Chikhalirecho Allah ndiye adakulengani ndi zimene mukuchita!”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
قَالُواْ ٱبۡنُواْ لَهُۥ بُنۡيَٰنٗا فَأَلۡقُوهُ فِي ٱلۡجَحِيمِ
Iwo adati: “Mmangireni ng’anjo, ndipo mponyeni m’motowo.”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَأَرَادُواْ بِهِۦ كَيۡدٗا فَجَعَلۡنَٰهُمُ ٱلۡأَسۡفَلِينَ
Adafuna kumchita chiwembu (kuti amuphe ndi moto), koma tidawachita kukhala onyozeka.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَقَالَ إِنِّي ذَاهِبٌ إِلَىٰ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
Ndipo (Ibrahim) adati: “Ndithu ine ndikupita kwa Mbuye wanga, Iye andiongolera.”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
رَبِّ هَبۡ لِي مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni mwana yemwe adzakhale (mmodzi) mwa olungama!”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَبَشَّرۡنَٰهُ بِغُلَٰمٍ حَلِيمٖ
Ndipo tidamuuza nkhani yabwino ya mwana wofatsa, (mwanayo ndi Ismaila).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَلَمَّا بَلَغَ مَعَهُ ٱلسَّعۡيَ قَالَ يَٰبُنَيَّ إِنِّيٓ أَرَىٰ فِي ٱلۡمَنَامِ أَنِّيٓ أَذۡبَحُكَ فَٱنظُرۡ مَاذَا تَرَىٰۚ قَالَ يَٰٓأَبَتِ ٱفۡعَلۡ مَا تُؤۡمَرُۖ سَتَجِدُنِيٓ إِن شَآءَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلصَّٰبِرِينَ
Ndipo (adabadwa ndi kuyamba kukula.) Pamene adakwana nsinkhu woyenda pamodzi ndi tate wake pochitachita za m’dziko (Ibrahim adayesedwa mayeso kupyolera m’maloto omwe adalota). Adati: “E mwana wanga! Ine kutulo ndikuona maloto (owona ochokera kwa Allah omwe akundilamula) kuti ndikuzinge (monga nsembe yopereka kwa Allah). Nanga ukuti bwanji?” (Mwana wabwino) adanena: “Bambo wanga! Kwaniritsani chimene mukulamulidwa. Ngati Allah afuna, mundipeza ndili mmodzi mwa opirira.”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: আচ-চা-ফফা-ত
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

ইয়াক অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহিম বিতালা।

বন্ধ