Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 尼萨仪   段:
ٱلَّذِينَ يَتَرَبَّصُونَ بِكُمۡ فَإِن كَانَ لَكُمۡ فَتۡحٞ مِّنَ ٱللَّهِ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَكُن مَّعَكُمۡ وَإِن كَانَ لِلۡكَٰفِرِينَ نَصِيبٞ قَالُوٓاْ أَلَمۡ نَسۡتَحۡوِذۡ عَلَيۡكُمۡ وَنَمۡنَعۡكُم مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ فَٱللَّهُ يَحۡكُمُ بَيۡنَكُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۚ وَلَن يَجۡعَلَ ٱللَّهُ لِلۡكَٰفِرِينَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ سَبِيلًا
(A chiphamaso) omwe akukuyembekezerani (kuti mavuto akugwereni), ngati mutapeza kupambana kochokera kwa Allah, amakuuzani: “Kodi sitidali nanu limodzi?” Koma ngati osakhulupirira atapeza gawo (lopambana), amanena (kwa osakhulupirira): “Kodi Sitidayandikire kukugonjetsani pamene tidali m’gulu lankhondo la okhulupirira koma timakutsekerezani kwa okhulupirira?” Koma Allah adzaweruza pakati panu tsiku la chiweruziro. Ndipo Allah sangawaikire njira osakhulupirira pa okhulupirira (kuti awagonjetse kotheratu).
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ يُخَٰدِعُونَ ٱللَّهَ وَهُوَ خَٰدِعُهُمۡ وَإِذَا قَامُوٓاْ إِلَى ٱلصَّلَوٰةِ قَامُواْ كُسَالَىٰ يُرَآءُونَ ٱلنَّاسَ وَلَا يَذۡكُرُونَ ٱللَّهَ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndithu achiphamaso akufuna kunyenga Allah koma Iye awalanga (chifukwa cha chinyengo chawocho). Ndipo akaimilira kupemphera Swala, amaimilira mwaulesi ndikungoonetsa anthu (kuti akupemphera). Ndipo satchula Allah koma pang’ono pokha.
阿拉伯语经注:
مُّذَبۡذَبِينَ بَيۡنَ ذَٰلِكَ لَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِ وَلَآ إِلَىٰ هَٰٓؤُلَآءِۚ وَمَن يُضۡلِلِ ٱللَّهُ فَلَن تَجِدَ لَهُۥ سَبِيلٗا
Akungoyendayenda pakati pa awa ndi awa (pakati pa Asilamu ndi osakhulupirira). Iwo sali mbali iyi kapena mbali inayo. Ndipo amene Allah wamlekelera kuti asokere sungampezere njira yolungama.
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُواْ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۚ أَتُرِيدُونَ أَن تَجۡعَلُواْ لِلَّهِ عَلَيۡكُمۡ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينًا
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite osakhulupirira kukhala abwenzi anu kusiya okhulupirira (Asilamu), kodi mukufuna kuti Allah akhale ndi umboni woonekera pa inu (kuti ndinu oyipa?)
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ فِي ٱلدَّرۡكِ ٱلۡأَسۡفَلِ مِنَ ٱلنَّارِ وَلَن تَجِدَ لَهُمۡ نَصِيرًا
Ndithu achiphamaso adzakhala pansi penipeni pa Moto; ndipo sudzampeza mthandizi woimira iwo.
阿拉伯语经注:
إِلَّا ٱلَّذِينَ تَابُواْ وَأَصۡلَحُواْ وَٱعۡتَصَمُواْ بِٱللَّهِ وَأَخۡلَصُواْ دِينَهُمۡ لِلَّهِ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَعَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۖ وَسَوۡفَ يُؤۡتِ ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ أَجۡرًا عَظِيمٗا
Kupatula amene alapa (pambuyo pa uchiphamaso wawo); nakonza (makhalidwe awo) nadziphatika kwa Allah; namuyeretseranso Allah chipembedzo chawo. Choncho iwo ali pamodzi ndi okhulupirira. Ndipo Allah adzapatsa okhulupirira malipiro akulu.
阿拉伯语经注:
مَّا يَفۡعَلُ ٱللَّهُ بِعَذَابِكُمۡ إِن شَكَرۡتُمۡ وَءَامَنتُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ شَاكِرًا عَلِيمٗا
Allah sangakulangeni ngati mumthokoze ndi kumkhulupirira. Ndithudi, Allah Ngolandira kuthokoza kwanu, ndiponso Ngodziwa.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭