Check out the new design

Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Az-Zomar   Vers:
قُلۡ إِنِّيٓ أُمِرۡتُ أَنۡ أَعۡبُدَ ٱللَّهَ مُخۡلِصٗا لَّهُ ٱلدِّينَ
Nena: “Ine ndalamulidwa kuti ndimpembedze Allah momuyeretsera mapemphero Ake (posamphatikiza ndi aliyense pa mapemphero, kapena kupemphera mwa chiphamaso).”
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأُمِرۡتُ لِأَنۡ أَكُونَ أَوَّلَ ٱلۡمُسۡلِمِينَ
“Ndalamulidwanso kuti ndikhale woyamba mwa ogonjera (malamulo Ake).”
Arabische uitleg van de Qur'an:
قُلۡ إِنِّيٓ أَخَافُ إِنۡ عَصَيۡتُ رَبِّي عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
Nena: “Ine ndikuopa chilango cha tsiku lalikulu, (loopsa), ngati ndinyoza Mbuye wanga.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
قُلِ ٱللَّهَ أَعۡبُدُ مُخۡلِصٗا لَّهُۥ دِينِي
Nena (kwa iwo, iwe Mneneri {s.a.w}): “Ndi Allah Yekha ndikumpembedza pomuyeretsera Iye mapemphero anga.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَٱعۡبُدُواْ مَا شِئۡتُم مِّن دُونِهِۦۗ قُلۡ إِنَّ ٱلۡخَٰسِرِينَ ٱلَّذِينَ خَسِرُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ وَأَهۡلِيهِمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۗ أَلَا ذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡخُسۡرَانُ ٱلۡمُبِينُ
“Choncho pembedzani zimene mwafuna, kumsiya Iye.” Nena (kwa iwo): “Ndithu otaika ndi kuonongeka kwakukulu, ndi amene adzitaya okha, (adziluzitsa okha), ndi maanja awo, patsiku la Qiyâma. Dziwa, ndithu kumeneko ndiko kuluza koonekera.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَهُم مِّن فَوۡقِهِمۡ ظُلَلٞ مِّنَ ٱلنَّارِ وَمِن تَحۡتِهِمۡ ظُلَلٞۚ ذَٰلِكَ يُخَوِّفُ ٱللَّهُ بِهِۦ عِبَادَهُۥۚ يَٰعِبَادِ فَٱتَّقُونِ
Pa iwo padzakhala misanjikosanjiko ya moto ndiponso pansi pawo. Ndi (chilango) chimenechi, Allah akuwaopseza nacho akapolo Ake. “E inu akapolo Anga! Ndiopeni!”
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ ٱجۡتَنَبُواْ ٱلطَّٰغُوتَ أَن يَعۡبُدُوهَا وَأَنَابُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِ لَهُمُ ٱلۡبُشۡرَىٰۚ فَبَشِّرۡ عِبَادِ
Ndipo amene apatukana nawo mafano ndi satana posiya kuzipembedza, ndikusiya kuziyandikira, ndipo mmalo mwake nkutembenukira kwa Allah (pa zochita zawo zonse), nkhani yabwino njawo (ponseponse). Auze nkhani yabwino akapolo Anga.
Arabische uitleg van de Qur'an:
ٱلَّذِينَ يَسۡتَمِعُونَ ٱلۡقَوۡلَ فَيَتَّبِعُونَ أَحۡسَنَهُۥٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ هَدَىٰهُمُ ٱللَّهُۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمۡ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Amene akumvetsera mawu ndi kutsatira amene ali abwino kwambiri. Iwowo ndi amene Allah wawaongola. Ndipo iwowo ndiwo eni nzeru.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَفَمَنۡ حَقَّ عَلَيۡهِ كَلِمَةُ ٱلۡعَذَابِ أَفَأَنتَ تُنقِذُ مَن فِي ٱلنَّارِ
Kodi yemwe chiweruzo cha chilango chatsimikizika pa iye, (mungamteteze)? Kodi iwe ungampulumutse yemwe ali m’Moto?
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَٰكِنِ ٱلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْ رَبَّهُمۡ لَهُمۡ غُرَفٞ مِّن فَوۡقِهَا غُرَفٞ مَّبۡنِيَّةٞ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُۖ وَعۡدَ ٱللَّهِ لَا يُخۡلِفُ ٱللَّهُ ٱلۡمِيعَادَ
Koma amene aopa Mbuye wawo, iwo adzakhala nazo Nyumba zikuluzikulu zimene zamangidwa mosanjikizana, mitsinje ikuyenda pansi pake. Ili ndi lonjezo lochokera kwa Allah. Allah saphwanya lonjezo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَسَلَكَهُۥ يَنَٰبِيعَ فِي ٱلۡأَرۡضِ ثُمَّ يُخۡرِجُ بِهِۦ زَرۡعٗا مُّخۡتَلِفًا أَلۡوَٰنُهُۥ ثُمَّ يَهِيجُ فَتَرَىٰهُ مُصۡفَرّٗا ثُمَّ يَجۡعَلُهُۥ حُطَٰمًاۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَذِكۡرَىٰ لِأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Kodi suona kuti Allah amatsitsa madzi kuchokera kumwamba, ndipo amawalowetsa mu akasupe mkati mwa nthaka, kenako amatulutsa ndi madziwo mbewu zosiyana mitundu: (chimanga, mpunga, tirigu, ndi zina zotere). Ndipo kenako zimauma (pambuyo pokhala zobiriwira); umaziona zili zachikasu. Kenako amazichita kukhala zidutswazidutswa? Ndithu muzimenezo muli chikumbutso kwa eni nzeru (zofufuzira zinthu).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Az-Zomar
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala - Index van vertaling

Vertaald door Khalid Ibrahim Bitala.

Sluit