Check out the new design

Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: ən-Nisa   Ayə:
ٱلَّذِينَ يَتَرَبَّصُونَ بِكُمۡ فَإِن كَانَ لَكُمۡ فَتۡحٞ مِّنَ ٱللَّهِ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَكُن مَّعَكُمۡ وَإِن كَانَ لِلۡكَٰفِرِينَ نَصِيبٞ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَسۡتَحۡوِذۡ عَلَيۡكُمۡ وَنَمۡنَعۡكُم مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ فَٱللَّهُ يَحۡكُمُ بَيۡنَكُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۚ وَلَن يَجۡعَلَ ٱللَّهُ لِلۡكَٰفِرِينَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ سَبِيلًا
(A chiphamaso) omwe akukuyembekezerani (kuti mavuto akugwereni), ngati mutapeza kupambana kochokera kwa Allah, amakuuzani: “Kodi sitidali nanu limodzi?” Koma ngati osakhulupirira atapeza gawo (lopambana), amanena (kwa osakhulupirira): “Kodi Sitidayandikire kukugonjetsani pamene tidali m’gulu lankhondo la okhulupirira koma timakutsekerezani kwa okhulupirira?” Koma Allah adzaweruza pakati panu tsiku la chiweruziro. Ndipo Allah sangawaikire njira osakhulupirira pa okhulupirira (kuti awagonjetse kotheratu).
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ يُخَٰدِعُونَ ٱللَّهَ وَهُوَ خَٰدِعُهُمۡ وَإِذَا قَامُوٓاْ إِلَى ٱلصَّلَوٰةِ قَامُواْ كُسَالَىٰ يُرَآءُونَ ٱلنَّاسَ وَلَا يَذۡكُرُونَ ٱللَّهَ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndithu achiphamaso akufuna kunyenga Allah koma Iye awalanga (chifukwa cha chinyengo chawocho). Ndipo akaimilira kupemphera Swala, amaimilira mwaulesi ndikungoonetsa anthu (kuti akupemphera). Ndipo satchula Allah koma pang’ono pokha.
Ərəbcə təfsirlər:
مُّذَبۡذَبِينَ بَيۡنَ ذَٰلِكَ لَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِ وَلَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِۚ وَمَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ سَبِيلٗا
Akungoyendayenda pakati pa awa ndi awa (pakati pa Asilamu ndi osakhulupirira). Iwo sali mbali iyi kapena mbali inayo. Ndipo amene Allah wamlekelera kuti asokere sungampezere njira yolungama.
Ərəbcə təfsirlər:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ أَتُرِيدُونَ أَن تَجۡعَلُواْ لِلَّهِ عَلَيۡكُمۡ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينًا
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite osakhulupirira kukhala abwenzi anu kusiya okhulupirira (Asilamu), kodi mukufuna kuti Allah akhale ndi umboni woonekera pa inu (kuti ndinu oyipa?)
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ فِي ٱلدَّرۡكِ ٱلۡأَسۡفَلِ مِنَ ٱلنَّارِ وَلَن تَجِدَ لَهُمۡ نَصِيرًا
Ndithu achiphamaso adzakhala pansi penipeni pa Moto; ndipo sudzampeza mthandizi woimira iwo.
Ərəbcə təfsirlər:
إِلَّا ٱلَّذِينَ تَابُواْ وَأَصۡلَحُواْ وَٱعۡتَصَمُواْ بِٱللَّهِ وَأَخۡلَصُواْ دِينَهُمۡ لِلَّهِ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَعَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۖ وَسَوۡفَ يُؤۡتِ ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Kupatula amene alapa (pambuyo pa uchiphamaso wawo); nakonza (makhalidwe awo) nadziphatika kwa Allah; namuyeretseranso Allah chipembedzo chawo. Choncho iwo ali pamodzi ndi okhulupirira. Ndipo Allah adzapatsa okhulupirira malipiro akulu.
Ərəbcə təfsirlər:
مَّا يَفۡعَلُ ٱللَّهُ بِعَذَابِكُمۡ إِن شَكَرۡتُمۡ وَءَامَنتُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ شَاكِرًا عَلِيمٗا
Allah sangakulangeni ngati mumthokoze ndi kumkhulupirira. Ndithudi, Allah Ngolandira kuthokoza kwanu, ndiponso Ngodziwa.
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: ən-Nisa
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Xalid İbrahim Bəytələ. - Tərcumənin mündəricatı

Khalid İbrahim Beytala tərəfindən tərcümə.

Bağlamaq