Check out the new design

Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: əz-Zumər   Ayə:
قُلۡ إِنِّيٓ أُمِرۡتُ أَنۡ أَعۡبُدَ ٱللَّهَ مُخۡلِصٗا لَّهُ ٱلدِّينَ
Nena: “Ine ndalamulidwa kuti ndimpembedze Allah momuyeretsera mapemphero Ake (posamphatikiza ndi aliyense pa mapemphero, kapena kupemphera mwa chiphamaso).”
Ərəbcə təfsirlər:
وَأُمِرۡتُ لِأَنۡ أَكُونَ أَوَّلَ ٱلۡمُسۡلِمِينَ
“Ndalamulidwanso kuti ndikhale woyamba mwa ogonjera (malamulo Ake).”
Ərəbcə təfsirlər:
قُلۡ إِنِّيٓ أَخَافُ إِنۡ عَصَيۡتُ رَبِّي عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
Nena: “Ine ndikuopa chilango cha tsiku lalikulu, (loopsa), ngati ndinyoza Mbuye wanga.”
Ərəbcə təfsirlər:
قُلِ ٱللَّهَ أَعۡبُدُ مُخۡلِصٗا لَّهُۥ دِينِي
Nena (kwa iwo, iwe Mneneri {s.a.w}): “Ndi Allah Yekha ndikumpembedza pomuyeretsera Iye mapemphero anga.”
Ərəbcə təfsirlər:
فَٱعۡبُدُواْ مَا شِئۡتُم مِّن دُونِهِۦۗ قُلۡ إِنَّ ٱلۡخَٰسِرِينَ ٱلَّذِينَ خَسِرُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ وَأَهۡلِيهِمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۗ أَلَا ذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡخُسۡرَانُ ٱلۡمُبِينُ
“Choncho pembedzani zimene mwafuna, kumsiya Iye.” Nena (kwa iwo): “Ndithu otaika ndi kuonongeka kwakukulu, ndi amene adzitaya okha, (adziluzitsa okha), ndi maanja awo, patsiku la Qiyâma. Dziwa, ndithu kumeneko ndiko kuluza koonekera.”
Ərəbcə təfsirlər:
لَهُم مِّن فَوۡقِهِمۡ ظُلَلٞ مِّنَ ٱلنَّارِ وَمِن تَحۡتِهِمۡ ظُلَلٞۚ ذَٰلِكَ يُخَوِّفُ ٱللَّهُ بِهِۦ عِبَادَهُۥۚ يَٰعِبَادِ فَٱتَّقُونِ
Pa iwo padzakhala misanjikosanjiko ya moto ndiponso pansi pawo. Ndi (chilango) chimenechi, Allah akuwaopseza nacho akapolo Ake. “E inu akapolo Anga! Ndiopeni!”
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱلَّذِينَ ٱجۡتَنَبُواْ ٱلطَّٰغُوتَ أَن يَعۡبُدُوهَا وَأَنَابُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِ لَهُمُ ٱلۡبُشۡرَىٰۚ فَبَشِّرۡ عِبَادِ
Ndipo amene apatukana nawo mafano ndi satana posiya kuzipembedza, ndikusiya kuziyandikira, ndipo mmalo mwake nkutembenukira kwa Allah (pa zochita zawo zonse), nkhani yabwino njawo (ponseponse). Auze nkhani yabwino akapolo Anga.
Ərəbcə təfsirlər:
ٱلَّذِينَ يَسۡتَمِعُونَ ٱلۡقَوۡلَ فَيَتَّبِعُونَ أَحۡسَنَهُۥٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ هَدَىٰهُمُ ٱللَّهُۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمۡ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Amene akumvetsera mawu ndi kutsatira amene ali abwino kwambiri. Iwowo ndi amene Allah wawaongola. Ndipo iwowo ndiwo eni nzeru.
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَمَنۡ حَقَّ عَلَيۡهِ كَلِمَةُ ٱلۡعَذَابِ أَفَأَنتَ تُنقِذُ مَن فِي ٱلنَّارِ
Kodi yemwe chiweruzo cha chilango chatsimikizika pa iye, (mungamteteze)? Kodi iwe ungampulumutse yemwe ali m’Moto?
Ərəbcə təfsirlər:
لَٰكِنِ ٱلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْ رَبَّهُمۡ لَهُمۡ غُرَفٞ مِّن فَوۡقِهَا غُرَفٞ مَّبۡنِيَّةٞ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُۖ وَعۡدَ ٱللَّهِ لَا يُخۡلِفُ ٱللَّهُ ٱلۡمِيعَادَ
Koma amene aopa Mbuye wawo, iwo adzakhala nazo Nyumba zikuluzikulu zimene zamangidwa mosanjikizana, mitsinje ikuyenda pansi pake. Ili ndi lonjezo lochokera kwa Allah. Allah saphwanya lonjezo.
Ərəbcə təfsirlər:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَسَلَكَهُۥ يَنَٰبِيعَ فِي ٱلۡأَرۡضِ ثُمَّ يُخۡرِجُ بِهِۦ زَرۡعٗا مُّخۡتَلِفًا أَلۡوَٰنُهُۥ ثُمَّ يَهِيجُ فَتَرَىٰهُ مُصۡفَرّٗا ثُمَّ يَجۡعَلُهُۥ حُطَٰمًاۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَذِكۡرَىٰ لِأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Kodi suona kuti Allah amatsitsa madzi kuchokera kumwamba, ndipo amawalowetsa mu akasupe mkati mwa nthaka, kenako amatulutsa ndi madziwo mbewu zosiyana mitundu: (chimanga, mpunga, tirigu, ndi zina zotere). Ndipo kenako zimauma (pambuyo pokhala zobiriwira); umaziona zili zachikasu. Kenako amazichita kukhala zidutswazidutswa? Ndithu muzimenezo muli chikumbutso kwa eni nzeru (zofufuzira zinthu).
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: əz-Zumər
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. - Tərcumənin mündəricatı

Khalid İbrahim Beytala tərəfindən tərcümə.

Bağlamaq